< Isaiah 55 >

1 Anunae tui aka hal boeih loh tui taengla cet lah. A taengah tangka aka om pawt long khaw paan lah. Lai lamtah ca van. Cet lamtah misur neh suktui te tangka nen pawt akhaw a phu nen pawt akhaw lai lah.
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Buh pawt mai ah tangka na thuek thil te ba ham nim? Na thaphu khaw na daeng a cungnah hae moenih. Kamah taengkah he hnatun, hnatun lamtah a then te ca uh. Na hinglu kah maehhloi nen khaw a pang a dok bitni.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
3 Na hna duen lamtah kai taengah pongpa lah. Ya van lamtah na hinglu te hing van saeh. David kah sitlohnah aka tangnah nangmih rhoek taengah kumhal paipi ka saii ni.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Anih te namtu kah laipai rhaengsang neh namtu rhoek aka uen la ka khueh coeng he.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Namtom na ming pawt loh ng'khue vetih namtom na ming pawt khaw nang taengla ha yong uh pawn ni ke. BOEIPA na Pathen neh Israel kah a cim loh nang n'cam coeng.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
6 Amah hmuh ham koi vaengah BOEIPA toem uh. A yoei la a om vaengah amah te khue uh.
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Halang loh amah khosing, boethae hlang loh a kopoek te hnoo saeh lamtah BOEIPA taengla mael saeh. Mamih kah Pathen taengah tah khodawkngai ham a puh sak vetih, anih te a haidam bitni.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 Ka kopoek he nangmih kopoek moenih, na khosing te ka khosing moenih. BOEIPA olphong ni.
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
9 Vaan ke diklai lakah sang tih ka khosing khaw na khosing lakah sang tangloeng. Ka kopoek khaw nangmih kopoek lakah dung.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Vaan lamkah khonal neh vuelsong a suntlak phoeiah pahoi a mael moenih. Diklai te a sulpuem sak tih a cun phoeiah sul a duei sak. Te dongah lo aka tawn ham cangti neh caak ham buh a paek.
Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 Ka ol aka om tangtae ka ka lamkah aka thoeng he kai taengah kuttling la ha mael mahpawh. Ka ngaih te a saii vetih ka tueih a thaihtak sak ni.
Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Kohoenah neh na hlah uh vetih ngaimongnah neh n'khuen bitni. Tlang neh som te na mikhmuh ah tamlung neh rhong uh ni. Khohmuen kah thing boeih khaw kut a paeng uh ni.
Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
13 Tangtii yueng la hmaical khawk ding vetih sakoeih hling yueng la cuihal thing khawk ding ni. BOEIPA ham kumhal miknoek la a ming om vetih phae voel mahpawh.
Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”

< Isaiah 55 >