< Isaiah 41 >

1 Sanglak te kai hmaiah duem omuh. Namtu rhoek khaw thadueng cawn saeh lamtah ha mop uh saeh. Te vaengah, “Laitloeknah ah tun capit uh sih,” ti uh saeh.
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Khocuk lamloh aka haenghang te unim? Anih te a kho kungah duengnah la a khue. Namtom rhoek te a mikhmuh ah a tloeng pah. Manghai rhoek te a hnaa tih a cunghang neh laipi bangla a saii, a liva te divawt bangla a khoek.
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Amih loh a hloem vaengah a kho loh a cawt noek pawh caehlong te sading la a poeng.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 A lu lamloh a saii tih a khuen phoeiah cadilcahma aka khue te unim? Lamhma khaw kai Yahovah ni, a hnukkhueng taengah khaw kamah ka om.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Sanglak rhoek loh a hmuh uh tih a rhih uh. Diklai khobawt rhoek khaw a lakueng uh dongah ha tawn uh tih halo uh.
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 Hlang loh a hui te bom uh saeh lamtah a manuca te, “Thaahuel lah,” ti nah saeh.
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 Kutthai loh sui aka cilpoe te a thaphoh. Kilung neh aka picai loh thilung aka hnaa te, “Khangtui khaw khaw then ngawn,” a ti nah. A tuen pawt ham thicung neh a khing.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Tedae ka lungnah Abraham tiingan, ka sal Israel nang neh Jakob nang la kan tuek.
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 Diklai khobawt lamloh nang kan doek tih, a hlahloei lamkah ni nang kang khue. Nang te, “Ka sal ni,” ka ti dongah nang kan coelh. Te dongah nang te kan hnawt moenih.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Rhih boeh, nang taengah kamah ka om. Mangthong ngawn boeh kai he na Pathen ni. Na nam kan ning sak vetih nang kam bom ngawn bitni. Kamah kah duengnah bantang kut neh nang kan moem bitni.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Nang taengah aka lungoe boeih tah yak uh vetih a hmaithae uh ni. Namah taengah tuituknah aka khueh hlang rhoek a hong la om vetih milh uh ni.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Na rhalcak te hlang na tlap cakhaw na hmu mahpawh. Nang kah caemtloek hlang rhoek te a hong neh a poei-oep la om ni.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Kai tah na bantang kut aka moem tih nang taengah, “Rhih boeh nang te kamah loh kam bom bitni,” aka ti Yahovah na Pathen ni.
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Jakob talam, Israel hlang loh rhih boeh. Kamah loh nang kan bom bitni. Israel kah hlangcim nang aka tlan, BOEIPA kah olphong ni.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 Nang te tloep dongkah thingphael no a thai kah kungmah la kang khueh ni. Tlang na til vetih na tip sak ni. Som khaw cangkik bangla na khueh ni.
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Amih te na rhuek vaengah yilh loh a khuen vetih hlipuei loh a taekyak ni. Tedae nang tah BOEIPA dongah na omngaih vetih Israel kah a cim dongah na thangthen bitni.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Mangdaeng neh khodaeng loh tui a tlap. Tuihalh dongah a lai om kolla koh coeng. Kai Israel Pathen Yahovah loh amih te ka doo tih amih te ka hnoo moenih.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Caphoei cuk ah tuiva, kolbawn laklung ah tuisih ka phuet sak ni. Khosoek te tuibap tui la, khohmuen rhamrhae te tui hnun la ka khueh ni.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Khosoek ah lamphai, thingkoi, cuihal neh situi thing ka khueh ni. kolken ah hmaical, kungkang neh ta-aw thing khaw tun a khueh.
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 Te vaengah BOEIPA kut loh a saii tih Israel kah a cim loh a suen te hmu uh saeh lamtah ming uh saeh, dueh uh saeh lamtah tun yakming uh saeh.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 BOEIPA loh, “Nangmih kah tuituknah phoe puei uh,” a ti. Jakob manghai long tah, “Namamih kah oelhnah te tawn uh,” a ti.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Hnukbuet kah aka thoeng te mamih taengah tawn saeh lamtah thui uh saeh. Amih loh mebang a thui akhaw mamih kah lungbuei ah khueh uh sih. A hmailong ah mamih kah n'yaak bangla a thoeng te ming uh sih.
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 A hnuk ah aka lo te thui lamtah nangmih na pathen uh te kam hmat uh eh. Na thae na then khaw ka uem uh vetih ka sawt khaw ka sawt mai bitni.
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Nangmih te tangkik tanglai ni he. Na bisai khaw a hong lakah nah. Nangmih aka coelh te khaw tueilaehkoi ni.
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Tlangpuei lamloh ka haeng tih khocuk khomik taeng lamloh halo. Ka ming te a phuk tih ukkung rhoek te amlai bangla a pah. Te vaengah amsai bangla tangnong a daep.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 A tong lamkah unim aka puen tih mikhmuh lamkah khaw ka ming vetih thuem ka ti uh eh. Aka puen khaw om pawh, aka yaak sak khaw om pawh, na ol aka ya khaw om pawh.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 Amih he lamhma la Zion taengah khaw, Jerusalem taengah khaw aka phong la ka paek coeng he.
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Ka hmuh nawn khaw hlang om pawh. Amih ka dawt vaengah ol mael hamla amih aka uen khaw om pawh.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Amih te boeih ah boethae ni ke. A bibi khaw a poei-oep, a tuisi khaw a khohli neh a hinghong ni.
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.

< Isaiah 41 >