< Isaiah 2 >

1 Judah neh Jerusalem ham Amoz capa Isaiah loh olka a hmuh.
Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
2 Hmailong kah a tue a pha vaengah BOEIPA im tlang te cikngae la om ni. Tlang dong neh som cawn vetih namtom boeih loh amah taengah hlampan uh ni.
Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3 Pilnam rhoek muep cet uh vetih, “BOEIPA kah tlang la cet uh sih, Jakob Pathen im te paan uh sih lamtah a longpuei te mamih n'thuinuet ni. Te daengah ni a caehlong ah m'pongpa eh. Olkhueng te Zion lamloh, BOEIPA ol tah Jerusalem lamloh ha thoeng ni.
Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4 Namtom rhoek lakli ah lai a tloek vetih, pilnam te a cungkuem la a tluung ni. Te vaengah a cunghang te tuktong la, a caai te vin la a dae uh ni. Namtom loh namtom taengah cunghang muk uh voel mahpawh. Caemtloek khaw cang uh voel mahpawh.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
5 Jakob imkhui halo lamtah BOEIPA kah vangnah khuiah cet uh sih.
Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
6 Na pilnam Jokob imkhui te na phap coeng. Khothoeng lamloh a et. Philisti bangla kutyaek a sawt uh tih kholong ca rhoek neh kut a paenguh.
Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7 A khohmuen ah ngun neh sui khaw bae tih a thakvoh khaw vawt pawh. A khohmuen ah marhang khaw bae tih a leng te bawt pawh.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8 A khohmuen ah a kut dongkah kutsai mueirhol bae tih a kutdawn neh a saii te a bakop thiluh.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9 Te dongah hlang he ngam vetih tongpa khaw kunyun ni. Tedae amih te dangrhoek boeh.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
10 BOEIPA taengkah birhihnah hmai lamloh, amah kah mingthennah rhuepomnah lungpang te paan saeh lamtah laipi khuiah khaw vuei uh saeh.
Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Hlang kah a oeknah mik tah kunyun vetih hlang buhuengpomnah khaw ngam ni. Te dongah te khohnin ah tah BOEIPA amah long ni a hoeptlang eh.
Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
12 Caempuei BOEIPA kah khohnin he thinthah neh aka pomsang boeih ham khaw, aka cangdoek neh kunyun boeih ham khaw om coeng.
Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
13 Lebanon lamphai boeih, Bashan kah thingsang, thinglen thingnu boeih ham khaw,
tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 Tlang sang boeih ham khaw, som thang boeih ham khaw,
tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 Rhaltoengim sang boeih ham khaw, vongtung, vong cak boeih ham khaw,
tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
16 Tarshish sangpho boeih ham khaw, sahnaih kutmuei boeih ham khaw om coeng.
tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
17 Te dongah hlang kah a oeknah te a ngam sak vetih, hlang kah buhuengpomnah khaw a kunyun sak ni. Te khohnin ah tah BOEIPA amah bueng ni aka sang eh.
Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18 Mueirhol rhoek khaw boeih khum ni.
ndipo mafano onse adzatheratu.
19 Diklai he huek ham a thoh vaengah BOEIPA kah birhihnah hmai neh amah mingthennah rhuepomnah lamloh lungpang lungko neh laipi khui te a paan uh.
Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 Te khohnin ah hlang loh amah kah cak mueirhol, sui mueirhol khaw a voeih ni. A bawk ham te khothal la, pumphak la a saii uh.
Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 Diklai huek ham a thoh vaengah BOEIPA kah birhihnah hmai neh a hoemdamnah rhuepomnah lamloh lungpang thaelrhaep neh thaelpang thaelvap la pawk uh ni.
Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
22 A hnarhong neh aka hiil hlang te toeng laeh, anih te metlamlae a ngai aih.
Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?

< Isaiah 2 >