< Isaiah 19 >

1 Egypt kah olrhuh, BOEIPA tah khomai dongah yanghoep la ngol tih Egypt la pawk. A mikhmuh ah Egypt mueirhol rhoek te hlinghlawk tih Egypt rhoek kah a thinko tah a khui ah paci coeng.
Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
2 Egypt te Egypt neh ka et thil vetih hlang long he a manuca khaw, hlang pakhat loh a hui khaw, khopuei neh khopuei khaw, ram pakhat ram pakhat a vathoh thil ni.
“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
3 Egypt kah a mueihla tah a khui ah hoep vetih a cilsuep ka hmaang sak ni. Te vaengah te mueirhol taengla, lung aka khueh, rhaitonghma neh hnam taengla a dawt uh bitni.
Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
4 Egypt te mangkhak boei rhoek kut ah ka det vetih amih te manghai aka tlung loh a ngol thil ni. Caempuei Yahovah Boeipa kah olphong coeng ni.
Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
5 Tuipuei tui khaw kak ni. Tuiva khaw rhaeng vetih haang ni.
Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
6 Tuiva te khaw pam vetih bawn ni. Egypt capu sokko te kak vetih carhaek khaw tloih ni.
Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
7 Sokko neh sokko hmoi kah sulhing neh sokko mutue boeih khaw rhae ni. Cuhu vetih om voel mahpawh.
ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
8 Tuihoi rhoek te huei uh vetih sokko ah vaih aka voei, lawk aka thing rhoek khaw boeih nguekcoi uh vetih tui soah tahah uh ni.
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
9 Hlamik a yawt neh aka thotat tih, hlabok aka tak rhoek khaw yak uh ni.
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 A rhungsut te tlawt vetih, kutphu la aka saii boeih khaw a hinglu ngat ni.
Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
11 Zoan mangpa rhoek khaw ang uh tangkik coeng tih Pharaoh kah olrhoep hlangcueih rhoek kah cilsuep khaw a dom coeng. Pharaoh te metlamlae, “Kamah tah hlamat kah manghai koca khuiah khaw ka cueih ca,” na ti eh?
Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
12 Nang kah hlangcueih rhoek te maelae me? Nang taengah ha puen uh laeh vetih caemgpuei Yahovah loh Egypt a caai thil te a ming uh laeh mako.
Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 Zoan mangpa rhoek te nga uh tih Noph mangpa rhoek khaw rhaithi uh thae. Egypt nim te amah koca rhoek te a cong cong ah kho a hmang uh coeng.
Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
14 BOEIPA loh a khui ah lungbuei lukil hnaven neh a thoek tih kho a hmang uh coeng. Egypt loh amah khoboe cungkuem dongah khohmang bangla a lok neh rhui uh.
Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 A lu neh a mai khaw, rhophoe neh canghlong khaw Egypt ham bitat aka saii thai te a om moenih.
Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
16 Tekah khohnin ah tah Egypt khaw huta bangla om vetih lakueng ni. Te vaengah anih a thueng thil caempuei BOEIPA kah kut thueng hmai ah birhih pueng ni.
Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
17 Judah khohmuen te Egypt taengah birhihkuihut la om ni. Anih a phoei carhui te khaw a taengah birhih ni. caempuei BOEIPA kah cilsuep loh anih a uen coeng.
Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
18 Tekah khohnin ah Egypt kho ah Kanaan ol la aka cal khopuei panga om ni. Te vaengah caempuei BOEIPA taengla ol aka caeng khopuei pakhat te tah koengloengnah khopuei a ti ni.
Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
19 Tekah khohnin ah Yahovah kah hmueihtuk te Egypt khohmuen kah a laklung ah, a khorhi ah Yahovah kah kaam om ni.
Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
20 Egypt khohmuen ah caempuei BOEIPA kah miknoek neh laipai la om ni. Aka nen kah mikhmuh ah BOEIPA taengla a pang uh vaengah amih aka khang tih aka tungaep ham te a tueih pah vetih amih te a huul ni.
Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
21 BOEIPA loh Egypt te a tukkil vetih Egypt loh BOEIPA te a ming uh ni. Te khohnin ah hmueih neh khocang neh tho a thuenguh. Te vaengah BOEIPA taengah olcaeng neh a caeng uh vetih a thuung uh ni.
Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
22 BOEIPA loh Egypt te a yawk sak ni. A yawk sak tih a hoeih daengah ni BOEIPA taengla a mael uh eh. Amih a thangthui uh vaengah amih te a hoeih sak ni.
Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
23 Te khohnin ah Egypt lamloh Assyria duela longpuei om. Assyria te Egypt la, Egypt khaw Assyria la cet ni. Egypt neh Assyria loh tho a thueng ni.
Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
24 Te khohnin ah Israel te a pathum la Egypt neh Assyria taengah diklai laklung kah yoethennah neh om van ni.
Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
25 Anih te caempuei BOEIPA loh a uem vetih, “Ka pilnam Egypt neh ka kut saii Assyria khaw, ka rho Israel khaw a yoethen,” a ti ni.
Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”

< Isaiah 19 >