< Suencuek 24 >
1 Abraham khaw a tue loh patong ben a paan coeng dae a cungkuem dongah BOEIPA loh Abraham te yoethen a paek.
Tsopano Abrahamu anali atakalamba kwambiri, ndipo Yehova anamudalitsa mu zonse anachita.
2 Te dongah Abraham loh a im kah a koe boeih aka taem sal a ham taengah, “Na kut te ka phai hmuiah tloeng laeh.
Tsiku lina Abrahamu anawuza wantchito wake wamkulu amene ankayangʼanira zonse anali nazo, kuti “Ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga.
3 Kai loh amih lakli ah kho ka sak dae Kanaan nu rhoek te ka capa kah a yuu la lo boeh.
Ndikufuna kuti ulumbire pamaso pa Yehova, Mulungu wakumwamba ndi dziko lapansi, kuti sudzamupezera mwana wanga mkazi pakati pa atsikana Achikanaani a kuno kumene ndikukhala,
4 Tedae ka khohmuen neh ka pacaboeina taengah cet lamtah ka ca Isaak ham yuu loh pah tila vaan Pathen, diklai Pathen BOEIPA ming neh nang kan toemngam sak,” a ti nah.
koma kuti udzapita ku dziko la kwathu ndi kukamupezera mkazi mwana wanga Isake pakati pa abale anga.”
5 Te dongah a sal loh Abraham te, “Hekah khohmuen la kai hnukah vai ham huta loh a huem pawt khaming, na poenah kho la na capa te ka bal khaw ka bal puei aya?” a ti nah.
Wantchito uja anafunsa kuti, “Nanga atakhala kuti mkaziyo sakufuna kubwera nane kuno? Kodi ine ndingadzatenge mwana wanu ndi kubwerera naye ku dziko kumene munachokera?”
6 Tedae Abraham loh anih taengah, “Nang te ngaithuen, ka capa te ke la na khuen ve ne.
Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.
7 A pa im neh ka pacaboeina khohmuen lamkah kai aka khuen tih ka taengah a thui vaengah, 'Hekah khohmuen he nang tiingan ham ka khueh ni, ' tila aka toemngam, vaan kah Pathen BOEIPA loh nang hmai ah amah kah puencawn te a tueih vetih ka capa ham a yuu te ke lamkah nan loh pah bitni.
Yehova Mulungu wakumwamba amene ananditenga kwa makolo anga nanditulutsa mʼdziko lobadwira, ameneyo anayankhula nane molumbira kuti, ‘Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko ili.’ Iyeyu adzatumiza mngelo wake kuti akutsogolere kumeneko kukapezera mwana wanga mkazi.
8 Tedae huta loh nang taengah lo ham a huem pawt atah ka olhlo dong lamloh m'hmil saeh. Tedae ka capa te ke la khuen boeh,” a ti nah.
Ngati mkaziyo adzakana kubwerera nawe ndiye kuti udzakhala womasuka ku lumbiro langa. Koma usadzamutenge mwana wanga ndi kubwerera naye kumeneko.”
9 Te dongah salpa loh a kut te a boei Abraham kah a phai hmuiah a khueh tih hekah olka ham amah taengah a toem a ngam.
Choncho wantchitoyo anayika dzanja lake pansi pa ntchafu ya mbuye wake Abrahamu nalumbira kwa iye kuti adzachitadi monga mwa mawu a Abrahamu.
10 Te phoeiah salpa loh a boei kah kalauk pumrha a loh tih a kut ah a boei kah thennah cungkuem neh cet. Te vaengah thoo tih Nakhaw kah khopuei Aramnaharaim la cet.
Tsono wantchito uja anatengapo ngamira khumi mwa ngamira za mbuye wake pamodzi ndi zinthu zabwino za mitundumitundu. Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda wa Nahori, mʼdziko la Mesopotamiya.
11 Tedae hlaem tue vaengkah tuithan rhoek a caeh tue vaengah kalauk te khopuei voel kah tuito tui taengah a kol sak tih,
Atafika, anagwaditsa pansi ngamira zija pafupi ndi chitsime chimene chinali kunja kwa mzinda uja. Awa anali madzulo ndithu, nthawi imene amayi amapita kukatunga madzi.
12 “Ka boei Abraham kah BOEIPA Pathen aw, ka boei Abraham taengah sitlohnah han saii lamtah tihnin ah kai he m'phu sak laeh.
Ndipo wantchito uja anapemphera nati, “Haa, Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, mulole kuti zinthu zindiyendere ine lero, ndipo muonetseni mbuye wanga Abrahamu kukoma mtima kwanu kosasinthika.
13 Tuiphuet tui kah ka pai vaengah tui than la khopuei hlang kah tanu aka lo rhoek khuikah,
Taonani ndayima pambali pa chitsimechi, ndipo atsikana a mu mzindawu akubwera kudzatunga madzi.
14 Hula aka om te, 'Na amrhaeng hal dae lamtah tui ka o eh?,’ ka ti nah vaengah, 'O lamtah na kalauk rhoek khaw tui kan tul eh?,’ aka ti te na sal Isaak ham na hmoel pah. Anih dongah ka boei taengah sitlohnah nan saii tila ka ming ni,” a ti nah.
Ine ndipempha mtsikana wina kuti, ‘Chonde tula mtsuko wako kuti ndimweko madzi.’ Tsono iye akayankha kuti ‘Imwani,’ ndipo ndidzapatsanso ngamira zanu madziwo, ameneyo akhale mkazi amene mwasankhira mtumiki wanu Isake.” Zimenezi zikachitika, ndidzadziwa kuti mwaonetsadi kukoma mtima kwanu kosasinthika kwa mbuye wanga.
15 Tedae a thui te a khah hlanah Abraham kah a manuca Nakhaw yuu Milkah capa Bethuel loh a sak Rebekah te a laengpang ah amrhaeng neh pakcak ha pawk.
Asanatsirize kupemphera, anangoona Rebeka watulukira atasenza mtsuko wake pa phewa. Iyeyu anali mwana wa Betueli mwana wa Milika, mkazi wa Nahori mʼbale wake wa Abrahamu.
16 A mueimae bahoeng aka then huta oila la om tih anih tetongpa loh ming hlan. Tuiphuet la suntla tih amrhaeng te a than tih yoeng.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri, namwali amene sanadziwe mwamuna. Iye anatsikira ku chitsime nadzaza mtsuko nakweranso ku mtunda.
17 Te dongah anih doe ham salpa te yong. Te phoeiah, “Nang kah amrhaeng tui bet n'coih ne,” a ti nah.
Wantchito uja anathamanga kukakumana naye nati, “Chonde patseko madzi pangʼono a mu mtsuko wakowo kuti ndimwe.”
18 Te dongah, “Ka boeipa o mai saw,” a ti nah tih a kut kah a amrhaeng te khaw koe a hal pah. Te phoeiah anih te a tul.
Mtsikanayo anati, “Imwani mbuye wanga.” Ndipo mofulumira anatsitsa mtsuko uja nawuyika mʼmanja ndi kumupatsa kuti amwe.
19 Anih te bawt a tul phoeiah, “Na kalauk rhoek ham khaw a ok rhoeh hil kan than dae eh,” a ti nah.
Atatha kupereka madzi akumwa kwa mlendo uja, mtsikanayo anati, “Ndikatungiranso ngamira madzi kuti zimwe mpaka zitakwana.”
20 Te phoeiah a amrhaeng te tuisoi dongah koe a kingling tih tui than hamla tuito la koep yong. Te phoeiah a kalauk boeih ham tui a than.
Choncho anafulumira kukhuthula madzi a mu mtsuko aja momwera ziweto, nathamanga kubwerera ku chitsime kukatunga madzi ena, ndipo anatunga okwanira ngamira zake zonse.
21 BOEIPA loh a longpuei a thaihtak sak neh a thaihtak sak pawt khaw ming hamla tongpa loh huta te duem a boelh.
Modekha, munthu uja anayangʼanitsitsa kwambiri mtsikana uja kuti adziwedi ngati Yehova anamutsogolera pa ulendo wake uja kapena ayi.
22 Te dongah kalauk loh bawt a ok nen tah tongpa loh sui hnaii a khiing beka khat neh a kut dongkah ham sui khungpak panit, a khiing parha te a loh.
Ngamira zija zitatha kumwa, mlendo uja anatulutsa chipini chagolide cholemera theka la sekeli ndi zibangiri zagolide ziwiri zolemera masekeli 100.
23 Te phoeiah, “Nang ukah canu lae? Kai taengah thui lah. Na pa im ah pah ham a hmuen kaimih ham om aya?,” a ti nah.
Kenaka anafunsa namwaliyo kuti, “Chonde tandiwuza, kodi ndiwe mwana wa yani? Ndipo kodi malo alipo kwanu woti ife nʼkugona?”
24 Te dongah anih taengah, “Kai tah Milkah loh Nakhaw ham a cun a capa Bethuel canu ni,” a ti nah.
Anamuyankha kuti, “Ine ndine mwana wa Betueli, mwana amene Milika anaberekera Nahori.”
25 Te phoeiah anih te, “Kaimih taengah cangkong khaw, kamvuelh khaw, coih tih rhaeh hmuen khaw om,” a ti nah.
Ndipo anapitiriza kunena kuti, “Chakudya chodyetsa nyamazi chilipo kwathu ndipo malo woti mugone aliponso.”
26 Te dongah tekah hlang te buluk tih BOEIPA te a bawk.
Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,
27 Te phoeiah, “Ka boei Abraham kah Pathen BOEIPA tah a yoethen pai. A sitlohnah neh uepomnah loh ka boei te hnoo pawh. Kai khaw ka boei kah a manuca im duela longpuei ah BOEIPA loh m'mawt coeng,” a ti.
nati, “Alemekezeke Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene waonetsa kukoma mtima kwake kosasintha ndi kukhulupirika kwake kwa mbuye wanga. Yehova wanditsogolera pa ulendo wanga mpaka ndafika ku nyumba kwa abale ake a mbuye wanga.”
28 Hula te khaw yong tih hekah olka te a manu cako ham a thui pah.
Mtsikana uja anathamanga nakafotokozera zimenezi anthu a kwa amayi ake.
29 Te vaengah Rebekah te a nganpa, a ming ah Laban khaw om. Te dongah Laban te tollong la yong tih tuiphuet kah hlang taengla cet.
Tsono Rebeka anali ndi mlongo wake dzina lake Labani.
30 Tedae hnaii neh a ngannu kut kah khungpak te lawt a hmuh tih a ngannu Rebekah loh, “Tekah hlang loh kai taengah a thui,” a ti nah, ol a yaak. Hlang te a paan vaengah tah, tuiphuet kah kalauk taengah sut ana pai pah.
Iyeyu atangoona chipini pa mphuno ndi zibangiri pa mikono ya mlongo wake komanso kumva zimene mlendo uja ananena kwa Rebekayo, anathamangira kwa mlendo uja, ndipo anamupeza atangoyima ndi ngamira zake pafupi ndi chitsime.
31 Te dongah, “BOEIPA kah yoethen a paek tah halo pai. Balae tih vongvoel ah na pai? Kai khaw im neh kalauk ham hmuen ka rhoekbah coeng ta,” a ti nah.
Iye anati, “Tiyeni kwathu, ndinu munthu amene Yehova wamudalitsa. Bwanji mwangoyimirira panja pano? Ine ndakukonzerani malo ogona inu ndi ngamira zanu.”
32 Te daengah tekah hlang loh im la cet tih kalauk te a hlam. Te phoeiah kalauk ham cangkong neh kamvuelh khaw, anih kho neh a taengkah hlang rhoek kho silh nah hamla tui khaw a paek.
Choncho munthu uja analowa mʼnyumba. Labani anatsitsa katundu anali pa ngamira uja. Kenaka anazipatsa ngamira zija chakudya, ndiponso anapereka madzi wosamba mapazi kwa mlendo uja ndi anthu ena onse.
33 Te phoeiah caak te amih hmai ah a tawn pah hatah, “Kamah kah olka ka thui hlanah ka ca mahpawh,” a ti nah. Te dongah, “Thui,” a ti nah hatah,
Chakudya chitabwera mlendo uja anati, “Sindidya mpaka nditakuwuzani zimene ndadzera kuno.” Labani anati, “Yankhulani.”
34 “Kai tah Abraham kah sal ni.
Motero iye anati, “Ine ndine wantchito wa Abrahamu.
35 Tahae ah BOEIPA loh ka boeipa te yoethen muep a paek dongah boei coeng. Te phoeiah anih te boiva khaw, saelhung khaw, cak neh sui khaw, salpa neh salnu khaw, kalauk neh laak khaw a paek.
Yehova wadalitsa mbuye wanga kwambiri, ndiponso walemera. Wamupatsa nkhosa ndi ngʼombe, siliva ndi golide, antchito aamuna ndi antchito aakazi, komanso ngamira ndi abulu.
36 Ka boeipa kah a yuu Sarah khaw a patong soiah ka boeipa ham ca a sak pah tih a taengkah koe boeih te anih ham a khueh pah.
Sara, mkazi wa mbuye wanga anamubalira iye mwana wamwamuna ngakhale kuti Sarayo anali wokalamba. Tsono mbuye wanga wamupatsa mwanayo chuma chonse.
37 Tedae ka boeipa loh kai te, 'Ka capa yuu ham tah kai loh kho ka sak thil khohmuen kah Kanaan nu te loh pah boeh.
Tsono mbuye wanga anandilumbiritsa kuti ndisunge mawu ake akuti, ‘Usadzamupezere mwana wanga mkazi kuchokera mwa atsikana a dziko lino la Kanaani,
38 Tedae a pa im la lat cet lamtah kamah huiko te ka ca yuu la loh pah,’ a ti tih a toem a ngam.
koma upite ku banja la abambo anga ndi kwa abale anga kuti ukamupezere mkazi mwana wanga.’”
39 Tedae ka boeipa te, 'Kai hnukah huta te halo pawt khaming,’ ka ti nah hatah,
“Ndipo ine ndinati kwa mbuye wanga, ‘Nanga mkaziyo akakapanda kubwera nane pamodzi?’
40 'BOEIPA amah mikhmuh ah ni kai ka caeh. Nang taengah amah kah puencawn te han tueih vetih na longpuei a thaihtak sak vaengah ka capa yuu khaw kamah huiko neh a pa im lamkah te na loh thai ni.
“Iye anayankha, ‘Yehova amene ndakhala ndikumumvera nthawi zonse, adzatumiza mngelo wake kuti akuperekeze ndipo adzakuthandiza mpaka ukamupezere mwana wanga mkazi kuchokera ku mtundu wanga, wa fuko langa.
41 Kamah huiko taengla na pawk mak atah kai kah thaephoeinah lamkah m'hmil bitni. Nang taengah a canu te m'paek uh pawt akhaw kai kah thaephoeinah lamkah ommongsitoe la na om ngawn ni, ' a ti.
Ukadzachita zimenezi udzakhala mfulu wosamangidwa ndi lumbiro langali. Koma tsono ukadzafika kwa fuko langa, ndipo ngati sadzalola kukupatsa mbeta ya mwana wanga, aponso udzamasuka ku lumbiro langali.’”
42 Tedae tihnin ah tuiphuet te kam pha tih, 'Ka boei Abraham kah Pathen BOEIPA aw, namah na om atah he la ka pongpa vaengah ka longpuei han thaihtak sak laeh.
“Tsono lero lino pamene ndafika pa chitsime, ndinapempha kuti, ‘Yehova, Mulungu wa mbuye wanga, Abrahamu, ngati Inu mwandidalitsadi pa ulendowu,
43 Kai loh tuiphuet kah tui taengah he ka pai vaengah tuithan la aka lo hula te om mai tih anih te, “Na amrhaeng dongkah tui te kai bet n'tul laem,’ ka ti nah vetih,
taonani ndayima pambali pa chitsime ichi; ndipo ndidzati kwa namwali amene atabwere kudzatunga kuti, chonde nditamwako madzi a mu mtsuko wakowu,’
44 Te vaengah kai taengah, 'Namah o ngawn lamtah na kalauk rhoek ham khaw kan than eh?,’ ti saeh. Tekah huta te ka boeipa kah a capa ham BOEIPA loh hmoel saeh,” ka ti.
ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”
45 Kai loh ka lungbuei ah ka thangthui te ka khah hlanah mah Rebekah loh a laengpang sokah amrhaeng neh tarha ha pawk tih tuiphuet la suntla thuk. Tui a than phoeiah anih te, 'Kai n'tul laem,’ ka ti nah.
“Ndisanatsirize kupemphera, ndinangoona Rebeka akutulukira mtsuko wake uli pa phewa. Anatsetserekera ku chitsime kukatunga madzi ndipo ndinati kwa iye, ‘Chonde patseko madzi akumwa.’
46 Te vaengah amah pum dongkah amrhaeng te koe a hal tih, 'O lamtah na kalauk rhoek khaw ka tul eh?,” a ti. Te dongah ka ok tih kalauk rhoek te khaw tui a tul.
“Mofulumira, anatsitsa mtsuko wake pa phewa pake nati, ‘Imwani ndiponso ndizimwetsa madzi ngamira zanuzi.’ Kotero ine ndinamwa ndipo anamwetsanso ngamirazo.
47 Te phoeiah anih te ka dawt tih, 'Nang u canu lae?' ka ti nah vaengah Milkah loh Nakhaw ham a sak pah a capa Bethuel canu ni, ' a ti. Te dongah a hnarhong ah hnaii ka bang pah tih a kut ah khungpak ka buen sak.
“Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,
48 Te phoeiah ka buluk tih BOEIPA te ka bawk vaengah, “Ka boei kah a manuca canu te a capa ham aka lo la oltak longpuei ah kai aka mawt ka boei Abraham kah BOEIPA Pathen te ka uem.
kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
49 Tedae tahae ah ka boeipa ham sitlohnah neh uepomnah tueng ham na huem atah kai taengah thui lah. Kai taengah na thui uh pawt bal atah banvoei bantang la ka mael mai eh,” a ti nah.
Tsono ngati mukufuna kuonetsa kukoma mtima kwanu kwa mbuye wanga, ndikuonetsa kukhulupirika kwanu, ndiwuzeni; ndipo ngati si choncho ndiwuzeninso kuti ndidziwe chochita.”
50 Te dongah Laban neh Bethuel loh a doo tih, “BOEIPA lamkah olka aka thoeng te a thae then khaw nang taengah ka thui rhoi thai pawh.
Labani ndi Betueli anayankha nati, “Izi ndi zochokera kwa Yehova, ndipo ife sitinganenepo kanthu.
51 Na mikhmuh ah Rebekah aka om he lo lamtah caeh puei. BOEIPA kah a thui vanbangla na boeipa capa kah a yuu la om saeh,” a ti rhoi.
Nayu Rebeka, mutengeni muzipita naye kuti akakhale mkazi wa mwana wa mbuye wanu, monga Yehova wanenera.”
52 Amih rhoi kah olka te Abraham kah sal loh a yaak vaengah BOEIPA taengah diklai la bakop tih a bawk.
Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.
53 Te phoeiah salpa loh cak hnopai neh sui hnopai khaw, himbai khaw a sat tih Rebekah te a paek. A nganpa neh a manu te khaw kawnthen a paek pah.
Kenaka wantchitoyo anatulutsa ziwiya zagolide ndi zasiliva ndi zovala nazipereka kwa Rebeka. Anaperekanso mphatso zina za mtengowapatali kwa mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka.
54 Te daengah amah neh amah taengkah hlang rhoek khaw a caak a ok uh tih rhaeh uh. Mincang a thoh uh vaengah, “Ka boeipa taengah kai n'tueih mai laeh,” a ti nah.
Tsono wantchito uja ndi anthu amene anali naye anadya, kumwa nagona komweko. Kutacha mmawa wake, wantchito uja anati, “Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
55 Tedae a nganpa neh a manu loh, “Hula he kaimih taengah khohnin hninrha tluk om dae vetih na cet mako,” a ti nah.
Koma mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka anayankha kuti, “Muloleni mtsikanayu abakhala nafe masiku khumi kapena kupyolerapo, kenaka mukhoza kupita.”
56 Te dongah Abraham kah salpa loh amih taengah, “BOEIPA loh ka longpuei han thaihtak sak vanbangla kai he n'hloh uh boel mai. Ka boeipa taengah n'tueih mai lamtah kai ka cet mai eh,” a ti nah.
Koma iye anawawuza kuti, “Chonde musandichedwetse. Yehova wandithandiza kale pa ulendo wanga. Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
57 Te dongah, “Hula te khue uh sih lamtah amah olthui te dawt uh dae sih,” a ti uh.
Koma iwo anati, “Bwanji timuyitane mtsikanayo ndipo timufunse ngati afuna kupita nanu panopa.”
58 Rebekah te a khue uh phoeiah, “Hekah hlang taengah na cet aya?” a ti nah uh vaengah, “Ka cet ni ta,” a ti.
Choncho iwo anamuyitana Rebeka uja namufunsa kuti, “Kodi ukufuna kupita ndi munthuyu panopa?” Iye anayankha kuti, “Ndipita.”
59 Te dongah a ngannu Rebekah neh anih kah cakhoem te khaw, Abraham kah sal neh a hlang rhoek te khaw a tueih uh.
Kotero anamulola Rebeka pamodzi ndi mlezi wake kuti apite ndi wantchito wa Abrahamu pamodzi ndi anthu amene anali naye.
60 Te vaengah Rebekah te yoethen a paek uh tih amah taengah, “Ka ngannu nang tah a thawng thawngrha la coeng lamtah, na tiingan loh a lunguet kah vongka te huul saeh,” a ti nahuh.
Ndipo iwo anadalitsa Rebeka ndi kumuwuza kuti, “Iwe ndiwe mlongo wathu, Mulungu akudalitse iwe, ukhale mayi wa anthu miyandamiyanda; ndi kuti zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo.”
61 Te phoeiah Rebekah neh hula rhoek te thoo uh tih kalauk soah ngol uh. tongpa hnukah a caeh uh ham coeng dongah Rebekah te Abraham kah sal loh a loh tih a caeh puei.
Kenaka Rebeka ndi antchito ake ananyamuka kukakwera ngamira zawo ndipo anapita naye pamodzi munthu uja. Choncho wantchito uja anatenga Rebeka nʼkumapita.
62 Te vaengah Negev kho ah khosak ham Beerlahairoi lamkah aka lo Isaak khaw ha pawk.
Pa nthawiyi nʼkuti Isake atafika kuchokera ku chitsime cha Wamoyo Wondipenya (Beeri-lahai-roi), popeza tsopano ankakhala ku Negevi.
63 Hlaem a pha vaengah Isaak te lohma la cet tih kho a poek. Te vaengah a mik a huel tih a sawt hatah kalauk tarha ha khong pah.
Tsiku lina chakumadzulo, Isake anatuluka kukayendayenda ku munda, ndipo atakweza maso anaona ngamira zikubwera.
64 Rebekah long khaw a mik a huel hatah Isaak te a hmuh tih kalauk so lamloh rhum thuk.
Rebeka nayenso anatukula maso naona Isake. Ndipo anatsika pa ngamira yake
65 Te phoeiah salpa taengah, “Mamih doe ham lohma li ah tongpa aka lo ke ulae?,” a ti nah vaengah a salpa loh, “Ka boeipa ni,” a ti nah dongah hnii te a loh tih a yil.
nafunsa wantchito uja kuti, “Kodi munthu uyo ndi ndani akuyenda mʼmundamo kubwera kudzakumana nafe?” Wantchitoyo anayankha, “Ndiye mbuye wanga.” Choncho Rebeka anatenga nsalu ndi kufunda kumaso.
66 Te phoeiah salpa loh a saii hno boeih te Isaak taengah a thui.
Tsono wantchito uja anawuza Isake zonse zimene anazichita.
67 Isaak loh hula te dap khuikah a manu Sarah taengla akhuen. Te phoeiah Rebekah te a loh tih anih yuu la coeng. Te dongah anih te a lungnah tih a manu hnukah Isaak khaw hal van.
Isake analowa naye Rebeka mu tenti ya amayi ake Sara, ndipo anakhala mkazi wake. Isake anamukonda kwambiri Rebeka mkazi wake motero kuti zimenezi zinamutonthoza imfa ya amayi ake.