< Ezekiel 28 >

1 BOEIPA ol te kai taengah ha pawk tih,
Yehova anandiyankhula nati:
2 “Hlang capa aw, Ka Boeipa Yahovah loh a thui he Tyre rhaengsang taengah thui pah. Na lungbuei sang tih, 'Kai la pathen, tuipuei tuilung kah pathen tolrhum ah ka ngol,’ na ti. Tedae nang hlang tangkik loh na lungbuei tah pathen lungbuei la na poek cakhaw na pathen moenih.
“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu; ndimakhala pa mpando wa mulungu pakati pa nyanja.’ Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu, ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.
3 Daniel lakah Daniel la na cueih ta te. A kael boeih khaw nang ham a hmuep moenih ko te.
Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli. Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.
4 Na cueihnah neh na lungcuei lamloh na thadueng la na saii. Na thakvoh khuiah sui neh cak na hen.
Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako unadzipezera chuma ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva mʼnyumba zosungira chuma chako.
5 Na hnothungnah dongah na cueihnah khaw puh tih na thadueng sai van. Tedae na thadueng dongah na thinko sang.
Ndi nzeru zako zochitira malonda unachulukitsa chuma chako ndipo wayamba kunyada chifukwa cha chuma chakocho.
6 Na thinko te pathen kah lungbuei bangla na ngai dongah ni ka Boeipa Yahovah loh he he a thui.
“‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Popeza umadziganizira kuti ndiwe mulungu,
7 Te dongah ni hlanghaeng neh namtom kholong te nang taengla kang khuen he. A cunghang neh na cueihnah sakthen te a khoh uh vetih na omyalnah khaw a poeih ni.
Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza, kuti adzalimbane nawe. Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako, ndipo adzawononga kunyada kwakoko.
8 Vaam khuila nang n'suntlak sak uh vetih tuipuei tuilung ah rhok dongkah dueknah neh na duek ni.
Iwo adzakuponyera ku dzenje ndipo udzafa imfa yoopsa mʼnyanja yozama.
9 Nang aka ngawn kah mikhmuh ah, 'Kai la pathen,’ na ti khaw na ti aya? Nang adam ngawn tah namah aka poeih kut ah na pathen moenih.
Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’ pamaso pa iwo amene akukupha? Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu, mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.
10 Kamah loh ka thui coeng dongah kholong kut ah ni pumdul kah dueknah neh na duek eh. He tah ka Boeipa Yahovah kah olphong ni,” a ti.
Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe mʼmanja mwa anthu achilendo. Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’”
11 BOEIPA ol te kai taengla ha pawk bal tih,
Yehova anandiyankhula kuti:
12 Hlang capa aw Tyre manghai ham rhahlung phueih pah lamtah amah te thui pah. Ka Boeipa Yahovah loh he ni a thui. Cueihnah khuengrhueng neh sakthen boeih kah cungkuemnah kutha aka daeng khaw nang ni.
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni, wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.
13 Pathen kah dum Eden ah tah lung vang cungkuem te na thoeicamnah tih lungling vaya, lungmik, timsuih, oitha, maihae, minhum khocillung neh tamkuei, na kamrhing neh na rhotak toembael sui hnopai neh nang n'suen khohnin ah ni na khuiah a tawn uh.
Iwe unkakhala ngati mu Edeni, munda wa Mulungu. Miyala yokongola ya mitundu yonse: rubi, topazi ndi dayimondi, kirisoliti, onikisi, yasipa, safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako. Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide. Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.
14 Nang tah koelhnah aka thingthung cherubim ni. Te dongah ni Pathen kah cimcaihnah tlang ah nang kang khueh. Hmai lungto lakli ah khaw na om tih na pongpa coeng.
Ndinayika kerubi kuti azikulondera. Unkakhala pa phiri langa lopatulika, ndipo unkayendayenda pakati pa miyala ya moto.
15 Nang kan suen khohnin lamloh na khuikah dumlai a phoe hil pataeng na longpuei ah na cuemthuek.
Makhalidwe ako anali abwino kuyambira pamene unalengedwa mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.
16 Na hnothungnah kah a puhnah lamloh na kotak te kuthlahnah hah tih na tholh. Te dongah ni Pathen kah tlang lamloh nang kam poeih tih hmai lungto lakli lamkah aka thingthung cherubim taeng lamloh nang kam milh sak.
Unatanganidwa ndi zamalonda. Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu ndi kumachimwa. Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika. Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa kukuchotsa ku miyala yamoto.
17 Na sakthen dongah na lungbuei khaw sang tih na cueihnah neh na poci. Na omyalnah dongah ni diklai la manghai rhoek kah mikhmuh ah nang kam voeih tih nang te sawt sak ham nang kang khueh.
Unkadzikuza mu mtima mwako chifukwa cha kukongola kwako, ndipo unayipitsa nzeru zako chifukwa chofuna kutchuka. Kotero Ine ndinakugwetsa pansi kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.
18 Na hnothungnah dumlai dongah namah kathaesainah tah khawk tih na rhokso ni na poeih coeng. Te dongah ni na khui lamloh hmai ka puek sak tih nang n'hlawp. Te vaengah nang aka so boeih kah mikhmuh ah nang te diklai hmaiphu la kang khueh.
Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako. Motero unayipitsa malo ako achipembedzo. Choncho ndinabutsa moto pakati pako, ndipo unakupsereza, ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi pamaso pa anthu onse amene amakuona.
19 Pilnam khuikah nang aka ming boeih loh nang soah hal uh coeng. Mueirhih la na poeh tanglang tih kumhal duela na phoe pawh,” a ti.
Anthu onse amitundu amene ankakudziwa akuchita mantha chifukwa cha iwe. Watheratu mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’”
20 BOEIPA ol te kai taengla ha pawk bal tih,
Yehova anandiyankhula nati:
21 “Hlang capa aw Sidon te na maelhmai khueh thil lamtah tonghma thil laeh.
“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti,
22 vaengah ka Boeipa Yahovah loh a thui he thui pah. Kai loh Sidon nang kam pai thil coeng ne. Na kotak khuiah ka thangpom uh vetih BOEIPA kamah tila m'ming uh bitni. Tholhphu te anih soah ka saii vetih a khuiah ka ciim uh bitni.
‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni, ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe. Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti ndine woyera pakati pako.
23 A khuikah duektahaw neh a kawtpoeng ah thii ka tueih vaengah a kaepvai kah cunghang neh a kholung ah a rhok la cungku ni. Te vaengah BOEIPA kamah te m'ming uh bitni.
Ndidzatumiza mliri pa iwe ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako. Anthu ophedwa ndi lupanga adzagwa mbali zonse. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
24 Te vaengah Israel imkhui ham tangti kah a huet neh hling kah a do khaw om voel mahpawh. A kaepvai boeih lamkah amih aka hnaep long khaw kai he ka Boeipa Yahovah ni tila a ming uh bitni.
“‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
25 Ka Boeipa Yahovah loh he ni a thui. Israel imkhui te pilnam lamloh ka coi. Amih taengla taekyak uh cakhaw namtom mikhmuh kah amih taengah ka ciim coeng. Te dongah a khohmuen ah kho a sak uh ni. Te te ka sal Jakob taengah ka paek coeng.
“‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo.
26 A khuiah ngaikhuek la hing uh vetih im a sak uh ni. Misur a phung uh vetih ngaikhuek la hing uh ni. A kaepvai lamkah amih aka hnaep boeih soah tholhphu ka suk vaengah kai he BOEIPA a Pathen la a ming uh bitni.
Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’”

< Ezekiel 28 >