< Thuituen 10 >
1 Dueknah pilyang loh thungnom situi thaa te a rhim sak bangla vel lunghmangnah vik te cueihnah lakah khaw, thangpomnah lakah khaw nul.
Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
2 Aka cueih kah lungbuei tah a bantang la mael tih aka ang kah lungbuei tah a banvoei la mael.
Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
3 Longpuei ah pataeng lunghmang tah lunghmang bangla a lungbuei a talh hil pongpa tih a lunghmang te a cungkuem taengah a thui.
Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
4 Aka taemrhai kah mueihla loh nang taengah pai mai cakhaw na hmuen phawt boeh. Hoeihnah long ni tholhnah a len khaw a duem sak.
Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
5 Boei mikhmuh lamloh tohtamaeh la aka thoeng ka hmuh te khomik hmuiah a thae la om.
Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
6 Pavai te hmuensang la muep a khueh vaengah hlanglen tah mathoe la kho a sak.
Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
7 Marhang dongkah sal rhoek ka hmuh vaengah mangpa rhoek tah diklai ah sal bangla pongpa uh.
Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
8 Rhom aka too khaw a khuila cungku tih vongtung aka phae khaw rhul loh amah a tuk.
Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
9 Lungto aka puen khaw amah ah a kothae tih thing aka phaek khaw te nen te tohngah saeh.
Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
10 Thi te duu tih a ha te a haat pawt atah thadueng khaw vak. Tedae rhoeikhangnah tah cueihnah long ni a khui sak.
Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
11 Calthai a om pawt ah rhul loh a tuk atah cal kung ham rhoeikhangnah moenih.
Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
12 Hlang cueih ka dongkah ol tah mikdaithen om tih aka ang kah hmuilai long tah amah a dolh.
Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
13 A ka dongkah ol tongnah te lunghmangnah la om tih a ka dongkah ol bawtnah khaw boethae angvawknah la om.
Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
14 Lunghmang tah ol pung tih metla a om khaw hlang loh ming pawh. A hnuk ah metla a om ham khaw a taengah ulong a thui pah voel?
ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
15 Hlang ang kah thakthaenah loh amah a kohnue sak tih khopuei la caeh ham khaw ming pawh.
Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
16 Na manghai khaw camoe tih na mangpa rhoek loh mincang ah nah a caak uh te, khohmuen nang ngawn tah khomap.
Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
17 Na manghai te hlangcoelh capa van tih, na mangpa rhoek long khaw rhuihahnah ham pawt tih thayung thamal hamla a tue vaengah aka ca khohmuen nang tah na yoethen.
Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
18 Ngaknah lamloh tul pae hmawn tih kut poemnah lamloh im cae.
Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
19 Nueihbu ham buh a khueh tih misurtui loh hingnah ko a hoe sak. Tedae tangka loh a cungkuem te a doo.
Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
20 Na cangnah nen khaw manghai te tap boeh. Imkhui kah na thingkong dongah khaw hlanglen te tap boeh. Vaan kah vaa loh ol te khuen vetih ol te a phae loh a kungmah taengah thui ve.
Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.