< 2 Khokhuen 30 >
1 Hezekiah loh Israel pum neh Judah a tah tih Ephraim neh Manasseh ham khaw Jerusalem kah BOEIPA im la a mop ham neh, Israel Pathen BOEIPA taengah Yoom saii ham te ca a daek pah.
Hezekiya anatumiza uthenga mʼdziko lonse la Israeli ndi ku Yuda ndiponso analemba makalata ku Efereimu ndi Manase, oyitana anthu kuti abwere ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli.
2 A hla bae dongah tah Yoom saii hamla manghai khaw, a mangpa rhoek khaw, Jerusalem kah hlangping boeih khaw a thui uh.
Mfumu ndi akuluakulu ake pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu anagwirizana kuti akondwerere Paska pa mwezi wachiwiri.
3 Tedae Yoom te te vaeng tue ah saii hamla noeng uh pawh. Khosoih rhoek khaw a rhoeh hil ciim uh hlan tih pilnam khaw Jerusalem ah tingtun hlan.
Iwo sanathe kukondwerera pa nthawi yake chifukwa si ansembe ambiri amene anadziyeretsa ndiponso anthu anali asanasonkhane mu Yerusalemu.
4 Te vaengah ol he manghai mikhmuh ah khaw, hlangping boeih kah mikhmuh ah khaw dueng ngawn.
Chikonzerochi chinaoneka kuti chinali chabwino kwa mfumu pamodzi ndi anthu onse.
5 A daek bangla a saii uh dae a cungkuem uh pawt dongah, Israel Pathen BOEIPA kah Yoom saii vaengah tah Jerusalem la mop sak ham, Israel pum ah, Beersheba lamloh Dan duela olthang pat ham ol a cak sakuh.
Iwo anagwirizana zoti alengeze mu Israeli monse kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani, kuyitana anthu kuti abwere ku Yerusalemu ndi kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. Si ambiri amene ankachita chikondwererochi monga momwe kunalembedwera.
6 Manghai neh a mangpa rhoek kut dongkah ca aka yong puei rhoek tah Judah neh Israel pum ah cet uh tih manghai olpaek bangla, “Israel ca rhoek aw, Abraham, Isaak, Israel Pathen BOEIPA taengla mael uh laeh. Te daengah ni nangmih aka sueng rhoek te Assyria manghai kut lamloh loeihnah la a mael eh.
Molamulidwa ndi mfumu, amithenga anapita mu Israeli yense ndi Yuda ndi makalata ochokera kwa mfumu ndi kwa akuluakulu ake, olembedwa kuti, “Aisraeli bwererani kwa Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Israeli, kuti abwerere kwa inu amene mwatsala, amene mwapulumuka mʼdzanja la mafumu a ku Asiriya.
7 A napa rhoek kah Pathen BOEIPA taengah boe aka koek na pa rhoek neh na manuca rhoek bangla om uh boeh. Te dongah amih te na hmuh uh bangla imsuep la a khueh.
Musakhale ngati makolo anu ndi abale anu, amene anali osakhulupirika kwa Yehova Mulungu wa makolo awo kotero kuti anawachititsa kuti akhale chinthu chochititsa mantha, monga mukuoneramu.
8 Tahae atah na pa rhoek bangla na rhawn te mangkhak sak uh boeh. BOEIPA taengah kut duen uh laeh. Kumhal hamla a ciim tangtae a rhokso kungla ha mop uh lamtah na Pathen BOEIPA taengah thothueng uh. Te daengah ni a thintoek thinsa te nangmih taeng lamloh a mael eh.
Musawumitse khosi monga anachitira makolo anu, Gonjerani Yehova. Bwerani ku malo opatulika, amene anawapatula kwamuyaya. Tumikirani Yehova Mulungu wanu kuti mkwiyo wake ukuchokereni.
9 BOEIPA taengla na mael uh mak atah na manuca rhoek neh na ca rhoek khaw, amih aka sol rhoek kah mikhmuh ah haidamnah la, te phoeiah he khohmuen la ha mael ni. Nangmih kah Pathen BOEIPA tah lungvatnah neh thinphoei la a om dongah a taengla na mael uh atah nangmih taeng lamloh maelhmai mangthong mahpawh,” a ti nah.
Ngati inu mubwerera kwa Yehova, pamenepo abale anu ndi ana anu adzachitiridwa chifundo ndi amene anawagwira ukapolo ndipo adzabwereranso ku dziko lino pakuti Yehova, Mulungu wanu ndi wokoma mtima ndi wachifundo. Iye sadzakufulatirani ngati inuyo mubwerera kwa Iye.”
10 Te phoeiah ca thak la aka om rhoek te khopuei lamloh khopuei khat hil, Ephraim neh Manasseh khohmuen neh Zebulun duela cet uh. Tedae amih aka nueih thil neh amih aka tamdaeng la om uh.
Amithenga aja anapita mzinda ndi mzinda wa ku Efereimu ndi Manase mpaka ku Zebuloni, koma anthu anawanyoza ndi kuwachita chipongwe.
11 Te cakhaw Asher lamkah, Manasseh neh Zebulun lamkah hlang rhoek tah kunyun uh tih Jerusalem la pawk uh.
Komabe anthu ena a ku Aseri, Manase ndi Zebuloni anadzichepetsa ndipo anapita ku Yerusalemu.
12 BOEIPA ol dongah manghai neh mangpa rhoek olpaek te vai sak ham, amih te lungbuei pakhat la khueh sak ham te Pathen kah kut tah Judah ah om bal coeng.
Dzanja la Mulungu linalinso pa anthu a ku Yuda, kuwapatsa mtima umodzi wochita zimene mfumu ndi akuluakulu ake analamula potsata mawu a Yehova.
13 A hla bae dongah tah vaidamding khotue te saii hamla pilnam loh Jerusalem ah muep tingtun uh tih hlangping khaw muep cungkuem uh.
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana mu Yerusalemu kudzachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti pa mwezi wachiwiri.
14 Te dongah thoo uh tih Jerusalem kah hmueihtuk te a khoe uh. Hlupnah hnopai boeih te khaw a khoe uh tih Kidron soklong la a voeih uh.
Anachotsa mu Yerusalemu maguwa ofukizira lubani ndipo anakawaponya mʼchigwa cha Kidroni.
15 A hla bae dongkah hnin hlai li vaengah tah Yoom te a ngawn uh. Te vaengah khosoih rhoek neh Levi rhoek tah a hmaithae uh. Te dongah a ciim uh phoeiah hmueihhlutnah te BOEIPA im la a khuen uh.
Iwo anapha mwana wankhosa wa Paska pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Ansembe ndi Alevi anachita manyazi ndipo anadziyeretsa ndi kubweretsa nsembe zopsereza ku Nyumba ya Yehova.
16 Pathen kah hlang Moses olkhueng dongkah a laitloeknah bangla amamih paihmuen ah pai uh. Khosoih rhoek loh Levi kut lamkah thii te a haeh uh.
Ndipo anakhala mʼmalo awo a nthawi zonse potsatira zolembedwa mʼmalamulo a Mose munthu wa Mulungu. Ansembe anawaza magazi amene anawapatsa Alevi.
17 Hlangping lakli ah aka ciim uh pawt khaw muep om. Te dongah aka cim pawt boeih kah Yoom ngawnnah ham neh BOEIPA taengah ciim ham te Levi rhoek loh a hut nah.
Popeza ambiri mʼgululo anali asanadziyeretse, Alevi anapha ana ankhosa a Paska a iwo amene, mwa mwambo, anali osayeretsedwa ndipo sakanatha kupereka ana ankhosa awo kwa Yehova.
18 A puehkan la pilnam aka ping Ephraim, Manasseh, Issakhar neh Zebulun lamkah tah caihcil uh pawt sitoe cakhaw a daek tangtae neh kalthalh la Yoom a caak uh. Tedae Hezekiah loh amih ham thangthui tih, “BOEIPA aw, a then la dawth pah mai saeh.
Ngakhale kuti ambiri mwa anthu ochokera ku Efereimu, Manase, Isakara ndi Zebuloni sanadziyeretse okha, komabe anadya Paska motsutsana ndi zimene zinalembedwa. Koma Hezekiya anawapempherera, kunena kuti, “Yehova wabwino, khululukirani aliyense
19 Hmuencim kah ciimnah bangla om pawt cakhaw a napa rhoek kah Pathen, Yahweh Pathen te toem hamla a thinko boeih a cikngae sak,” a ti.
amene wayika mtima wake kufunafuna Yehova, Mulungu wa makolo ake, ngakhale ali wosayeretsedwa molingana ndi malamulo a malo opatulika.”
20 BOEIPA loh Hezekiah taengkah te a yaak van neh pilnam te a hoeih sak.
Ndipo Yehova anamvera Hezekiya ndipo anachiritsa anthuwo.
21 Jerusalem ah aka mop Israel ca rhoek loh hnin rhih khuiah vaidamding khotue te a saii uh. Hnin bal hnin bal BOEIPA taengah kohoenah a len neh a thangthen uh. Khosoih neh Levi rhoek loh BOEIPA te a sarhi tumbael neh a thangthenuh.
Aisraeli amene anali mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti kwa masiku asanu ndi awiri akusangalala kwambiri, pamene Alevi ndi ansembe amayimbira Yehova tsiku lililonse, akuyimbira zida zamatamando za Yehova.
22 BOEIPA kah lungmingnah then neh aka cangbam Levi pum kah lungbuei ah Hezekiah loh a thui pah. Te dongah hnin rhih tingtunnah khuiah tah rhoepnah hmueih la a nawn te a caak uh tih a napa rhoek kah Pathen BOEIPA te a uem uh.
Hezekiya anayankhula molimbikitsa Alevi onse amene anaonetsa kumvetsa bwino za kutumikira Yehova. Kwa masiku asanu ndi awiri anadya gawo lawo ndi kupereka nsembe zachiyanjano ndi kutamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo.
23 Te phoeiah hnin rhih koep saii ham te hlangping boeih loh a thui dongah kohoenah neh hnin rhih a saii uh.
Ndipo msonkhano wonse unagwirizana zopitiriza chikondwerero kwa masiku ena asanu ndi awiri. Kotero kwa masiku ena asanu ndi awiri anachita chikondwererocho mosangalala.
24 Judah manghai Hezekiah loh hlangping ham vaito thawng khat, boiva thawng rhih a pom pah. Mangpa rhoek long khaw hlangping ham te vaito thawng khat, boiva thawng rha a pom pah tih khosoih rhoek te a cungkuem la a ciim uh.
Hezekiya mfumu ya Yuda anapereka ngʼombe zamphongo 1,000 ndi nkhosa ndi mbuzi 7,000 ku msonkhanoko ndipo akuluakulu ake anapereka ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa ndi mbuzi 10,000. Ansembe ambiri anadziyeretsa.
25 Te vaengah Judah hlangping boeih khaw, khosoih neh Levi rhoek khaw, Israel lamkah aka pawk hlangping boeih neh Israel khohmuen lamkah aka pawk yinlai khaw, Judah kah khosa rhoek kaw a kohoe uh.
Gulu lonse la ku Yuda linasangalala, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ndi onse amene anasonkhana ochokera ku Israeli, kuphatikizanso alendo amene anachokera ku Israeli ndi amene amakhala ku Yuda.
26 Te dongah Jerusalem ah kohoenah a len om coeng. Israel manghai David capa Solomon tue lamloh he bang he Jerusalem ah a om noek moenih.
Munali chikondwerero chachikulu mu Yerusalemu, pakuti kuyambira masiku a Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli sizinachitikepo zotere mu Yerusalemu.
27 Levi khosoih rhoek te pai uh tih pilnam yoethen a paekuh. Amih kah thangthuinah loh a hmuencim kah khuirhung vaan duela a pha dongah amih ol te a hnatun pah.
Ansembe ndi Alevi anayimirira kudalitsa anthu, ndipo Mulungu anawamvera pakuti pemphero lawo linafika kumwamba, malo ake oyera.