< 2 Khokhuen 24 >
1 Joash te kum rhih a lo ca vaengah manghai tih Jerusalem ah kum sawmli manghai. A manu ming tah Beersheba lamkah Zihiah ni.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 Khosoih Jehoiada kah a tue khuiah tah Joash loh BOEIPA mikhmuh ah a thuem a saii.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
3 Anih ham te Jehoiada loh yuu panit a paek tih canu capa a sak.
Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
4 Te dongah a hnuk lamtah BOEIPA im te tlaih ham Joash kah lungbuei ah a om pah.
Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
5 Te phoeiah khosoih rhoek neh Levi rhoek te a coi tih amih te, “Judah khopuei rhoek la cet uh. Na Pathen im duel hamla kum khat, kum khat a rhoeh la Israel pum taengkah tangka coi uh. Nangmih te a ol bangla na tokthuet uh mai akhaw Levi rhoek tah tok boel saeh,” a ti nah.
Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
6 Manghai loh boeilu Jehoiada te a khue tih a taengah, “Olphong dap dongkah hamla BOEIPA kah sal Moses neh Israel hlangping kah buham te, Judah lamkah neh Jerusalem lamloh khuen ham te balae tih Levi taengah na toem pawh?
Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
7 Halangnu Athaliah kah a ca rhoek loh Pathen im te a muk uh coeng. BOEIPA im kah hnocim boeih khaw Baal hamla a saii uh,” a ti nah.
Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
8 Te dongah manghai loh a ti bangla thingkawng pakhat a saii uh tih BOEIPA im poeng ben vongka ah a khueh uh.
Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
9 Te phoeiah ah tah khosoek kah Israel taeng lamloh Pathen kah sal Moses buham te BOEIPA taengla khuen ham te Judah ah khaw Jerusalem ah ol a paek uh.
Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
10 Te vaengah mangpa boeih neh pilnam boeih khaw a kohoe uh. Te dongah a khuen uh tih a thingkawng dongah a bae la a sang uh.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
11 A tue a pha vaengah tah thingkawng te Levi kut lamloh manghai kah cawhkung taengla a khuen. Amih loh tangka muep a hmuh vaengah tah manghai kah cadaek neh khosoih boeilu kah hlangtawt te ha pawk. Te vaengah thingkawng te a kong uh tih a khuen uh. Amah a hmuen la a mael puei uh tih a hnin, hnin ah te tlam te a saii uh dongah tangka khaw a cung la a tung uh.
Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
12 Te te manghai neh Jehoiada loh BOEIPA im kah thothuengnah bitat aka saii taengah a paek tih BOEIPA im a tlaih vaengkah lungto aka dae neh kutthai rhoek, BOEIPA im a duel vaengkah thi neh rhohum kutthai rhoek ham khaw a paang nah la om.
Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
13 Aka saii rhoek loh bitat a saii uh van dongah amih kut dongkah bitat tah sading la cet. Pathen im te a lan a tang bangla a thoh uh tih a duel uh.
Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
14 A khah uh phoeiah tah tangka coih te manghai neh Jehoiada mikhmuh la a khuen uh. Te te BOEIPA im kah hnopai la, thohtatnah hnopai la a saii tih yakbu, sui neh cak hnopai khaw a khuen. Te dongah Jehoiada tue khuiah tah BOEIPA im ah hmueihhlutnah aka khuen khaw phueih om.
Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
15 Jehoiada te patong tih a khohnin khaw cup coeng. A dueknah te khaw kum ya sawmthum a lo ca vaengah duek.
Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
16 Anih tah Israel khuiah khaw Pathen ham neh a im ham a then a saii dongah David khopuei ah manghai rhoek taengah a up uh.
Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
17 Tedae Jehoiada a dueknah hnukah tah Judah mangpa rhoek te cet uh tih manghai taengah bakop uh. Te vaengah manghai loh amih taengkah te a hnatun.
Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
18 A napa rhoek kah Pathen BOEIPA im te a hnoo uh tih Asherah neh muei taengah tho a thueng uh. Amih kah dumlai kongah Judah neh Jerusalem soah thinhulnah om coeng.
Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
19 Amih te BOEIPA taengla mael puei ham amih taengah tonghma rhoek a tueih tih amih te a rhalrhing sak uh akhaw hnatun uh pawh.
Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
20 Te vaengah Pathen kah Mueihla loh khosoih Jehoiada capa Zekhariah te a thing. Te dongah pilnam te a taengah a pai thil tih amih te, “Pathen loh he ni a thui. Balae tih BOEIPA kah olpaek te na poe. Te dongah na thaihtak uh mahpawh. BOEIPA te na hnoo uh dongah nangmih khaw n'hnoo van coeng,” a ti nah.
Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
21 Te dongah anih te a taeng uh tih manghai olpaek bangla BOEIPA im kah vongup ah lungto neh a dae uh.
Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
22 Zekhariah napa Jehoiada loh Joash taengah a tueng sak sitlohnah te manghai Joash loh a poek moenih. Tedae a capa te a ngawn pah tih a duek thuk vaengah tah, “BOEIPA loh hmu saeh lamtah toem nawn saeh,” a ti.
Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
23 Kum te a thoknah a pha vaengah tah Aram caem loh anih taengla cet. Judah neh Jerusalem te a kun thiluh. Te vaengah pilnam lamkah pilnam mangpa boeih te a phae uh tih amih kah kutbuem boeih te Damasku manghai taengla a pat uh.
Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
24 Aram caem te hlang a yol neh cet dae, tatthai cungkuem aka yet bangla BOEIPA loh amih kut ah a paek. A napa rhoek kah Pathen BOEIPA te a toeng uh dongah Joash soah tholhphu a suk.
Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
25 Anih taeng lamloh a khoe uh vaengah anih te boengha boengha hoeng la hnoo uh. Khosoih Jehoiada koca rhoek kah thii kongah anih te a sal rhoek loh a taeng uh tih a baiphaih dongah amah la a ngawn uh. A duek vaengah anih te David khopuei ah a up uh. Tedae manghai phuel ah a up moenih.
Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
26 Anih aka taeng rhoek tah Ammoni Shimeath capa Zabad, Moab Shimrith capa Jehozabad.
Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
27 Anih koca rhoek neh a cungkuem dongah anih kah laipuei olrhuh khaw, Pathen im a phueng te khaw, manghai rhoek kah cil neh cabu khuiah a daek uh ne. Te phoeiah a capa Amaziah te anih yueng la manghai.
Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.