< 1 Manghai 3 >
1 Solomon loh Egypt manghai Pharaoh te a masae nah. Pharaoh canu te a loh dae anih te David khopuei la a thak tih amah im neh BOEIPA im neh Jerusalem kaepvai kah vongtung a thoh te a khah hlan khuiah a om nah.
Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
2 Te vaeng tue hil BOEIPA ming ham im a sak pawt dongah pilnam loh hmuensang ah a nawn.
Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
3 Solomon loh BOEIPA te a lungnah dongah a napa David kah khosing dongah pongpa. Tedae hmuensang ah a nawn tih a phum.
Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
4 Te vaengah manghai tah hmuensang tanglue te pahoi nawn ham Gibeon la cet. Solomon loh te kah hmueihtuk dongah hmueihhlutnah thawngkhat a khuen.
Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
5 Gibeon ah tah BOEIPA te Solomon ham khoyin kah a mang ah a phoe pah. Te vaengah Pathen loh, “Bih lah, nang te balae kam paek eh?” a ti nah.
Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
6 Te dongah Solomon loh, “Namah loh na sal, a pa David taengah sitlohnah a len na tueng coeng. Anih te na mikhmuh ah oltak neh, duengnah neh, namah taengah thinko thuemnah neh pongpa coeng. Te dongah ni anih ham sitlohnah a len he na ngaithuen pah. Te phoeiah anih te tahae khohnin kah bangla a ngolkhoel dongah aka ngol capa na paek.
Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
7 “Ka Pathen, BOEIPA namah loh na sal te a pa David yueng la nan manghai sak coeng. Tedae kai camoe ca loh ka kunael ham neh ka vuenva ham ka ming moenih.
“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
8 Na pilnam lakli kah na sal loh pilnam miping na coelh te tae thai pawt tih a cung la a soep moenih.
Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
9 Te dongah na sal taengah na pilnam kah laitloek pah ham, a thae a then te a laklo ah yakming thai ham olngai lungbuei mah pae. Na pilnam miping he laitloek pah ham unim aka coeng thai eh?” a ti nah.
Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
10 Solomon loh he ol he a bih vanbangla Boeipa mikhmuh ah tah ol he voelphoeng coeng.
Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
11 Te dongah Pathen loh anih te, “He ol he nan dawt coeng tih namah ham khohnin a puh khaw nan bih moenih, namah ham khuehtawn khaw nan bih moenih, na thunkha kah hinglu khaw nan bih moenih. Namah ham tiktamnah ngai ham te yakming ham nan bih.
Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
12 Na ol bangla ka saii bitni ne. Aka cueih tih aka yakming lungbuei te nang taengah kam paek bitni ne. Namah bang namah mikhmuh ah om pawt tih nang hnukah khaw namah bang he phoe mahpawh.
Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
13 Na bih pawt te khaw nang taengah khuehtawn neh thangpomnah la kam paek ni. Na hing tue khuiah tah manghai rhoek lakli ah khaw namah bang he hlang om mahpawh.
Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
14 Na pa David a pongpa bangla ka oltlueh neh ka olpaek ngaithuen ham te ka longpuei ah na pongpa atah na khohnin khaw ka pueh ni,” a ti nah.
Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
15 Solomon a haenghang vaengah mang la tarha a om pah. Te dongah Jerusalem la mael tih ka Boeipa kah paipi thingkawng hmai ah pai. Hmueihhlutnah a khuen tih rhoepnah te a saii phoeiah a sal boeih ham khaw buhkoknah a saii.
Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
16 Te vaengah pumyoi nu rhoi te manghai taengla pawk rhoi tih a mikhmuh ah pai rhoi.
Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
17 Te phoeiah huta pakhat loh, “Aw, ka boeipa, kai neh he huta he im pakhat ah ka om rhoi tih anih neh im pakhat ah ca ka cun rhoi.
Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
18 Kai loh camoe ka cun phoeikah a hnin thum dongah he kah huta khaw camoe a cun van. Kaimih rhoi bueng coeng tih im khuikah kaimih rhoi taengah yin a om moenih. Im ah tah kaimih rhoi bueng coeng ni.
Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
19 He huta kah a capa tah khoyin ah a yalh thil tih duek.
“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
20 Te dongah khoyin bangli ah thoo tih ka capa te kamah taeng lamloh a loh. Na salnu he muelh a ti vaengah a rhang dongla a yalh sak tih a capa aka duek te kai kah rhang dongla a yalh sak.
Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
21 Mincang ah ka capa te khut ham ka thoo dae vik ana duek. Mincang ah anih te ka phatuem dae ka cun ka capa la vik ana om pawh,” a ti nah.
Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
22 Huta tloe van long khaw, “Moenih, kai capa he hing tih nang capa duek,” a ti nah. Tedae te tlam ni, “Moenih, nang capa duek, kai capa hing,” a ti rhoi tih manghai mikhmuh ah a thui rhoi.
Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
23 Te vaengah manghai loh, “He loh, 'Kai capa he hing tih nang capa duek,’ a ti. Ke long khaw, 'Pawh, nang capa duek tih kai capa la aka hing dae,’ a ti,” a ti nah.
Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
24 Te phoeiah manghai loh, “Kai taengla cunghang hang khuen,” a ti nah tih cunghang te manghai mikhmuh ah a tawn uh.
Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
25 Te phoeiah manghai loh, “Camoe aka hing te panit la saek lamtah rhakthuem te pakhat taengah, rhakthuem te pakhat taengah pae,” a ti nah.
Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
26 Te vaengah a capa aka hing huta tah a capa soah a haidamnah tloo tih manghai te a thui pah tih, “Aw ka boeipa, a hing la aka om te anih taengah pae lamtah anih te duek rhoe duek sak boel mai,” a ti nah. Tedae khat long tah, “Kai ham khaw, nang ham khaw om boel saeh, saek saeh,” a ti.
Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
27 Manghai loh a doo tih, “A hing la aka om te anih taengah pae laeh. Duek rhoe duek sak boeh, anih he a manu ni,” a ti nah.
Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
28 Manghai kah laitloeknah loh a tang te Israel pum loh a yaak vaengah manghai mikhmuh ah a rhih uh. Te vaengah laitloeknah saii ham a khui kah Pathen cueihnah te a hmuh uh.
Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.