< 1 Khokhuen 5 >
1 Israel caming Reuben koca ah amah te caming ni. Tedae a napa kah rhaenghmuen te a poeih pah dongah a caminghamsum te Israel capa Joseph koca taengla a paek. Te dongah caminghamsum kah a khuui la om voel pawh.
Ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli (iye anali woyamba kubadwa, koma atagona ndi mkazi wamngʼono wa abambo ake, ulemu wake wokhala mwana woyamba unaperekedwa kwa ana a Yosefe. Kotero iye sanalembedwe pa mndandanda wa mayina ngati mwana woyamba kubadwa,
2 Judah khaw a manuca lakli ah tah len tih amah lamloh rhaengsang cakhaw caminghamsum tah Joseph taengah ni a om.
ndipo ngakhalenso Yuda anali wamphamvu kwambiri pakati pa abale ake, ndi kuti wolamulira anachokera mwa iye, ulemu wa mwana woyamba kubadwa unaperekedwa kwa Yosefe)
3 Israel caming Reuben koca ah Enok, Pallu, Khetsron neh Karmee.
ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli ndi awa: Hanoki, Palu, Hezironi, ndi Karimi.
4 Joel koca ah, a capa Shemaiah, Shemaiah capa Gog, Gog capa Shimei.
Ana a Yoweli anali awa: Semaya, Gogi, Simei,
5 Shimei capa Maikah, Mikah capa Reaiah, Reaiah capa Baal.
Mika, Reaya, Baala,
6 Baal capa Beerah. Anih te Reuben kah a khoboei la om dae Assyria manghai Tiglathpileser loh a poelyoe.
ndiponso Beeri, amene Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri anamugwira ukapolo. Mtsogoleri wa fuko la Rubeni anali Beeri.
7 A manuca khaw amah koca ah tah a khuui la ana om van. Amih rhuirhong khuikah a lu la Jeiel, Zekhariah,
Abale awo mwa mabanja awo, potsata mndandanda wa mʼbado wawo, ndi awa: Yeiyeli, mtsogoleri, Zekariya,
8 Azaz capa Bala, Shema capa Azaz, Joel capa Shema loh Aroer neh Nebo Baalmeon duela kho a sak.
ndiponso Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoweli. Iwo ankakhala ku Aroeri mpaka ku Nebo ndi Baala-Meoni.
9 Amih kah boiva he Gilead khohmuen ah a ping pah dongah khocuk ah Perath tuiva lamloh khosoek hmoi hil kho a sak.
Iwo anakhala cha kummawa mpaka kukafika polowera mʼchipululu cha mbali ina ya Mtsinje wa Yufurate, chifukwa ziweto zawo zinaswana kwambiri mʼdziko la Giliyadi.
10 Saul tue vaengah tah Hagri taengah caemtloek a saii tih amih kut ah cungku uh. Te vaengah amih kah dap ah Gilead khocuk imdan pum ah kho a sak uh.
Pa nthawi ya Sauli anachita nkhondo ndi Ahagiri ndi kuwagonjetsa. Tsono iwo anakhala mʼmatenti a Ahagiri ku dera lonse la kummawa kwa Giliyadi.
11 Amih hmatoeng te Gad koca rhoek tih Bashan khohmuen ah Salkhah duela kho a sak uh.
Anthu a fuko la Gadi anakhala moyandikana ndi fuko la Rubeni ku Basani mpaka ku Saleka:
12 Bashan ah a lu la Joel tih a hnukthoi ah Shapham, Janai neh Shaphat om.
Mtsogoleri wawo ku Basani anali Yoweli, wachiwiri anali Safamu, kenaka Yanayi ndi Safati.
13 A napa imkhui ah a manuca rhoek tah Michael, Meshullam, Sheba, Jorai, Jakhan, Zia, Eber neh parhih louh.
Abale awo mwa mabanja awo anali awa: Mikayeli, Mesulamu, Seba, Yorayi, Yakani, Ziya ndi Eberi, onse ali asanu ndi awiri.
14 Abihail koca rhoek he Huri koca, Jaorah koca, Gilead koca, Michael koca, Jeshishai capa, Jahdo koca, Buz koca la om.
Amenewa ndiwo anali ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Giliyadi, mwana wa Mikayeli, mwana wa Yesisayi, mwana wa Yahido, mwana wa Buzi.
15 Guni koca Abdiel capa Ahi he a napa imkhui ah a lu la om.
Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, anali mtsogoleri wa banja la makolo awo.
16 Te dongah Gilead ah khaw, Bashan ah khaw a vang khui neh Sharon khocaak pum ah a hmoi duela kho a sak uh.
Fuko la Gadi linakhala ku Giliyadi, ku Basani ndi midzi yozugulira, madera onse a msipu a ku Saroni mpaka kumene amalekezera.
17 Amih boeih te Judah manghai Jotham tue ah khaw, Israel manghai Jeroboam tue ah khaw a khuui a thuep coeng.
Mayina onsewa analembedwa potsata mndandanda wa mibado yawo pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu mfumu ya Yuda ndi Yeroboamu mfumu ya Israeli.
18 Reuben koca, Gad koca, photling neh cunghang aka muk, lii aka oei, caemtloek neh aka phaep uh tih caempuei la aka pawk, Manasseh koca rhakthuem lamkah hlang, tatthai capa he thawng sawmli thawng li ya rhih sawmrhuk lo.
Mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la Manase, anali ndi anthu 44, 760 okonzeka kulowa usilikali; anthu amatupi amphamvu, amene amatha kugwiritsa ntchito chishango ndi lupanga, amene amatha kugwiritsa ntchito uta, amene anaphunzitsidwa kumenya nkhondo.
19 Te vaengah Hagri, Jetur, Naphish neh Nodab taengah caemtloek la thoo uh.
Iwo anachita nkhondo ndi Ahagiri, Yeturi, Nafisi ndi Nodabu.
20 Caemtloek vaengah khaw Pathen taengah pang uh tih amah dongah a pangtung uh dongah amih ham khaw a rhoi pah. Te dongah amih te a bom tih Hagri neh a taengkah boeih te amih kut ah a paek.
Iwowo anathandizidwa polimbana nawo ndipo Mulungu anapereka Ahagiri mʼmanja mwawo; popeza iwo anafuwulira kwa Mulungu pa nkhondopo. Iye anayankha mapemphero awo chifukwa anamudalira.
21 Amih kah boiva te a sol uh tih a kalauk thawng sawmnga, boiva thawng yahnih thawng sawmnga, laak thawng hnih, hlang kah hinglu thawng yakhat lo.
Choncho iwo analanda ziweto za Ahagiri: ngamira 50,000, nkhosa ndi mbuzi 250,000 ndi abulu 2,000. Ndiponso anagwira akapolo 100,000,
22 Pathen taeng lamkah caemtloek la a om dongah a rhok la muep cungku uh. Te dongah a vangsawn khohnin hil tah amih yueng la kho a sak uh.
enanso ambiri anaphedwa, chifukwa nkhondoyo inali ya Mulungu. Ndipo iwo anakhala mʼdzikomo mpaka pa nthawi ya ukapolo.
23 Manasseh koca hlangvang ca rhoek khaw khohmuen ah Bashan lamloh Baalhermon hil kho a sak uh. Senir neh Hermon tlang ah khaw amih te ping uh.
Theka la fuko la Manase linkakhala ku dziko la kummawa kuyambira ku Basani mpaka ku Baala-Herimoni, kumene ndi ku Seniri (Phiri la Herimoni) ndipo anthuwo anali ochuluka kwambiri.
24 A napa rhoek kah imkhui kah a lu he tah, Epher, Ishi, Eliel, Azriel, Jeremiah, Hodaviah, Jahdiel. He tah a napa rhoek imkhui kah a lu la aka om hlang neh tatthai hlangrhalh hlang kah a ming ni.
Atsogoleri a mabanja awo anali awa: Eferi, Isi, Elieli, Azirieli, Yeremiya, Hodaviya ndi Yahidieli. Iwo anali asilikali olimba mtima, anthu otchuka, ndiponso atsogoleri a mabanja awo.
25 Tedae a napa rhoek kah Pathen taengah boe a koek uh tih Pathen loh amih mikhmuh lamkah a mitmoeng sak khohmuen pilnam kah pathen roek taengla cukhalh uh.
Koma iwo anali osakhulupirika kwa Mulungu wa makolo awo ndipo anadzipereka okha kwa milungu ya anthu okhala mʼdzikomo amene Mulungu anawawononga pamene iwowo ankafika.
26 Te dongah Israel Pathen loh Assyria manghai Pul kah mueihla neh Assyria manghai Tiglathpileser kah mueihla te a haeng pah. Te vaengah amih, Reuben neh Gad, Manasseh koca hlangvang te a poelyoe. Te phoeiah amih te Halah, Habor, Hara neh tahae khohnin hil Gozan tuiva la a khuen.
Kotero Mulungu wa Israeli anayika mkwiyo mwa Puli mfumu ya Asuri (ameneyu ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri) amene anatenga fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase kupita nawo ku ukapolo. Iye anapita nawo ku Hala, Habori, Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, kumene ali mpaka lero lino.