< Rom 14 >

1 Tangnah aka vawtthoek te doe uh lamtah poeknah neh boelhkhoehnah te khueh boeh.
Mulandire amene ndi ofowoka mʼchikhulupiriro, osatsutsana naye pa maganizo ake.
2 Pakhat long ngawn tah boeih caak ham a tangnah. Tedae tattloel long tah toian a caak.
Chikhulupiriro cha munthu wina chimamulola kudya china chilichonse koma munthu wina, amene chikhulupiriro chake ndi chofowoka, amangodya zamasamba zokha.
3 Aka ca loh aka ca pawt te hnaelcoe boeh. Aka ca pawt long khaw aka ca te kamkaih boeh. Anih te khaw Pathen loh a doe coeng.
Munthu amene amadya chilichonse sayenera kunyoza amene satero, ndipo munthu amene samadya chilichonse asaweruze munthu amene amatero, pakuti Mulungu anamulandira.
4 Nang tah metlam na om aih tih hlanglang kah imkhut te na coel? Anih te a boei hut la pai tih yalh ta. Tedae Boeipa loh anih te a thoh thai dongah pai ngawn ni ta.
Kodi ndiwe ndani kuti uweruze wantchito wamwini? Mbuye wake yekha ndiye aweruze ngati iye wakhoza kapena walephera pa ntchito yake. Ndipo adzakhoza popeza kuti Mbuye wake angathe kumukhozetsa.
5 Te dongah pakhat loh khohnin pakhat lakah khohnin pakhat te a poek. Tedae pakhat loh khohnin boeih he tanglue la a poek. Pakhat rhip loh amah lungbuei ah tangnah saeh.
Munthu wina amayesa tsiku limodzi lopatulika kuposa lina. Munthu wina amayesa masiku onse ofanana. Aliyense akhale otsimikiza mʼmaganizo ake.
6 Khohnin aka yaeh loh Boeipa ham a yaeh tih aka ca loh boeipa ham a caak dongah Pathen te a uem. Aka ca pawt long khaw Boeipa ham a caak pawt dongah Pathen te a uem.
Iye amene amaganiza kuti tsiku limodzi ndi lopambana, amatero kwa Ambuye. Iye amene amadya nyama, amadya mwa Ambuye pakuti amayamika Mulungu. Ndipo iye amene sadya, amatero kwa Ambuye ndi kuyamika Mulungu.
7 Te dongah amah ham aka hing he mamih ah om pawt tih amah ham aka duek khaw om pawh.
Pakuti palibe wina wa ife amene amakhala moyo pa yekha ndiponso palibe wina wa ife amene amafa pa yekha.
8 N'hing uh atah Boeipa ham n'hing uh tih n'duek uh atah Boeipa ham n'duek uh. Te dongah hing akhaw duek akhaw Boeipa kah hut la n'om uh.
Ngati ife tikhala ndi moyo, ife tikhala ndi moyo kwa Ambuye. Ndipo ngati ife tifa, tifa kwa Ambuye. Choncho, ngati tikhala ndi moyo kapena kufa, ndife ake a Ambuye.
9 Te ham te Khrih duek tih hing coeng. Te daengah ni aka duek neh aka hing kah boei la bok a om eh.
Pa chifukwa ichi, Khristu anafa ndi kuukanso kotero kuti Iye akhale ndi Ambuye wa akufa ndi amoyo.
10 Te koinih nang tah balae tih na manuca te na kamkaih. Nang tah balae tih na manuca te na hnaelcoe. Mamih boeih tah Pathen kah ngolkhoel ah m'pai uh ni.
Tsono nʼchifukwa chiyani iwe ukuweruza mʼbale wako? Kapena nʼchifukwa chiyani ukumunyoza mʼbale wako? Pakuti ife tonse tidzayima pa mpando wakuweruza wa Mulungu.
11 A daek vanbangla Boeipa loh, “Kai tah ka hing. Te dongah Hlang boeih loh kai taengah khuklu cungkueng saeh lamtah olka boeih loh Pathen ming te phong saeh,” a ti.
Kwalembedwa, akutero Ambuye, “Pamene Ine ndili ndi moyo, aliyense adzandigwadira ndipo lilime lililonse lidzavomereza Mulungu.”
12 Te dongah mamih khat rhip loh amah amah kah lannah te Pathen taengah a paek tangloeng ni.
Choncho tsopano, aliyense wa ife adzafotokoza yekha kwa Mulungu.
13 Te dongah khat neh khat soah laitloek uh thae boel sih. Tedae manuca taengah caehkoek neh thangkui khueh pawt ham he mah laitloek uh.
Motero, tiyeni tisiye kuweruzana wina ndi mnzake. Mʼmalo mwake, tsimikizani mʼmaganizo anu kuti musayike chokhumudwitsa kapena chotchinga mʼnjira ya mʼbale wanu.
14 Amah ah aka tanghnong he om pawh tila Boeipa Jesuh ah ka ngaitang tih ka ming dae khat khat loh mebang khaw tanghnong a ti atah anih ham tanghnong la om ni.
Monga mmodzi amene ndili mwa Ambuye Yesu, ndine wotsimikiza mtima kuti palibe chakudya chimene pachokha ndi chodetsedwa. Koma ngati wina atenga china chake kukhala chodetsedwa, kwa iyeyo ndi chodetsedwa.
15 Caak rhangneh na manuca te a khothet atah lungnah neh na caeh moenih. Anih ham aka duek Khrih te nang kah cakok neh na poci sak ham moenih.
Ngati mʼbale wako akuvutika chifukwa cha chimene umadya, iwe sukuchitanso mwachikondi. Usamuwononge mʼbale wako amene Khristu anamufera chifukwa cha chakudya chakocho.
16 Te dongah nangmih ham aka then tah soehsal boeh.
Musalole kuti chimene muchiyesa chabwino achinene ngati choyipa.
17 Pathen kah ram tah caak neh ook dongah pawt tih duengnah, rhoepnah, Mueihla Cim ah omngaihnah dongah ni a om.
Pakuti Ufumu wa Mulungu si nkhani yakudya ndi kumwa, koma chilungamo, mtendere ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera.
18 Te dongah he nen he Khrih kah sal aka bi tah Pathen ham kolonah neh hlang ham ueppang koi la om.
Nʼchifukwa chake aliyense amene atumikira Khristu mʼnjira iyi akondweretsa Mulungu ndi kuvomerezedwa ndi anthu.
19 Te dongah rhoepnah koi neh khat neh khat ham hlinsainah koi te hnuktlak uh tangloeng sih.
Tsono tiyeni tiyesetse kuchita zimene zidzabweretsa mtendere ndi kulimbikitsana mwachikondi.
20 Caak ham dawk neh Pathen kah bibi te phae boeh. A cungkuem he caih ngawn dae caak rhangneh hlang ham caehkoek la a om te thae.
Musawononge ntchito ya Mulungu chifukwa cha chakudya. Chakudya chonse ndi choyera, koma munthu amalakwa ngati adya chilichonse chimene chimakhumudwitsa wina.
21 Maeh caak pawt khaw, misurtui a ok ham pawt rhangneh na manuca loh a tongtah pawt te then.
Nʼkwabwino kusadya kapena kumwa vinyo kapena kuchita chilichonse chimene chidzachititsa mʼbale wako kugwa.
22 Nang namah loh tangnah na khueh te Pathen hmaiah khueh. Amah loh a soepsoei tangtae te lai aka tloek thil pawt tah a yoethen.
Tsono zimene ukukhulupirira pa zinthu izi zikhale pakati pa iwe ndi Mulungu. Wodala munthu amene sadzitsutsa yekha pa zimene amazivomereza.
23 Tedae a boelhkhoeh tih a caak atah tangnah lamkah pawt dongah boe coeng. Te dongah tangnah lamkah pawt boeih te tah tholhnah ni.
Koma munthu amene akukayika atsutsidwa ngati adya, chifukwa kudya kwake si kwa chikhulupiriro; ndipo chilichonse chosachokera mʼchikhulupiriro ndi tchimo.

< Rom 14 >