< Tingtoeng 68 >
1 Aka mawt ham David kah tingtoeng laa Pathen he thoo vetih a thunkha rhoek taekyak uh mako. A lunguet rhoek khaw a mikhmuh lamkah rhaelrham uh mako.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
2 Halang rhoek he Pathen hmai ah hmaikhu a yah bangla na yah vetih, hmai hmai ah khoirhat a paci bangla milh uh saeh.
Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
3 Tedae hlang dueng rhoek tah kohoenah neh Pathen hmai ah a sundaep neh a kohoe uh saeh lamtah ngaingaih uh saeh.
Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
4 Pathen te hlai lamtah a ming te tingtoeng uh lah. Vaan kolken dongah aka ngol BOEIPA ming te pomsang uh lamtah a hmai ah sundaep uh.
Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
5 Amah kah khuirhung hmuencim ah aka om Pathen tah cadah rhoek kah a napa neh nuhmai rhoek kah laitloekkung la om.
Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
6 Pathen loh oingaih cangloeng te imlo neh kho a sak sak tih thongtla rhoek te lolmangcil neh a khuen. Tedae thinthah rhoek tah rhamrhae ah kho a sakuh.
Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
7 Pathen aw na pilnam hmai ah na caeh vaengah, khopong la na luei vaengah. (Selah)
Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
8 Israel Pathen, Pathen hmai ah, Sinai Pathen hmai ah, diklai he hinghuen tih vaan khaw cip.
dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
9 Pathen namah loh kothoh khonal nan suep tih thahnoeng khaw na rho neh na thoh.
Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 Pathen nang loh mangdaeng ham na hnothen te na soepboe pah tih a khuiah na hingnah loh kho a sakuh.
Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
11 Ka Boeipa loh a olkhueh te a paek tih olthangthen aka phong caempuei khaw len.
Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
12 Manghai rhoek kah caempuei loh yong rhoela yong uh tih im kah toitlim te kutbuem la a tael.
“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
13 Tuvong ah na yalh uh vaengkah te, cak neh a hluk vahui phae, sui hing neh a hluk phaemul van pawn ni.
Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
14 Tlungthang Pathen loh a khuikah manghai rhoek a taek a yak vaengah Zalmon ah vuel bo.
Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
15 Pathen kah tlang, Bashan tlang, Bashan tlang kah tlang som rhoek,
Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
16 Ba dongah tlang som rhoek loh na pangoe uh. Te kah tlang te Pathen Amah loh khosak thil ham a nai tih BOEIPA loh yoeyah la kho a sak thil ni.
Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
17 Pathen kah leng tah a rhaepnah thawng thawngrha lo. Hmuencim kah aka om Sinai kah amih lakli ah Boeipa om.
Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
18 Hmuen sang la na luei tih tamna rhoek na sol vaengah BOEIPA Pathen namah loh khosak puei ham hlang taeng neh thinthah rhoek taengkah kutdoe pataeng na doe.
Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
19 Ka Boeipa tah a hnin, hnin ah a yoethen pai saeh. Mamih kah khangnah Pathen tah mamih ham thinrhih coeng. (Selah)
Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 Mamih kah Pathen tah khangnah Pathen la om tih, ka Boeipa Yahovah taengah dueknah lamkah longrhael khaw om.
Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
21 Amah kah tholhnah neh aka pongpa tah Pathen loh thunkha lu bangla a luki sam soah a phop ni.
Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
22 Ka Boeipa loh, “Bashan lamkah kam bal puei vetih tuitunli kah a laedil lamkah kam mael puei ni.
Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
23 Te vaengah thunkha lamkah thii na kho na nuem thil, te na ui rhoek loh a lai neh a laeh uh vetih amih kah rhuimal khaw na pang uh ni,” a ti.
Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
24 Pathen namah kah lambong rhoek, ka Pathen, ka manghai kah lambong rhoek loh hmuencim la a khong uh te a hmuh uh coeng.
Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
25 Laa sa rhoek loh lamhma uh tih a hnukthoi loh a tumbael a tum, a laklung kah hula rhoek loh toemrhang a tum uh.
Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
26 Pathen te khangkhung lakli ah, BOEIPA te Israel thunsih ah uem lah.
Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
27 Canoi Benjamin loh Judah mangpa hlangkuk rhoek, Zebulun mangpa rhoek, Naphtali mangpa rhoek te a taemrhai.
Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
28 Pathen namah loh na sarhi te uen lamtah kaimih ham na saii bangla Pathen namah te mah tanglue lah.
Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
29 Na bawkim rhang neh manghai rhoek loh nang ham kutdoe te Jerusalem la hang khuen uh ni.
Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
30 Capu mulhing ke tluung lah. Pilnam saelca rhoek neh aka lueng rhaengpuei khaw cak boeng neh a san thil. Caemrhal aka ngaih pilnam rhoek khaw a haeh.
Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
31 Egypt lamkah laipai rhoek halo uh ni. Kusah loh Pathen taengah a kut a duen ni.
Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
32 Diklai ram rhoek loh Pathen te hlai uh lamtah ka Boeipa te tingtoeng uh. (Selah)
Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
33 Hlamat lamkah vaan dong vaan dongah aka ngol loh a ol neh sarhi ol a paek coeng ke.
Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
34 Pathen kah sarhi te doek uh lah. A hoemnah neh khomong dongkah a sarhi tah Israel soah om.
Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
35 Pathen namah kah rhokso ah a rhih om pai. Israel Pathen amah loh pilnam taengah sarhi neh thadueng a paek. Pathen tah a yoethen pai saeh.
Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!