< Tingtoeng 56 >

1 Aka mawt ham Gath ah Philisti loh amah a khoh vaengkah David kah lakhla olmueh vahui laa Kho hnin takuem kai aka nen la aka nen, hlanghing loh kai n'hloem dongah, Pathen aw kai n'rhen dae.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
2 Ka lungawn rhoek loh khohnin takuem n'hloem uh tih, kai he koevoeinah neh aka nen khaw yet.
Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
3 Kai loh ka rhih khohnin ah, namah dongla ka pangtung.
Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
4 Pathen rhang neh amah kah olka te ka thangthen. Pathen dongah ka pangtung tih ka rhih mahpawh. Pumsa loh kai taengah balae a saii thai.
Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
5 Khohnin yung ah kai ol a yakdam uh tih a kopoek boeih khaw kai taengah thae uh.
Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
6 Amih loh ka kholaeh te, a dawn a dawn uh tih m'mae uh. Ka hinglu he a lamtawn uh dongah n'tawt uh.
Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
7 Amih kah boethae ah na thintoek loh pilnam rhoek a hlak te hlawt la om saeh saw Pathen aw.
Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
8 Ka poengdoenah he namah loh tae lamtah, ka mikphi he na tuitang khuiah than lah. Na cabu dongah om pawt nim?
Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
9 Te dongah amah te ka khue khohnin kah, ka thunkha rhoek a bal uh nen te, kai ham Pathen om tila ka ming ni.
Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
10 Pathen rhang neh olka te ka thangthen. BOEIPA rhang neh olka te ka thangthen.
Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
11 Pathen dongah ka pangtung dongah ka rhih mahpawh. Hlang loh kai taengah balae a saii thai?
mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
12 Aw Pathen, kai sokah na olcaeng ham, nang taengah uemonah neh kan thuung ni.
Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
13 Dueknah lamkah ka hinglu nan huul phoeiah, Pathen mikhmuh kah hingnah khosae ah caeh ham ka kho he thuihkoek lamkah han hlawt moenih a?
Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.

< Tingtoeng 56 >