< Tingtoeng 28 >

1 David kah Kai kah lungpang, BOEIPA nang te kan khue. Kai taengah olmueh boeh. Kai hamla na ngam vetih tangrhom ah aka suntlak neh n'thuidoek ve.
Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2 Nang taengah ka pang vaengah, namah hmuencim kah cangimphu benla kut ka dawn vaengah ka huithuinah ol he han ya lah.
Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3 Halang tih boethae aka saii rhoek neh kai he hmaih n'sol boeh. A hui taengah rhoepnah a thui dae a thinko khuiah thae.
Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4 Amih a bisai neh a khoboe thaenah vanbangla amih ham khueh pah. A kut bibi vanbangla amih neh aka tiing te hmoel lamtah amih taengah pae.
Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5 BOEIPA kah thaphu neh a kut dongkah bibi a yakming uh pawt dongah amih te a koengloeng vetih koep suem mahpawh.
Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
6 Ka huithuinah ol a yaak dongah BOEIPA te a yoethen saeh.
Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7 BOEIPA tah ka sarhi neh ka photling ni. Amah te ka lungbuei loh a pangtung tih n'bom dongah ka lungbuei sundaep. Te dongah ka laa neh amah te ka uem ni.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8 BOEIPA tah amih kah sarhi neh, a koelh hlang kah khangnah lunghim ni.
Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9 Na pilnam te khang lamtah na rho te a yoethen saeh. Amih te luem puei lamtah amih te kumhal duela phuei lah.
Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

< Tingtoeng 28 >