< Tingtoeng 137 >
1 Babylon tuiva ah te ka ngol uh tih Zion ka poek uh vaengah ka rhap uh.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 A khui kah tuirhi dongah ka rhotoeng te ka bang uh.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 Kaimih aka sol rhoek kaimih te laa ol hnap n'dawt uh. Kaimih aka parhaengkung long khaw, “Zion laa te kaimih ham kohoenah neh hlai uh lah,” a ti uh.
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Balae tih BOEIPA laa he kholong kho ah ka hlai uh eh?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Jerusalem nang te kan hnilh atah ka bantang kut he hnilh uh saeh.
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Nang te kan thoelh pawt tih, Jerusalem te ka kohoenah somtung la ka pacuet pawt atah ka lai he ka dang la kap uh saeh.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 BOEIPA aw Jerusalem tue vaengkah Edom koca rhoek loh, “A khoengim duela kingling uh kingling uh,” a ti uh te poek pah.
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 Hlang aka rhoelrhak Babylon nu aw, kaimih taengah na saii bangla na thaphu te namah taengah aka thuung tah a yoethen.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Na camoe rhoek te a tuuk tih, thaelpang dongah aka phop tah a yoethen.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.