< Tingtoeng 105 >

1 BOEIPA te uem uh lah. A ming te khue uh lah. A khoboe te pilnam rhoek taengah tukkil uh lah.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Amah te hlai uh lah. Amah te tingtoeng uh lamtah amah kah khobaerhambae boeih te lolmang taeng uh lah.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 A ming cim neh thangthen uh lamtah, BOEIPA aka tlap rhoek kah a lungbuei tah a kohoe saeh.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 BOEIPA neh amah kah a sarhi te tlap lah. A maelhmai khaw tlap taitu lah.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 A kopoekrhainah a saii neh a ka dongkah laitloeknah bangla anih khobaerhambae khaw,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 A sal Abraham tiingan neh a coelh Jakob koca rhoek loh thoelh uh lah.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 BOEIPA amah ni mamih kah Pathen coeng. A laitloeknah khaw diklai pum ah om.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 A paipi tekumhal duela a thoelh dongah cadilcahma thawngkhat ham olka a uen.
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 Abraham neh Isaak taengah a saii a olhlo te,
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 Jakob taengah oltlueh la, Israel taengah kumhal paipi la a sut pah.
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 Te dongah, “Kanaan kho rhi te na rho la nang taengah kam paek ni,” na ti nah.
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 A hlang kah hlangmi te a sii la om pueng tih, a khuiah bakuep uh.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Te vaengah namtom taeng lamkah namtom taengla, ram pakhat lamkah pilnam pakhat taengla poengdoe uh.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Amih aka hnaemtaek ham hlang khueh pah pawt tih amih kongah manghai rhoek khaw a tluung pah.
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 Ka koelh soah ben boel lamtah ka tonghma rhoek te thaehuet thil boeh,” a ti nah.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Khokha a khue vaengah kho khuiah conghol neh caak boeih te a phae pah.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Amih hmai kah a tueih hlang, Joseph te sal bangla a yoih.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 A kho te hlong neh a phaep pah uh a hinglu ah thicung loh a toeh.
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 A olthui a thoeng tue a pha due BOEIPA kah olthui loh ol loh anih te a cil a poe.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Manghai loh a tah dongah pilnam aka taem loh anih a doek tih a hlah.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Amah im kah boei neh a hnopai boeih aka taemrhai hamla,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 A hinglu bangla a mangpa rhoek te khoh tih a hamca rhoek te cueih sak ham te a khueh.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Te vaengah Israel loh Egypt la kun tih Jakob loh Ham kho ah bakuep.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Tedae a pilnam te muep a pungtai sak tih a rhal rhoek lakah a yet sak.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 BOEIPA loh a sal rhoek te rhaithi sak tih, a pilnam aka hmuhuet ham Egypt rhoek kah lungbuei te a maelh pah.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 A sal Moses neh anih ham a coelh Aron te a tueih.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Amih rhoi loh Egypt rhoek taengah Boeipa kah miknoek olka a tueng sak rhoi tih, Ham kho ah khaw kopoekrhai hno te a tueng sak rhoi.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Khohmuep a tueih tih a hmuep sak dongah Boeipa kah olthui olka te koek uh thai pawh.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 A tui te thii la a poeh sak tih a nga khaw a duek sak.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 A kho kah bukak rhoek te a manghai rhoek kah imkhui la a khae sak.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Amah loh a uen tih a khorhi tom ah pil neh pilhlip uihli tlung.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Khonal te rhael la a poeh sak tih a kho ah hmaisai hmai la coeng.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 A misur neh a thaibu te khaw a haih pah tih a khorhi kah thing te a khaem pah.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 A uen bal tih kaisih neh lungang te tae na pawt la halo.
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 Te vaengah a kho kah baelhing boeih a caak tih a khohmuen kah a thaihtae khaw a caak pah.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 A kho khuikah caming boeih neh a thahuem boeih khuikah a thaihcuek te a ngawn pah.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Te vaengah amih te cak neh, sui neh ham pawk puei dongah amah koca rhoek khuikah tah paloe pawh.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Amih Egypt rhoek te birhihnah loh a vuei tih amih rhoek a nong vaengah a kohoe uh.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Himbaiyan bangla cingmai a yaal pah tih khoyin ah hmai a vang pah.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 A bih vaengah tanghuem a khuen pah tih vaan kah buh te amih a kum sak.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Lungpang a ong vaengah tui ha phuet tih rhamrhae ah tuiva la a long sak te,
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 a sal Abraham taengkah a olkhueh cim te a poek dongah ni.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 A pilnam khaw omngaihnah tamlung a coelh neh a khuen.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Te vaengah namtu rhoek kah a thakthaenah namtom khohmuen te a paek tih a pang uh te,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 a oltlueh ngaithuen sak ham neh a olkhueng te kueinah sak ham ni. BOEIPA te thangthen lah.
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Tingtoeng 105 >