< Maikah 6 >
1 BOEIPA loh a thui te hnatun uh laeh. Thoo tlang te ho laeh. Na ol te som long khaw ya saeh.
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 Tlang rhoek neh diklai yung cak loh BOEIPA kah tuituknah te hnatun saeh. BOEIPA kah tuituknah he a pilnam taeng neh Israel taengah a thui coeng.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 Ka pilnam nang taengah balae ka saii tih nang te metlam kang ngae? Kamah taengah thui lah.
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 Nang te Egypt kho lamloh kang khuen tih sal rhoek imkhui lamloh nang kan lat. Na mikhmuh ah Moses, Aaron neh Miriam kan tueih.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 Ka pilnam aw, Moab manghai Balak loh a uen te khaw, Beor capa Balaam loh anih a doo te poek uh laeh. Te daengah ni Shittim lamloh Gilgal duela BOEIPA kah duengnah a ming.
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 Ba nen lae BOEIPA ka doe vetih hmuensang Pathen taengah ka duengyai eh. Amah te hmueihhlutnah neh, sael kum khat ca nen a ka doe eh?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 BOEIPA loh tutal thawngkhat neh, situi soklong thawngrha nen khaw a moeithen aya? Ka caming te ka boekoeknah dongah, ka bungko thaihtae te ka hinglu kah tholhnah dongah ka paek thai aya?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 Hlang nang taengah melae aka then, nang kah te BOEIPA loh balae a toem ti khaw, tiktamnah te rhep saii ham khaw, sitlohnah te lungnah ham khaw, na Pathen taengah kodo la pongpa ham khaw ha puen coeng.
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 BOEIPA ol tah khopuei taengah pang coeng. Lungming cueihnah tah na ming te a hmuh. Hnatun uh lah, caitueng neh unim a tuentah coeng?
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Halang im neh halangnah thakvoh te hlihloeh tih cangnoek pawtrhawt te kosi a hong thil pueng aya?
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Halangnah cooi ham neh hlangthai palat kah coilung sungsa te ka cim sak aya?
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 A hlanglen rhoek kongah kuthlahnah cung uh tih a khuikah khosa rhoek loh a honghi a thui uh. A ol tah a ka ah palyal uh mai.
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Te dongah nang ngawn ham neh na tholhnah dongah nang pong sak ham kai loh kantloh sak.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Na caak akhaw na hah hae pawt vetih na pongnah he na ko khuiah om ni. Na balkhong dae na loeih hae mahpawh. Na loeih cakhaw cunghang taengla ka paek ni.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Na tuh dae na at mahpawh. Olive te na neet cakhaw situi na hluk hae mahpawh. Misur thai na khueh akhaw misurtui na o mahpawh.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Omri kah khosing neh Ahab imkhui kah khoboe boeih te a dawn coeng. Amih kah cilkhih dongah na pongpa uh. Te dongah ni kai loh nang te imsuep la kang khueh. Tedae rhoek khosa rhoek kah thuithetnah neh ka pilnam kah kokhahnah ni na phueih uh eh.
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”