< Luka 11 >
1 Amah a om vaengah a tue a pha tih hmuen pakhat ah thangthui. A thangthui bawt ah, a hnukbang pakhat loh Jesuh taengah, “Boeipa, kaimih he thangthui ham n'thuituen lah, Johan long khaw a hnukbang rhoek te a thuituen van,” a ti nah.
Tsiku lina Yesu amapemphera pamalo ena. Atamaliza, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Ambuye tiphunzitseni kupemphera, monga momwe Yohane anaphunzitsira ophunzira ake.”
2 Te dongah amih te, “Na thangthui uh vaengah, 'A pa na ming tah ciim pai saeh, na ram pai saeh.
Yesu anawawuza kuti, “Pamene mukupemphera muzinena kuti: “‘Atate, dzina lanu lilemekezedwe, ufumu wanu ubwere.
3 Khohhnin rhamhnin kaimih kah buh he amah khohnin ah kaimih m'pae lah.
Mutipatse chakudya chathu chalero,
4 Kaimih kah tholhnah soah kaimih he n'hlah lah, kaimih khaw kaimih taengah laiaka ba boeih te ka hlah uh van dongah. Cuekhalhnah khuila kaimih n'khuen boeh, 'ti uh,” a ti nah.
mutikhululukire machimo athu, monga ifenso timakhululukira aliyense amene watilakwira. Ndipo musalole kuti tigwe mʼmayesero.’”
5 Te phoeiah amih te, “Nangmih khuikah pakhat loh paya a khueh tih, ihdulh ah anih taengla cet mai ni. Te vaengah anih te, 'Ka paya, vaidam pa thum ah kai m'pu dae.
Kenaka anawawuza kuti, “Tiyerekeze: Mmodzi mwa inu atakhala ndi bwenzi lake, ndipo iye nʼkupita ku nyumba yake pakati pa usiku, nakanena kuti, ‘Mnzanga, bwereke malofu atatu abuledi,
6 Ka paya yin lamkah kai taengla ha pawk tih, anih ham ka tawn pah khaw ka khueh pawh,’ a ti nah.
chifukwa ndalandira bwenzi langa amene ali pa ulendo ndipo ine ndilibe choti ndimupatse.’
7 Te long khaw a khuiah a doo tih, 'Thakthaenah nen khaw kai n'toeh boeh. Thohka a khaih coeng, ka taengkah ka ca rhoek khaw ihnah dongla om uh coeng, nang paek ham ka tho thai mahpawh,’ a ti nah ni.
“Ndipo yerekezani kuti amene ali mʼnyumbamo ndi kuyankha kuti, ‘Usandivutitse ine, ndatseka kale chitseko, ndipo ine ndi ana anga tagona. Ine sindingadzukenso kuti ndidzakupatse.’
8 Nangmih taengah ka thui, anih te a paya la a om dongah thoo cakhaw pae mai mahpawh. Tedae a paya te a calaak coeng atah thoo vetih a kuek yet te a paek ni.
Ine ndikukuwuzani kuti adzadzuka ndi kumupatsa bulediyo, osati chifukwa ndi bwenzi lake, koma chifukwa cha liwuma la munthu wopemphayo, ndipo kudzamupatsa zonse zimene akuzifuna.
9 Nangmih taengah ka thui, Bih uh lamtah, nangmih tem'paek bitni, toem uh lamtah na hmuh uh bitni, khoek uh lamtah nangmih ham a ong binit.
“Choncho Ine ndikunena kwa inu kuti: Pemphani ndipo adzakupatsani. Funafunani ndipo mudzapeza. Gogodani ndipo adzakutsekulirani.
10 Aka bih loh boeih a dang tih, aka toem loh a hmuh dongah aka khoek ham khaw a ong pah ni.
Pakuti aliyense amene amapempha amalandira. Munthu amene amafunafuna amapeza. Iye amene amagogoda amamutsekulira.
11 Nangmih khuikah napa pakhat te a ca loh nga a hoe vaengah, nga yueng la rhul a doe aya?
“Ndani mwa inu abambo, kodi mwana wanu atapempha nsomba, mʼmalo mwake mungamupatse njoka?
12 Aiduei hoe koinih a ca te saelkhui-ta-ai a paek aya?
Kapena atapempha dzira, kodi mungamupatse chinkhanira?
13 Te dongah nangmih a thae la aka om long pataeng, na ca rhoek te kutdoe then paek ham na ming uh atah, vaan lamkah pa loh muep a ming ngai dongah amah aka dawt rhoek te tah Mueihla Cim a paek ni,” a ti nah.
Tsono ngati inu, anthu oyipa, mumadziwa kupereka mphatso zabwino kwa ana anu, koposa kotani Atate anu akumwamba, angalephere bwanji kupereka Mzimu Woyera kwa amene awapempha!”
14 Rhaithae om tih a haek hatah olmueh la ana poeh pah. Te dongah rhaithae te vawl a caeh daengah olmueh te koep cal tih hlangping khaw a ngaihmang.
Yesu amatulutsa chiwanda chimene chinali chosayankhula. Chiwandacho chitatuluka, munthu wosayankhulayo anayankhula, ndipo gulu la anthu linadabwa.
15 Tedae amih khuikah hlangvang loh, “Rhaithae boei Beelzebul rhangnen ni rhaithae a haek,” a ti uh.
Koma ena mwa iwo anati, “Iye akutulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu mfumu ya ziwanda.”
16 A tloe rhoek loh a noemcai uh tih vaan lamkah miknoek te anih taengah a toem uh.
Ena anamuyesa pomufunsa chizindikiro chochokera kumwamba.
17 Tedae amah loh amih kah kopoek te a ming dongah amih te, “Ram boeih he amah a paekboe atah poci tih, imkhui loh imkhui a paekboe thil atah cungku.
Yesu anadziwa maganizo awo ndipo anawawuza kuti, “Ufumu uliwonse wogawikana udzawonongeka, ndipo nyumba yogawikana idzapasuka.
18 Satan khaw amah neh amah paekboe uh koinih, metlam lae a ram a pai eh? Kai loh Beelzebul rhangneh rhaithae a haek na ti uh.
Ngati Satana adziwukira yekha, ufumu wake ungalimbe bwanji? Ine ndikunena izi chifukwa inu mukuti Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu.
19 Tedae Beelzebul rhangneh rhaithae te ka haek koinih, na ca rhoek long tah u rhangnen lae a haekuh. Te dongah amih te nangmih soah laitloekkung la om uh ni.
Tsopano ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu, nanga ophunzira anu amazitulutsa ndi mphamvu ya ndani? Choncho, iwowo ndiye adzakhala oweruza anu.
20 Tedae Pathen kah kutdawn neh rhaithae te ka haek koinih, nangmih soah Pathen kah ram ha pai coeng.
Koma ngati ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Mulungu, ndiye kuti ufumu wa Mulungu wafika pakati panu.
21 Khangmai la aka nuet uh long ni a vongup te a hung tih a khuehtawn loh ngaimong la om van.
“Munthu wamphamvu, amene ali ndi zida, akamalondera nyumba yake, katundu wake amatetezedwa.
22 Tedae anih lakah aka tlung ngai ha pawk vaengah tah anih te a noeng. Te vaengah a pangtung thil lungpok haica te a rhawt pah tih, a kutbuem a poelyoe pah.
Koma pakabwera wina wamphamvu zoposa namugonjetsa, amalanda zida zimene munthuyo amazidalirazo ndi kugawa katundu wake.
23 Kai taengah aka om pawt tah kai aka koek ni. Kai taengah aka coi pawt loh a thaek.
“Munthu amene sali mbali yanga ndi wotsutsana nane. Ndipo wosandithandiza kusonkhanitsa, ameneyo ndi womwaza.
24 Mueihla thae tah hlang taeng lamkah a nong vaengah tuihang hmuen te a hil tih duemnah a tlap. Tedae hmuen a hmuh pawt vaengah, “Ka nong tak tangtae kamah im la ka mael ni,' a ti.
“Mzimu woyipa ukatuluka mwa munthu, umakayendayenda ku malo owuma, kufunafuna malo opumulirako ndipo suwapeza. Kenaka umati, ‘Ndibwerera ku nyumba kwanga kumene ndachokera.’
25 Ha pawk vaengah, im te nawt tangtae neh a khoem la a hmuh
Ukafika umapeza mʼnyumba mosesedwa bwino ndi mokonza.
26 Te dongah cet tih amah lakah aka thae mueihla tloe parhih te a khuen. Te phoeiah a kun puei tih pahoi a om puei dongah tekah hlang kah a hnukkhueng tah lamhma kah lakah a thae la om,” a ti nah.
Pamenepo umakatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa iwowo ndipo imakalowa ndi kukhala mʼmenemo. Ndipo makhalidwe otsiriza a munthuyo amakhala oyipa kuposa oyamba aja.”
27 Te a thui vaengah hlangping khui lamkah huta pakhat loh ol a huel tih Jesuh te, “Nang aka yom bung neh aka cun rhang suk tah a yoethen,” a ti nah.
Pamene Yesu ankanena zonsezi, mayi wina mʼgulu la anthuwo anafuwula nati, “Ndi wodala amayi amene anakubalani ndi kukulerani!”
28 Tedae Jesuh loh, “Pathen ol aka ya tih aka tuem rhoek tah a yoethen ngai,” a ti nah.
Koma Yesu anayankha kuti, “Odala ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kuwasunga.”
29 Hlangping he a khawk vaengah a tong tih, “Tahae kah cadil tah rhaithae cadil ni, Miknoek te a toem uh dae Jonah kah miknoek pawt atah miknoek pae mahpawh.
Pamene gulu la anthu limachuluka, Yesu anati, “Uno ndi mʼbado oyipa. Umafuna kuona chizindikiro chodabwitsa. Koma sadzachiona kupatula chizindikiro chija cha Yona.
30 Jonah tah Nineveh ham miknoek la a om vanbangla, hlang capa khaw tahae kah cadil taengah om van ni.
Monga Yona uja anali chizindikiro kwa anthu ku Ninive, momwemonso Mwana wa Munthu adzakhala chizindikiro kwa anthu a mʼbado uno.
31 Tahae cadil hlang rhoek taengkah laitloeknah ah tuithim manghainu te thoo vetih amih te a boe sak ni. Anih tah Solomon kah cueihnah hnatun ham diklai khobawt lamkah ha pawk. He ah he Solomon lakah aka khuet om ta he.
Mfumu yayikazi yakummwera idzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi anthu a mʼbado uno ndipo idzawatsutsa, chifukwa iyo inachokera kumapeto a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomoni. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Solomoni.
32 Ninevi hlang rhoek loh tahae cadil kah laitloeknah te a pai uh thil vetih a boe sak ni. Jonah kah olhoe neh a yut uh atah, he ah aka om he Jonah lakah khuet dae ta he.
Anthu a ku Ninive adzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi mʼbado uno ndipo adzawutsutsa, pakuti anatembenuka mtima ndi ulaliki wa Yona. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Yona.
33 Hmaiim a tok te tanhnaem ah khueh pawt tih voh khuiah khaw a muek moenih. Tedae aka kun rhoek loh vangnah hmu van saeh tila hmaitung soah ni a khueh.
“Palibe amene amayatsa nyale ndi kuyiika pa malo poti sionekera, kapena pansi pa mtsuko. Mʼmalo mwake amayika pa choyikapo chake, kuti iwo amene akulowamo aone kuwunika.
34 Na mik tah na pum kah hmaiim ni. Na mik loh cilrhik la a om vaengah na pum boeih te cilping la om van. Tedae a thae la a om vaengah na pum tah hmuep van.
Diso lanu ndi nyale ya thupi lanu. Pamene maso anu ali bwino, thupi lanu lonse limadzaza ndi kuwunika. Koma ngati ali oyipa, thupi lanunso ndi lodzaza ndi mdima.
35 Te dongah ngaithuen, na khuikah vangnah te yinnah la poeh ve.
Onetsetsani tsono, kuti kuwunika kuli mwa inu si mdima.
36 Te dongah na pum te boeih vang tih cungvang ah a hmuep pakhat khaw a om pawt atah, hmaiim loh a aa neh nang n'tue vaengkah bangla phaeng aka vang la om ni,” a ti nah.
Choncho, ngati thupi lanu lonse ndi lodzaza ndi kuwunika, ndiye kuti palibe dera lina lili mdima, lonselo lidzakhala kuwunika, monga momwe kuwunika kwa nyale kumakuwalirani.”
37 A thui vaengah, Pharisee loh a taengah buh ca la anih te a cael dongah kun tih a ngol puei.
Yesu atamaliza kuyankhula, Mfarisi wina anamuyitana kuti akadye naye. Tsono Yesu analowa mʼnyumba ndi kukhala podyera.
38 Buh kungah khut a nuem lamhma pawt te Pharisee loh a hmuh tih a ngaihmang.
Mfarisiyo anadabwa atazindikira kuti Yesu anayamba kudya wosatsata mwambo wawo wakasambidwe ka mʼmanja.
39 Tedae Boeipa loh anih te, “Nangmih Pharisee rhoek loh boengloeng neh baelpuei kah a hmanhu tah na cil na poe coeng. Tedae na khuiah halhkanah neh halangnah ni aka bae.
Kenaka Ambuye anamuwuza kuti, “Inu Afarisi mumatsuka kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkati mwanu ndi modzaza ndi kudzikonda ndi zoyipa.
40 Hlang ang rhoek! a sohman ah aka saii loh a khui te khaw a saii moenih a?
Anthu opusa inu! Kodi amene anapanga zamʼkati sanapangenso zakunja?
41 Tedae a khuikah aka om te doedannah la pae uh lamtah, nangmih ham boeih caih ni.
Koma popereka kwa osauka, perekani chimene chili mʼkati ndipo chilichonse chidzakhala choyera.
42 Anunae nangmih Pharisee rhoek! Sungii, sungsing neh toian boeih tah na paek uh dae Pathen kah tiktamnah neh lungnah tah na hnalvaluh. Saii hamla a kuek te dalrha uh tak boeh.
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumapereka kwa Mulungu chakhumi cha timbewu tonunkhira, ndi timbewu tokometsera chakudya ndi mbewu zina zonse za mʼmunda, koma mumakana chilungamo ndi chikondi cha Mulungu. Mumayenera kuchita zomalizirazi osalekanso kuchita zoyambazi.
43 Anunae nangmih Pharisee rhoek te! tunim kah ngolhmuen then neh hnoyoih hmuen kah toidalnah ni na lungnah uh.
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumakonda mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malonje mʼmalo a pa msika.
44 Anunae nangmih aih te, hlan bangla lumrhilumrha la na om uh dongah a sokah aka pongpa hlang loh ming pawh,” a ti nah.
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa muli ngati manda osawaka, amene anthu amangoyendapo, osawadziwa.”
45 Olming pakhat loh Jesuh te a doo tih, “Saya, na thui te kaimih ni nan neet,” a ti nah.
Mmodzi mwa akatswiri a Malamulo anamuyankha Iye nati, “Aphunzitsi, pamene mukunena zinthu izi, mukutinyoza ifenso?”
46 Tedae Jesuh loh, “Nangmih olming rhoek khaw anunae, hlang rhoek te hnophueih neh phueihtloel la na nan uh tih, namamih tah na kutdawn pakhat nen khaw hnophueih te na ben uh pawh.
Yesu anayankha kuti, “Tsoka kwa inunso akatswiri a Malamulo chifukwa mumawalemetsa anthu ndi mtolo umene iwo sangathe kunyamula, ndipo inu eni ake simutenga chala chanu kuti muwathandize.
47 Anunae nangmih aih, tonghma rhoek kah phuel te na sak uh dae na pa rhoek long ni amih te a ngawn.
“Tsoka kwa inu, chifukwa mumawaka manda a aneneri, komatu ndi makolo anu amene anawapha.
48 Na pa rhoek kah a khuui la na om uh van dongah a khoboe te na rhoihuh. Tonghma rhoek te amih loh a ngawn tih nangmih loh phuel im na sak pa uh.
Tsono potero mumachitira umboni za zimene makolo anu anachita. Anapha aneneri, ndipo inu mumawaka manda awo.
49 Te dongah Pathen kah cueihnah long khaw, “Amih taengah tonghma rhoek neh caeltueih rhoek te ka tueih van vaengah, amih te a ngawn uh vetih a hnaemtaek bitni,” a ti.
Chifukwa cha ichi, Mulungu mu nzeru zake anati, ‘Ine ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, ena mwa iwo adzawapha ndipo ena adzawazunza.’
50 Te dongah Diklai a tongnah lamkah tahae cadil rhoek loh a long sak tonghma rhoek kah a thii phu te boeih suk nawn saeh.
Choncho mʼbado uwu udzasenza magazi a aneneri onse amene anakhetsedwa kuyambira pachiyambi cha dziko,
51 Abel thii lamloh Zekhariah thii duela hmueihtuk neh im laklo ah ni a poci. Ue ta, nangmih taengah ka thui, tahae kah cadil taengah a suk bitni.
kuyambira magazi a Abele kufikira magazi a Zakariya amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi malo opatulika. Inde, Ine ndikuwuzani inu, mʼbado uno udzasenza zonsezi.
52 Anunae nangmih olming rhoek te, mingnah cabi na pom lalah namamih khaw na kun uh pawt tih aka kun rhoek te na kang uh,” a ti nah.
“Tsoka kwa inu akatswiri a Malamulo, chifukwa mwachotsa kiyi wachidziwitso inu eni akenu musanalowemo, ndipo mwatsekerezanso iwo amene amalowa.”
53 Te lamkah loh Jesuh vawl a nong phoeiah tah cadaek rhoek neh Pharisee rhoek loh mat a hmuhuet uh tih anih kawng te muep a cawh uh.
Pamene Yesu anachokamo, Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo anayamba kumamutsutsa koopsa ndi kumupanikiza ndi mafunso,
54 A ka lamkah ol khat khat neh tangkhuep ham amah te a rhongngol uh.
pofuna kumukola muchina chilichonse chimene Iye angayankhule.