< Laitloekkung 9 >

1 Jerubbaal capa Abimelek te a nupu rhoek taengah Shekhem la cet tih amih te khaw, a manu kah a napa imkhui cako boeih te a voek.
Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
2 Shekhem boei boeih kah a hna dongah khaw, “Jerubbaal ca rhoek hlang sawmrhih boeih loh nangmih soah a ngol ham neh hlang pakhat bueng loh nangmih soah a ngol ham te nangmih ham melae aka then bet eh? Te dongah kai khaw na rhuh na saa van ni tite poek uh,” a ti nah.
“Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
3 Te olka boeih te Shekhem boei rhoek boeih kah hna dongah tah, “Anih kah a nupu pai ni,” a ti uh tih, “Anih te mah manuca ni,” a ti uh dongah Abimelek taengla a lungbuei boeih hooi uh.
Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
4 Te dongah Baalberith im lamkah tangka sawmrhih te anih a paek uh. Te nen te Abimelek loh hlang hoeng rhoek neh aka soetae rhoek te a paang tih a hnukah bang uh.
Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
5 Ophrah kah a napa im la a pawk vaengah a manuca rhoek, Jerubbaal ca rhoek hlang sawmrhih te lungto pakhat dongah rhenten a ngawn. Tedae Jerubbaal capa a poeih Jotham tah thuh uh tih sueng.
Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
6 Shekhem boei rhoek boeih neh Bethmillo boeih loh a tingtun uh phoeiah cet uh tih Abimelek te Shekhem kah aka pai thingnu kaepah manghai la a manghai sak uh.
Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
7 Tedae Jotham taengla a puen pa uh vaengah tah Gerizim tlang som la luei tih pai. Te phoeiah a ol a huel tih a pang doela, “Shekhem boei rhoek ka ol he hnatun uh lah. Te daengah ni Pathen loh nangmih ol te a hnatun eh.
Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
8 Thing rhoek loh a manghai situi koelh ham cet cet uh tih olive taengah, ‘Kaimih soah manghai khaw manghai mai laeh he,’ a ti na uh.
Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
9 Tedae amih te olive loh, ‘Pathen neh hlang aka thangpom ka maehhloi he ka toeng mai vetih thing rhoek soah vikvuek ham ka cet aya?’ a ti nah.
“Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
10 Thing rhoek loh thaibu taengah khaw, ‘Namah halo lamtah kaimih soah manghai mai laeh,’ a ti na uh.
Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
11 Tedae amih te thaibu loh, ‘Ka didip neh ka thaih then he ka toeng mai vetih thing rhoek soah vikvuek ham ka cet aya?’ a ti nah.
Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
12 Misur taengah khaw thing rhoek loh, ‘Nang halo lamtah kaimih soah manghai khaw manghai mai laeh,’ a ti na uh.
Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
13 Tedae amih te misur loh, ‘Pathen neh hlang ko aka hoe sak ka misur thai te ka toeng mai vetih thing rhoek soah vikvuek ham ka cet aya?’ a ti nah.
Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
14 Thing rhoek boeih long te tangkul taengla, ‘Nang halo lamtah kaimih soah manghai mai saw,’ a ti na uh.
Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
15 Tangkul long tah thing rhoek taengah, ‘Na oltak nen ni nangmih sokah manghai la kai n'koelh uh van atah, halo uh lamtah ka hlipkhup ah ying uh. Te pawt koinih tangkul puep lamkah hmai puek vetih Lebanon lamphai khaw a hlawp ni,’ a ti nah.
Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
16 “Tahae ah oltak neh a khangmai la na saii uh tih Abimelek te na manghai sak uh coeng atah Jerubbaal ham neh a imkhui ham hnothen nim na saii uh tih a taengah a kut neh aka tiing lam nim na saii uh.
Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
17 A pa loh nangmih ham a vathoh tih a hmai ah a hinglu a voeih dongah nangmih te Midian kut lamloh n'huul.
Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
18 Tedae nangmih loh tihnin ah a pa cako te na thoh thil uh tih a ca rhoek hlang sawmrhih te lungto pakhat dongah na ngawn uh. A salnu kah a ca Abimelek vik te na manuca na ti uh tih Shekhem boei rhoek soah na manghai sak uh.
Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
19 Tihnin Jerubbaal taeng neh a cako taengah oltak neh a khangmai la na saii uh coeng atah Abimelek dongah kohoe uh lamtah anih khaw nangmih dongah a kohoe saeh.
Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
20 Abimelek lamloh hmai puek tih Shekhem boei rhoek neh Bethmillo te a hlawp pawt atah Shekhem boei rhoek neh Bethmillo lamkah hmai aka puek loh Abimelek te hlawp saeh,” a ti nah.
Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
21 Te ah kho a sak te a maya Abimelek kah mikhmuh la a om dongah Jotham loh rhaelrham tih aka yong te Beer la pawk.
Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
22 Abimelek te Israel soah kum thum boei.
Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
23 Tedae Pathen loh Abimelek laklo neh Shekhem boei rhoek kah laklo ah mueihla thae a tueih pah dongah Shekhem boei rhoek loh Abimelek te a hnukpoh thil uh.
Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
24 Te tah Jerubbaal ca rhoek hlang sawmrhih te kuthlahnah a khuen thil tih a aka ngawn a manuca Abimelek so neh a manuca rhoek ngawn sak ham a kut aka thoh Shekhem boei rhoek soah a thii phu a suk ham dongah ni.
Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
25 Abimelek te a moeh uh tih tlang som ah aka rhongngol Shekhem boei rhoek loh longpuei ah aka pongpa boeih te a rheth uh te Abimelek taengla a puen pah.
Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
26 Te vaengah Ebed capa Gaal neh a manuca rhoek tah ha pawk tih Shekhem la a kat uh hatah Shekhem boei rhoek loh anih dongah pangtung uh.
Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
27 Lo a pha uh vaengah misur a hoel uh tih a hoem uh dongah cangkoeinah a saii uh. Te phoeiah a pathen im la kun uh tih a caak a ok uh phoeiah Abimelek te a tap uh.
Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
28 Te vaengah Ebed capa Gaal loh, “Abimelek te unim, anih taengah thohtat ham khaw Shekhem te unim? Jerubbaal capa, a hlangtawt khaw Zebul moenih a? Shekhem napa Hamor hlang rhoek taengah thotat uh. Balae tih mamih loh anih taengah n'thotat uh eh?
Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
29 Unim mah, pilnam he ka kut dongah han tloeng atah Abimelek ngawn tah ka rhoe vetih Abimelek te, ‘Na caempuei khaw kuk lamtah ha mop lah,’ ka ti bitni,” a ti nah.
Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
30 Ebed capa Gaal ol te khopuei mangpa Zebul loh a yaak vaengah a thintoek a sai pah.
Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
31 Te dongah puencawn rhoek te Abimelek taengah a huep la a tueih tih, “Ebed capa Gaal neh a manuca rhoek loh Shekhem la ha pawk uh te, khopuei ah nang aka dum ham ni ke.
Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
32 Te dongah namah neh namah taengkah pilnam loh khoyin ah thoo uh lamtah lohma ah ana rhongngol uh laeh.
Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
33 Mincang a pha tih khomik a cuk vaengah thoo uh lamtah khopuei te cuuk thil uh. Amah khaw, amah taengkah pilnam khaw nang taengla ha pawk vaengah na kut loh a tong sarhui bangla anih te saii uh,” a ti nah.
Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
34 Te dongah Abimelek neh a taengkah pilnam pum te khoyin ah a thoh tih Shekhem ah than li la a rhongngol uh.
Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
35 Te dongah Ebed capa Gaal te moe phai tih khopuei vongka kah thohka ah pai. Te vaengah Abimelek neh a pilnam te rhong lamkah ha thoo.
Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
36 Pilnam te a hmuh vaengah Zebul te Gaal loh, “Pilnam loh tlang som lamkah ha suntla ke,” a ti nah. Tedae Zebul loh, “Nang khaw mah, tlang kah mueihlip maco hlang bangla na hmuh,” a ti nah.
Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
37 Tedae Gaal loh a thui te koep a khoep tih, “Khohmuen laklung khui lamloh pilnam suntla tih kutyaek thingnu longpuei lamloh rhoi at ha thoeng ke,” a ti nah.
Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
38 Te vaengah Zebul loh, “‘Anih taengah thohtat ham khaw Abimelek te unim,’ na ti vaengkah na ka te tahae atah melam a om, anih he a pilnam neh na sawtsit thil moenih a? Tahae ah paan to lamtah amah ke hnuei kanoek saw,” a ti nah.
Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
39 Te dongah Gaal tah Shekhem boei rhoek kah mikhmuh la moe phai tih Abimelek te a hnueih.
Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
40 Tedae anih te Abimelek loh a hloem tanglai atah a mikhmuh lamloh rhaelrham tih vongka thohka due, hmalaem la muep cungku uh.
Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
41 Abimelek te Arumah ah kho a sak ngawn dae Shekhem ah kho aka sa khui lamkah Gaal neh a manuca rhoek te Zebul loh vik a haek.
Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
42 A vuen ah om tih pilnam te pong la a caeh ham vaeng daengah Abimelek taengla a puen pa uh.
Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
43 Te dongah pilnam te a loh tih hlop thum la a boel phoeiah lohma ah a rhongngol sak. Te vaengah khopuei lamkah pilnam ha pawk te lawt a hmuh dongah amih te a pai thil tih a tloek.
Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
44 Te vaengah Abimelek neh a rhoi rhoek te capit uh tih khopuei vongka kah thohka te a pai thil uh. Tedae rhoi nit long te lohma kah rhoek te boeih a capit thil uh tih a tloek uh.
Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
45 Abimelek loh khohnin yung ah khopuei te a vathoh thil tih khopuei te a loh. A khuikah pilnam te khaw a ngawn tih khopuei te a palet phoeiah lungkaeh a phul thil.
Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
46 Boei kuirhang boeih loh a yaak uh vaengah Elberith im kah hmuensang la ael uh.
Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
47 Tedae boei kuirhang rhoek loh boeih a coi uh thae te Abimelek taengla a puen pa uh.
Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
48 Te dongah Abimelek loh a taengkah pilnam boeih te Zalmon tlang la a caeh puei. Te vaengah Abimelek loh a kut dongkah hai te a loh tih thing hlaeng a saih. Thing hlaeng te a thueng tih a laengpang dongah a khueh. Te phoeiah a taengkah pilnam te, “Ka saii he so uh lamtah kai bangla koe saii uh,” a ti nah.
Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
49 Te dongah pilnam boeih long khaw thing hlaeng rhip a saih uh tih Abimelek hnuk a vai uh. Te phoeiah hmuensang te a hong thil uh tih hmuensang te hmai a hlup uh vaengah tah kuirhang huta tongpa hlang thawngkhat tluk boeih duek uh.
Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
50 Abimelek te Thebez la cet tih a rhaeh thil phoeiah Thebez te a loh.
Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
51 Tedae khopuei khui ah sarhi rhaltoengim pakhat om tih huta tongpa boeih neh khopuei kah boei boeih loh te lam te rhaelrham uh tih a hnuk te malh a buk phoeiah rhaltoengim kah imphu la luei uh.
Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
52 Te phoeiah rhaltoengim te Abimelek loh a paan tih a vathoh thil. Te dongah hmai neh hoeh hamla rhaltoengim kah thohka la thoeih.
Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
53 Tedae Abimelek kah a lu te huta pakhat loh sumngol phaklung neh a dae pah tih a luhih a po pah.
Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
54 Te dongah a hnopai aka phuei camoe te koe a khue tih, “Na cunghang te bong lamtah kai he ng'ngawn to laeh, kai he, ‘Huta loh a ngawn,’ ti uh ve,” a ti nah. Te dongah a camoe long te a thun tih duek.
Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
55 Israel hlang loh Abimelek a duek te a hmuh uh. Te phoeiah tah hlang loh amah hmuen la cet uh.
Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
56 Abimelek loh a napa taengah boethae a saii tih a manuca hlang sawmrhih a ngawn te Pathen loh a thuung pah.
Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
57 Shekhem hlang kah boethae boeih te khaw amamih lu dongah Pathen loh a thuung pah tih Jerubbaal capa Jotham kah rhunkhuennah te khaw amih soah tla.
Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.

< Laitloekkung 9 >