< Laitloekkung 6 >

1 Israel ca rhoek loh BOEIPA mikhmuh ah thae a saii. Te dongah BOEIPA loh amih te kum rhih khuiah Midian kut ah a paek.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
2 Te dongah Midian mikhmuh ah, Midian kut te Israel soah tanglue. Israel ca rhoek loh amamih ham buep te tlang, lungko neh, rhalmahim ah a tuk uh.
Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
3 Israel kah a lotawn khaw Midian, Amalek neh khothoeng ca loh ham paan tih a luei thil uh.
Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
4 Amih te a rhaeh thil uh tih khohmuen cangpai te a phae uh. Gaza duela na ka cet te Israel neh tu, vaito, laak ham kangna khaw hinglu hlawtnah paih uh pawh.
Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
5 Amih loh a dap te boiva neh a paan uh. A paan uh vaengah hlangping neh kaisih bangla muep ha pawk uh. Te vaengah amih neh a kalauk rhoek tah tae lek na moenih. Te dongah khohmuen phae ham ni a muk uh.
Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
6 Midian mikhmuh ah Israel he bahoeng a tlayae coeng dongah Israel ca rhoek loh BOEIPA a pang thiluh.
Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
7 Midian kawng dongah BOEIPA te Israel ca rhoek loh a pang thil uh khaw ana om coeng.
Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
8 Te vaengah Israel ca rhoek ham tonghma pakhat te BOEIPA loh a tueih tih, “Amih te, 'Israel Pathen BOEIPA loh, 'Nangmih he kai loh Egypt lamkah kan doek tih sal imkhui lamloh nangmih he kam poh.
Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
9 Egypt kut lamkah khaw, nangmih aka nen kut cungkuem lamkah khaw, nangmih kan lat coeng. Nangmih mikhmuh lamloh amih te ka haek tih amih khohmuen te nangmih kam paek.
Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
10 Te vaengah nangmih taengah, 'Kai tah BOEIPA na Pathen ni, a khohmuen ah na om uh thil Amori pathen te rhih uh boeh,’ ka ti lalah ka ol na hnatun uh pawh,’ a ti,” a ti nah.
Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
11 BOEIPA kah puencawn te koep ha pawk tih Ophrah kah rhokael hmuiah ngol. Te vaengah Midian mikhmuh lamkah rhaelrham ham Abiezer Joash neh a capa Gideon loh misur rhom ah cang a boh.
Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
12 Anih taengah khaw BOEIPA puencawn a phoe pah tih, “Tatthai hlangrhalh nang taengah BOEIPA om,” a ti nah.
Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
13 Tedae anih te Gideon loh, “Ka boeipa, kaimih taengah BOEIPA om ta. Tedae balae tih kaimih taengah a cungkuem he a thoeng? A khobaerhambae cungkuem te melae? Te te kaimih taengah a pa a thui vaengah tah Kaimih he BOEIPA loh Egypt lamkah n'doek moenih a?” a ti. Tedae BOEIPA loh kaimih he n'phap tih Midian kut ah kaimih n'tloeng coeng he,” a ti nah.
Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
14 Te vaengah BOEIPA te anih taengla la hooi uh tih, “Na thadueng neh cet lamtah Midian kut lamkah Israel he khang laeh. Nang kan tueih rhoe moenih a?” a ti nah.
Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
15 Te dongah amah te, “Ka Boeipa aw, Israel he ba nen lae ka khang eh? Manasseh khuiah tattloel la kai he thawngkhat ka lo tih a pa imko khuiah kai ni canoi coeng,” a ti nah.
Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
16 Tedae anih te BOEIPA loh, “Nang taengah ka om vetih Midian te hlang pakhat banglam ni na tloek ngawn eh?,” a ti nah.
Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
17 Te vaengah Gideon loh, “Na mikhmuh ah mikdaithen ni ka dang atah kai taengah na thui te miknoek la kai taengah han saii laeh.
Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
18 Nang taengla ka pawk tih ka khosaa kang khuen te na mikhmuh ah ka tloeng duela he lamloh ana nong boel dae,” a ti nah. Te dongah, “Kai khaw nang bal duela kana om bitni,” a ti nah.
Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
19 Gideon te cet tih maae ca neh vaidam te vaidamding la cangnoek pakhat a hmoel. Maeh te vaihang dongah a doh phoeiah maehhang te am khuiah a thun. Te phoeiah rhokael hmui kah puencawn taengla a khuen tih a tawn pah.
Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
20 Pathen kah puencawn loh Gideon taengah, “Maeh neh vaidamding te lo lamtah thaelpang soah tloeng lah. Te phoeiah maehhang bueih thil,” a ti nah vanbangla a saii pah.
Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
21 Te phoeiah BOEIPA puencawn loh a kut dongkah cunghol hmuidong te a thueng tih maeh neh vaidamding te a nawn te a nawn hatah lungpang lamloh hmai thoo tih maeh neh vaidamding te a hlawp. Te phoeiah BOEIPA puencawn khaw a mikhmuh lamloh vik cet.
Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
22 Te daengah anih te BOEIPA kah puencawn la Gideon loh a hmuh. Te phoeiah Gideon loh, “Aw, ka Boeipa Yahovah, BOEIPA puencawn te maelhmai neh ka hmuh,” a ti.
Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
23 Tedae anih te BOEIPA loh, “Na sading saeh, rhih boeh, na duek mahpawh,” a ti nah.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
24 Te dongah Gideon loh BOEIPA ham hmueihtuk pahoi a suem pah. Hmueithuk te khaw ngaimongnah BOEIPA a sui tih tihnin duela Abiezer Ophrah ah om pueng.
Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
25 Tekah khoyin ah Gideon te BOEIPA loh, “Na pa kah vaito a tal pakhat neh vaitotal kum rhih koep khuen lamtah na pa kah Baal hmueihtuk koengloeng laeh, a taengkah Asherah te khaw top pah.
Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
26 Hekah lunghim som ah he BOEIPA na Pathen ham hmueihtuk suem laeh. Vaito a pabae te maehlaep la khuen lamtah na top sut Asherah thing neh hmueihhlutnah la nawn laeh,” a ti nah.
Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
27 Te dongah Gideon loh a sal hlang parha te a khuen tih BOEIPA loh a taengah a thui pah vanbangla a saii. Tedae khothaih ah a saii ham te a napa cako neh khopuei kah hlang rhoek te a rhih dongah khoyin ah a saii.
Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
28 Mincang ah khopuei kah hlang rhoek loh a thoh uh vaengah Baal kah hmueihtuk te ana tim tih a taengkah Asherah khaw ana top pa uh, vaito pabae te khaw hmueihtuk a suem tangtae dongah tarha ana nawn pauh.
Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
29 Te dongah hlang loh a hui taengah, “Hekah hno aka saii he ulae?” a ti uh tih a cae uh. Tedae a tlap uh vaengah tah, “Hekah hno he Joash capa Gideon long ni a saii,” a ti uh.
Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
30 Te dongah khopuei hlang rhoek loh Joash taengah, “Na capa te hang khuen, Baal kah hmueihtuk a palet tih a taengkah Asherah a top dongah duek kangna saeh,” a ti uh.
Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
31 Tedae a taengkah aka pai rhoek boeih taengah Joash loh, “Nangmih loh Baal ham na kamkaih uh a ya? Anih te nangmih loh na khang uh tang a ya? Anih aka oelh tah mincang a pha neh ki duek bitni. Baal he pathen la a om van oeh atah a hmueihtuk a palet pah vaengah amah loh a huul kanoek mako,” a ti nah.
Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
32 Te dongah tekah khohnin lamkah longtah tah, “A hmueihtuk ka palet pah tih Baal amah te khaw ka ho coeng,” a ti nah ngaih la Gideon te Jerubbaal la tloep a khue.
Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
33 Te vaengah Midian boeih neh Amalek khaw khothoeng ca rhoek loh tun kibaeng uh tih a kat phoeiah Jezreel kol ah rhaeh uh.
Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
34 Tedae BOEIPA Mueihla loh Gideon te a thing dongah tuki te a ueng tih a hnukkah Abiezer te a hueh.
Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
35 Manasseh ram tom ah puencawn te a tueih tih amah hnuk ah a khue. Te phoeiah puencawn te Asher, Zebulun neh Naphtali la a tueih tih amih doe hamla cet uh.
Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
36 Te phoeiah Gideon loh Pathen te, “Na thui tangtae bangla Israel te ka kut neh aka khang la na om atah,
Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
37 Tumul hluem khat te cangtil hmuen ah ka khueh he. Teka tumul hluem khat dong bueng ah buemtui om tih diklai boeih te phueihuet la a om atah na thui bangla Isreal te ka kut neh na khang ni tila ka ming eh?,” a ti nah.
onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
38 Te dongah om tangloeng tih a vuen kah a thoh vaengah tah tumul hluem te a sui. Te vaengah tumul hluem dongkah buem tui te baeldung a bae la a sui.
Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
39 Tedae Gideon loh Pathen taengah, “Na thintoek loh kai taengah sai boel mai saeh lamtah, vai mah ka thui mai vai bueng mah ka noem dae eh, tumul hluem a phueihuet he tumul hluem amah thim la om vetih diklai pum he buemtui a om atah,” a ti nah bal.
Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
40 Pathen long khaw a rhoi pah dongah tekah khoyin ah tah tumul hluem bueng te phueihuet la om tih diklai pum te buemtui boeih bo.
Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.

< Laitloekkung 6 >