< Laitloekkung 20 >

1 Israel ca rhoek boeih capit uh tih Dan lamloh Beersheba neh Gilead kho duela rhaengpuei loh Mizpah kah BOEIPA taengah pakhat la tingtun uh.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
2 Pathen kah pilnam hlangping lakli ah pilnam boeih te a cong cong ah, Israel koca rhoek khaw boeih a pai uh vaengah rhalkap hlang thawng ya li loh cunghang a pom.
Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
3 Israel ca rhoek Mizpah la a caeh uh te Benjamin ca rhoek loh a yaak uh. Te vaengah Israel ca rhoek loh, “Hekah boethae he metlam a om thui uh lah,” a ti uh.
Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
4 Te dongah a ngawn uh huta kah a va Levi hlang loh a doo tih, “Benjamin kah Gibeah la kamah ka cet tih ka yula taengah ka rhaeh.
Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
5 Te vaengah Gibeah boei rhoek loh kai n'thoh thil uh tih kai te khoyin ah im neh rhen m'vael uh. Kai te ngawn ham cai uh coeng dae ka yula te a phaep uh tih duek.
Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
6 Israel khuiah boethae halang neh khonuen rhamtat la a saii uh dongah ka yula te ka loh tih ka sah phoeiah Israel kah rho, khohmuen tom la ka pat.
Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
7 Nangmih Israel ca boeih loh namamih kah olka neh cilsuep khaw pahoi pae uh laeh,” a ti nah.
Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
8 Te vaengah pilnam pum loh pumkhat la pai tih, “Hlang pakhat long khaw a dap la cet boel saeh lamtah pakhat khaw a im la phael boel saeh.
Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
9 Tedae tekah olka vanbangla Gibeah te hmulung neh saii sih.
Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
10 Israel khuiah boethae halang boeih a saii vanbangla Geba kah Benjamin te aka paan tih aka saii pilnam ham lampu aka lo la Israel koca boeih te yakhat ah hlang rha, thawngkhat ah yakhat, thawngrha dongah thawngkhat lo sih,” a ti uh.
Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
11 Te dongah Israel hlang boeih loh khopuei te a capit thil uh tih pumkhat hui uh.
Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
12 Te dongah Israel ca rhoek loh Benjamin koca rhoek boeih taengah hlang a tueih uh tih, “Balae tih hebang boethae loh na khuiah a om?
Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
13 Gibeah kah hlang muen ca rhoek te han tloeng laeh. Amih te ka duek sak uh daengah ni Israel khui lamkah boethae te ka khoe pueng eh,” a ti nah. Tedae a pacaboeina Israel ca rhoek kah ol te Benjamin ca rhoek loh hnatun ham huem uh pawh.
Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
14 Tedae khopuei rhoek lamkah Benjamin ca rhoek loh Israel ca rhoek taengah caemtloek la caeh ham Gibeah ah tingtun uh.
Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
15 Te vaeng khohnin ah khopuei takuem lamkah Benjamin ca rhoek te soep uh thae tih cunghang aka pom hlang thawng kul thawng rhuk neh Gibeah kah aka om hlang ya rhih te a soep uh tih a coelh thil uh.
Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
16 Te vaengah pilnam boeih khuikah tongpa ya rhih te a coelh uh. Amih te bantang kut aka poem la boeih om dae lungto a dong uh vaengah sam pataeng pit tlaih pawh.
Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
17 Benjamin kah a voel ah Israel ca loh buel uh cunghang aka pom caemtloek hlang he a pum boeih la hlang thawng ya li louh.
Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
18 Tedae thoo uh tih Bethel la a yoeng vaengah Pathen te a dawt uh hatah Israel ca rhoek loh, “Benjamin ca rhoek te caemtloek thil ham kaimih ah ulae lamhma la aka cet eh?,” a ti na uh. Te vaengah BOEIPA loh, “Judah te lamhma saeh,” a ti nah.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
19 Te dongah Israel ca rhoek loh mincang ah thoo uh tih Gibeah ah rhaeh uh.
Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
20 Benjamin te caemtloek thil ham Israel hlang te cet tih Israel caemtloek hlang he Gibeah ah yaal uh.
Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
21 Te vaengah Gibeah lamkah Benjamin ca rhoek ha pawk uh tih lohma sa ah Israel hlang thawng kul thawng hnih te hnin at dongah a phop.
A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
22 Tedae Israel hlang pilnam loh a thaa a huel tih lamhma khohnin kah rhongpai hmuen ah caemtloek ham te rhong koep a pai uh.
Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
23 Te daengah Israel ca rhoek loh cet uh tih kholaeh duela BOEIPA mikhmuh ah rhap uh. BOEIPA te a dawt uh tih, “Ka manuca Benjamin ca rhoek te caemtloek la thoeih ham ka khoep aya?,” a ti na uh. Te vaengah BOEIPA loh, “Anih te caeh thil uh,” a ti nah.
Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
24 Te dongah a hnin bae dongah Israel ca rhoek loh Benjamin ca rhoek taengla mop uh.
Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
25 A hnin bae dongah tah amih aka doe ham te Benjamin khaw Gibeah lamkah ha pawk tih Israel ca khui lamkah cunghang aka pom hlang thawng hlai rhet te lohma sa ah boeih a thup uh bal.
Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
26 Te dongah Israel ca rhoek boeih neh pilnam pum loh cet uh tih Bethel a paan uh. Te vaengah a rhah doela BOEIPA mikhmuh ah ngol uh. Hnin at neh kholaeh duela a yaeh tih BOEIPA mikhmuh ah hmueihhlutnah neh rhoepnah te a nawn uh.
Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
27 Te phoeiah BOEIPA te Israel ca rhoek loh a dawt uh. Te vaeng tue ah tah Pathen kah paipi thingkawng khaw te ah te om.
Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
28 Te vaeng tue ah Aaron koca Eleazar ca Phinekha tah paipi thingkawng hmai ah pai tih, “Ka manuca Benjamin ca rhoek taengah caemtloek la caeh ham te koep ka rhaep aya, ka toeng pawn aya?,” a ti nah. Tedae BOEIPA loh, “Anih te thangvuen ah tah nang kut dongla kan tloeng ham coeng dongah cet ngawn,” a ti nah.
Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
29 Te dongah Israel loh Gibeah kaepvai ah rhongngol a khueh.
Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
30 A hnin thum dongah tah Benjamin ca rhoek te Israel ca rhoek loh a paan uh tih a noek noek kah bangla Gibeah te rhong a pai thiluh.
Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
31 Te vaengah pilnam aka doe ham te Benjamin ca rhoek ha hlah uh tih khopuei lamloh baat cing uh. A noek noek kah bangla pilnam soah a rhok la tloek banlak ham te Bethel neh Gibeah la aka pawk longpuei ah a tong uh tih Israel hlang sawmthum tluk te lohma sa ah a ngawnuh.
Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
32 Te vaengah Benjamin ca rhoek loh, “Lamhma kah bangla mamih mikhmuh ah yawk uh coeng,” a ti uh. Tedae Israel ca rhoek loh, “Rhaelrham uh sih lamtah khopuei lamloh longpuei la cing tak sih,” a ti uh.
Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
33 Te dongah Israel hlang boeih tah a hmuen lamloh thoo uh tih Baaltamar la rhong a pai uh. Te vaengah Israel khuikah aka rhongngol te Gibeah pool lamloh amah hmuen la a poh.
Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
34 Te phoeiah Israel boeih khui lamkah hlang thawng rha a coelh loh Gibeah imdan te a paan uh hatah caemtloek khaw a lalh na uh. Tedae yoethae loh amih taengla a paan te Benjamin ca rhoek ming uh pawh.
Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
35 Benjamin te Israel mikhmuh ah BOEIPA loh a yawk sak coeng dongah Benjamin khui lamkah cunghang aka pom hlang thawng kul thawng nga yakhat te hnin at nen ni Israel ca rhoek loh a thup.
Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
36 Amamih a yawk uh te Benjamin ca rhoek loh a hmuh uh. Te vaengah Israel hlang tah Gibeah kah a khueh rhongngol dongla a pangtung coeng dongah Benjamin ca rhoek loh a hmuen vik a paek.
Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
37 Rhongngol rhoek long khaw Gibeah la tawn uh tih capit uh tih rhongngol patoeng te a sol dongah khopuei pum te cunghang ha dongla a kaeh.
Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
38 Israel hlang neh rhongngol te tingtunnah a om vaengah khopuei lamkah hmaikhu loh cangpaiso bangla muep luei.
Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
39 Tedae caemtloek vaengah Israel hlang loh ki a buung hatah Israel hlang la hlang sawmthum tluk te Benjamin loh a rhok la pahoi a tloek tih, “Lamhma kah caemtloek bangla mamih mikhmuh ah yawk rhoela yawk ngawn coeng,” a ti uh.
ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
40 Tedae hmaikhu tung te khopuei lamloh cangpaiso neh koe luei. Benjamin khaw a hnuk la a mael hatah khopuei pum te vaan la tarha ana khuu pah.
Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
41 Te vaengah Israel hlang te ha mael van hatah yoethae loh n'rhul thil coeng tila Benjamin hlang loh a hmuh dongah hlawt let.
Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
42 Te dongah Israel hlang kah mikhmuh ah khosoek longpuei la hooi uh. Tedae amih te caem loh han cuuk thil tih khopuei lamkah rhoek long khaw amih te a laklo ah a thup.
Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
43 Benjamin te a hloem uh tih a dum uh coeng dongah Gibeah khocuk due a yoeikoek la a cuuk uh.
Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
44 Te vaengah Benjamin khui lamkah tatthai hlang kak hlang thawng hlai rhet cungku.
Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
45 Te dongah hooi uh tih khosoek kah Rimmon thaelpang la rhaelrham uh. Tedae longpueng ah hlang thawng nga a paco uh. Te vaengah Gidom duela a cuuk uh tih hlang a thawng thawng la a ngawn uh.
Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
46 Te vaengah Benjamin khui lamkah aka cungku rhoek boeih he hnin at dongah mah cunghang aka pom tatthai hlang kak te hlang thawng kul thawng nga om.
Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
47 Tedae hlang ya rhuk tah hooi uh tih khosoek kah Rimmon thaelpang la a rhaelrham uh dongah Rimmon thaelpang ah hla li om uh.
Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
48 Te phoeiah Israel hlang loh Benjamin ca rhoek te a mael thil uh tih cunghang ha neh a ngawn uh. Khopuei lamkah hlang boeih neh a hmuh sarhui rhamsa khaw, kho tom kah a hmuh sarhui te khaw hmai neh a hla thiluh.
Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.

< Laitloekkung 20 >