< Joshua 10 >
1 Joshua loh Ai a buem vaengah Jerikho neh Jerikho manghai taengkah a saii bangla Ai neh Ai manghai taengah a saii tih a thup te khaw, Gibeon khosa rhoek, amih khuikah aka om rhoek khaw Israel neh mooi a thuung uh thae te Jerusalem manghai Adonizedek loh a yaak.
Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
2 Ram kah khopuei rhoek khuiah Gibeon tah pakhat nah khopuei bangla len. Ai lakah a len dongah tongpa hlangrhalh boeih long pataeng mat a rhih uh.
Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
3 Te dongah Jerusalem manghai Adonizedek loh Hebron manghai Hoham, Jarmuth manghai Piram, Lakhish manghai Japhia neh Eglon manghai Debir te a tah.
Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
4 Te vaengah, “Kai taengla ha yoeng uh lamtah kai n'bom uh dae. Joshua taeng neh Israel ca rhoek taengah moi aka thuung Gibeon ke tloek uh dae sih,” a ti nah.
Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
5 Te dongah Amori kah manghai panga neh Jerusalem manghai, Hebron manghai, Jarmuth manghai, Lakhish manghai, Eglon manghai loh tingtun uh tih a lambong neh boeih khoong uh. Te phoeiah Gibeon ah a rhaeh thil uh tih a vathoh thil uh.
Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
6 Te vaengah Gibeon kah hlang rhoek te Gilgal rhaehhmuen kah Joshua taengla a tueih uh tih, “Na sal rhoek taengah na kut han hlong boeh. Kaimih taengah koe halo lamtah kaimih he n'khang mai. Tlang kah khosa Amori manghai boeih loh kaimih taengla a tingtun uh dongah kaimih m'bom dae,” a ti nah.
Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
7 Te dongah Joshua amah neh amah taengkah caemtloek pilnam boeih, tatthai hlangrhalh boeih khaw Gilgal lamloh a khoong puei.
Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
8 Tedae BOEIPA loh Joshua taengah, “Amih te rhih boeh, na kut dongah kan tloeng coeng dongah amih khuikah pakhat khaw na mikhmuh ah pai mahpawh,” a ti nah.
Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
9 Gilgal lamkah khoyin khing a caeh puei vaengah Joshua loh amih taengla buengrhuet pawk.
Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
10 Amih te Israel mikhmuh ah BOEIPA loh a khawkkhek tih Gibeon ah hmasoe len neh a tloek uh. Te phoeiah amih te Bethhoron tangkham long ah a hloem tih Azekah neh Makkedah duela a tloek.
Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
11 Amih khaw Israel mikhmuh lamloh Bethhoron singling ah rhaelrham uh. Tedae amih te BOEIPA loh Azekah duela vaan lamkah lungcang len neh a lun thil. Te dongah Israel ca rhoek loh cunghang neh a ngawn lakah lungcang rhael dongah aka duek te muep duek uh ngai.
Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
12 Te dongah Joshua loh BOEIPA te a voek tih, “Aw BOEIPA Amori he Israel ca kah mikhmuh la tihnin ah tloeng pah laeh. Israel mikhmuh ah khomik loh Gibeon ah, hla long khaw Aijalon kol ah duem dae saeh,” a ti nah.
Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
13 Te dongah a thunkha namtom te phu a loh hil khomik loh duem tih hla khaw uelh. Jashar cabu dongah khaw, 'Vaan boengli ah khomik loh pai tih hnin at puet ah hat khum pawh,’ tila a daek moenih a?
Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
14 A mikhmuh ah tekah khohnin bang neh BOEIPA loh hlang ol a hnatun tih Israel ham aka vathoh BOEIPA he a om noek moenih.
Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
15 Te phoeiah Joshua neh Israel pum loh te Gilgal kah rhaehhmuen la bal uh.
Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
16 Te vaengah manghai panga te rhaelrham uh tih Makkedah kah lungko khuiah thuh uh.
Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
17 Tedae Joshua taengah a puen pa tih, “Makkedah kah lungko khuiah aka thuh manghai panga te a hmuh uh coeng,” a ti nah.
Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
18 Te dongah Joshua loh, “Lungko kah a rhai ah lungnu lungrhang paluet thil uh lamtah aka tawt ham koi hlang khaw hlah uh.
Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
19 Tedae nangmih loh na thunkha hnuk na hloem uh te toeng uh mueh la amih te tloek uh. Amih te nangmih kut dongah BOEIPA na Pathen loh han tloeng coeng dongah a khopuei la kun sak ham amih te hlah uh boeh,” a ti nah.
Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
20 Joshua neh Israel ca rhoek loh amih te bawt a tloek vaengah hmasoe len muep om tih dalh milh uh. Tedae amih khuiah aka coe tih rhaengnaeng rhoek tah khopuei hmuencak la pawk uh.
Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
21 Te dongah pilnam pum loh Makkedah rhaehhmuen kah Joshua taengah sading la mael uh. A hmui a lai loh Israel ca rhoek hlang pakhat khaw hlavawt pawh.
Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
22 Te vaengah Joshua loh lungko kah a rhai te ong uh lamtah lungko khui lamkah manghai panga te kai taengla hang khuen uh,” a ti nah.
Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
23 Te dongah lungko khui kah manghai panga la Jerusalem manghai, Hebron manghai, Jarmuth manghai, Lakhish manghai, Eglon manghai te a khuen pa uh.
Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
24 Manghai rhoek te Joshua taengla a khuen uh vaengah Israel hlang boeih te Joshua loh a khue tih anih taengla aka pawk caemtloek hlang kah rhalboei rhoek taengah, “Halo uh manghai rhoek he a rhawn ah na kho tloeng thil uh,” a ti nah. Te dongah halo uh tih amih rhawn dongah a kho a tloeng uh.
Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
25 Te phoeiah amih te Joshua loh, “Rhih boeh, rhihyawp boeh, thaahuel lamtah namning sak. Nangmih loh na vathoh thil na thunkha rhoek boeih te BOEIPA loh a saii bitni,” a ti nah.
Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
26 Amih te khaw Joshua loh a tloek tih a duek sak. Thing panga dongah a kuiok sak tih kholaeh due thing dongah dingkoei uh.
Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
27 Khotlak tue a lo vaengah Joshua loh a uen tih amih te thing dong lamloh a hlak uh. Amih te a thuh nah uh lungko khuiah pahoi a voeih uh tih lungko rhai kah lungnu a kuk uh te tihnin due hnorhuh la om pueng.
Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
28 Tekah khohnin dongah Joshua loh Makkedah te a loh tih cunghang ha neh a ngawn. A manghai neh a khuikah hinglu boeih te khaw a thup pah tih rhaengnaeng khaw paih pawh. Jerikho manghai taengkah a saii bangla Makkedah manghai taengah khaw a saii.
Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
29 Te phoeiah Joshua neh Israel pum te Makkedah lamloh Libnah la kat uh tih Libnah te a vathoh thil uh.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
30 Libnah te khaw BOEIPA loh Israel kut ah a paek. Te dongah a manghai te cunghang ha neh a ngawn tih a khuikah hinglu boeih te rhaengnaeng khaw hlun pawh. Te vaengah Jerikho manghai taengkah a saii bangla a manghai taengah khaw a saii.
Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
31 Te phoeiah Joshua neh Israel pum loh Libnah lamkah Lakhish la thoeih tih a vathoh thil, a rhaeh thil.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
32 Lakhish te khaw Israel kut dongah BOEIPA loh a paek. A hnin bae dongah te te a buem thai tih cunghang ha neh a tloek. A khuikah hinglu boeih te khaw Libnah bangla boeih a saii.
Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
33 Te vaengah Lakhish te bom ham Gezer manghai Horam te cet. Tedae anih khaw Joshua neh a pilnam loh rhaengnaeng a sueng pawt hil a tloek.
Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
34 Te phoeiah Joshua neh Israel pum te Lakhish lamkah Eglon la thoeih uh tih vathoh thil hamla a rhaeh thil uh.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
35 Amah khohnin ah Eglon te a buem uh tih cunghang ha neh a ngawn uh. A khuikah hinglu boeih te khaw amah khohnin ah Lakhish a saii bangla boeih a thup.
Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
36 Te phoeiah Joshua neh Israel pum tah Eglon lamloh Hebron la cet tih a tloek uh.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
37 Te te a buem uh vaengah a manghai neh a khopuei boeih, a khuikah hinglu boeih khaw, cunghang ha neh a ngawn uh. Eglon taengah boeih a saii bangla a khuikah hinglu te boeih a thup tih aka rhaengnaeng khaw hlun voel pawh.
Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
38 Te phoeiah Joshua neh Israel pum te Debir la bal tih a vathoh thil uh.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
39 Debir a buem vaengah khaw a manghai neh a khopuei boeih te cunghang ha neh a ngawn uh. Hebron a saii bangla Debir khaw a saii tih rhaengnaeng om mueh la a khuikah hinglu boeih te a thup uh. Libnah neh Libnah manghai taengkah a saii bangla Debir manghai taengah khaw a saii.
Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
40 Te dongah Israel Pathen BOEIPA kah a uen vanbangla Joshua loh tlang paengpang boeih neh Negev khaw, kolrhawk neh tuibah khaw a tloek. A manghai boeih te rhaengnaeng om mueh la hiil aka khueh boeih khaw a thup.
Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
41 Te phoeiah Joshua loh Kadeshbarnea lamloh Gaza due, Goshen khohmuen pum neh Gibeon duela a tloek.
Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
42 Tedae Israel ham te Israel Pathen BOEIPA loh a vathoh pah dongah ni te rhoek kah manghai rhoek neh a khohmuen te Joshua loh voei khat la boeih a buem thai.
Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
43 Te daengah Joshua neh Israel pum tah Gilgal kah rhaehhmuen la bal uh.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.