< Jeremiah 31 >
1 Te vaengkah a tue ah BOEIPA kah olphong om coeng. Israel cako boeih kah Pathen la ka om vetih amih te kamah taengah pilnam la om uh ni.
“Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
2 BOEIPA loh he ni a. thui. Cunghang kah a caknoi pilnam tah khosoek ah mikdaithen la a hmuh vetih Israel amah te hoep ham ni a. pongpa eh.
Yehova akuti, “Anthu amene anapulumuka ku nkhondo ndinawakomera mtima mʼchipululu; pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”
3 BOEIPA tah kai taengah daengrhae daengkhoi la ha phoe coeng dongah kumhal kah lungnah neh nang kan lungnah tih sitlohnah neh nang kan dangrhoek tangloeng coeng.
Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati, “Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire. Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
4 Israel oila nang te koep kan thoh vetih na thoo bitni. Na kamrhing te koep na oi vetih lamnah dongah na luem doela na pawk bitni.
Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli; mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu, ndipo mudzapita kukavina nawo anthu ovina mwachimwemwe.
5 Samaria tlang ah misur koep na phung te a phung, a phung uh vetih a poek a yak uh ni.
Mudzalimanso minda ya mpesa pa mapiri a Samariya; alimi adzadzala mphesa ndipo adzadya zipatso zake.
6 Ephraim tlang kah aka dawn rhoek loh, “Thoo uh lamtah mamih kah Pathen BOEIPA taengah Zion la cet uh sih,” tila a hoe uh khohnin khaw om bitni.
Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula pa mapiri a Efereimu nati, ‘Tiyeni tipite ku Ziyoni, kwa Yehova Mulungu wathu.’”
7 BOEIPA loh he ni a. thui. Jakob ham tamhoe uh lamtah kohoenah neh hlampan uh. Namtom boeilu te yaak sak lamtah a thangthen neh, “BOEIPA aw na pilnam Israel kah a meet te khang laeh,” ti saeh.
Yehova akuti, “Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo, fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse. Matamando anu amveke, ndipo munene kuti, ‘Yehova wapulumutsa anthu ake otsala a Israeli.’
8 Amih te tlangpuei khohmuen lamloh kang khuen coeng he. Te dongah amih te diklai a hlaep lamloh ka coi ni. Amih taengkah mikdael neh khokhaem khaw, aka vawn neh cacun khaw hlangping la muep ha mael uh rhenten ni.
Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto, ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi. Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
9 Rhahnah neh ha pawk uh cakhaw amih huithuinah neh ka khuen ni. Amih te soklong tui ah ka pongpa puei vetih, a thuem longpuei ah paloe uh mahpawh. Israel taengah ana pa la ka om tih Ephriam te ka caming ni.
Adzabwera akulira; koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza. Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo. Chifukwa ndine abambo ake a Israeli, ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
10 Namtom rhoek BOEIPA ol he hnatun uh. Khohla bangsang kah sanglak ah khaw puen uh lamtah Israel khuikah a thaekyak te thui pah. Anih te a coi vetih a tuping aka dawn bangla anih te a ngaithuen ni.
“Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
11 BOEIPA loh Jakob te a lat tih anih lakah tlungluen kut lamloh a tlan coeng.
Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
12 Ha pawk uh vaengah Zion hmuensang ah tamhoe uh ni. BOEIPA kah thennah dongah, cangpai dongah, misur thai dongah, situi dongah, boiva neh saelhung ca dongah hlampan uh ni. A hingah te khosul dum bangla om vetih a kha koep ham koei mahpawh.
Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni; adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova. Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta, ana ankhosa ndi ana angʼombe. Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino, ndipo sadzamvanso chisoni.
13 Te vaengah oila khaw tongpang neh patong taengah lamnah neh thikat la a kohoe ni. Amih kah nguekcoinah te omngaihnah la ka hoi pah vetih amih te ka hloep ni. Amih kah kothaenah yueng la amih ko ka hoe sak ni.
Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala. Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala. Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo; ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
14 Khosoih rhoek kah hinglu te maehhloi neh ka sulpuem sak vetih ka pilnam khaw ka thennah neh cung uh ni. He tah BOEIPA kah olphong ni.
Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,” akutero Yehova.
15 BOEIPA loh he ni a. thui. Ramah ah rhathinah ol a yaak. Rakhel tah a ca rhoek ham kosidung kah rhahnah neh rhap coeng. A ca rhoek a om pawt dongah kohlawt ham khaw a aal coeng.
Yehova akuti, “Kulira kukumveka ku Rama, kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake. Sakutonthozeka chifukwa ana akewo palibe.”
16 BOEIPA loh he ni a. thui. Na ol te rhahnah lamloh, na mik te khaw mikphi lamloh tuem laeh. BOEIPA kah olphong bangla na khoboe ham thapang om vetih thunkha khohmuen lamloh ha mael uh bitni.
Yehova akuti, “Leka kulira ndi kukhetsa misozi pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,” akutero Yehova. “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
17 BOEIPA kah olphong bangla na hmailong ham ngaiuepnah om tangloeng coeng tih ca rhoek khaw a khorhi la mael uh bitni.
Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,” akutero Yehova. “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.
18 Ephraim kah a rhaehba te a yaak rhoela ka yaak coeng. Kai nan thuituen vaengah a phaep noek pawh vaitoca bangla n'thuituen coeng. Namah tah BOEIPA ka Pathen la na om dongah kai m'mael sak lamtah ka mael pawn eh.
“Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti, ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva. Koma inu mwatiphunzitsa kumvera. Mutibweze kuti tithe kubwerera, chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
19 Ka mael hnukah ni damti coeng. Ka hlit dongkah kutpaeng khaw ka ming phoeiah ni ka yah pueng. Ka camoe lamkah kokhahnah te ka phueih tih ka hmaithae coeng.
Popeza tatembenuka mtima, ndiye tikumva chisoni; popeza tazindikira ndiye tikudziguguda pachifukwa. Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
20 Ephraim he kamah taengkah oingaih capa maco? Anih te ka thui dingdoeng vaengah khaw hlahmaenah camoe ni. Te dongah anih te ka poek rhoe ka poek pueng. Ka ko anih hamla umya tih anih te haidam rhoela ka haidam coeng. He tah BOEIPA kah olphong ni.
Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa, mwana amene Ine ndimakondwera naye? Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukumbukirabe. Kotero mtima wanga ukumufunabe; ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,” akutero Yehova.
21 Namah ham pangkae te ling lamtah miknawt khaw namah ham khueh laeh. Longpuei lamhlawn te na lungbuei ah dueh lamtah pongpa rhoe pongpa laeh. Israel oila ha mael lamtah na khopuei ah he ha mael laeh.
“Muyike zizindikiro za mu msewu; muyimike zikwangwani. Yangʼanitsitsani msewuwo, njira imene mukuyendamo. Bwerera, iwe namwali wa Israeli, bwerera ku mizinda yako ija.
22 Hnukmael canu te me hil nim na dongpam ve? BOEIPA loh diklai dongah a thai la a suen vetih huta tongpa loh a vael bitni.
Udzakhala jenkha mpaka liti, iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika? Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”
23 Israel Pathen caempuei BOEIPA loh he ni a. thui. He ol he Judah kho khui neh a khopuei rhoek khuiah koep a thui uh vaengah amih khuikah thongtla te kai taengla ha mael ni. Duengnah tlang cim tolkhoeng dongkah BOEIPA loh nang n'uem nawn saeh.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
24 Te vaengah Judah amah neh a khopuei boeih ah tun kho a sak uh lopho khaw tuping neh ha hlah uh ni.
Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
25 Buhmueh rhathih kah a hinglu te ka sulpuem sak vetih aka kha kah hinglu te boeih ka cung sak ni.
Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
26 Ka haenghang vaengah he khaw ka sawt tih ka ih khaw kai ham tui mai.
Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
27 BOEIPA kah olphong khohnin ha pawk coeng ke. Israel imkhui neh Judah imkhui khaw, hlang kah tiingan neh rhamsa kah tiingan khaw ka phul pueng ni.
“Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
28 Phuk ham neh phil ham khaw, koengloeng ham neh milh sak ham khaw, thaehuet ham khaw amih ka hak thil bangla thoeng van. Te dongah thoh ham neh phung ham khaw amih te ka hak thil ni. He tah BOEIPA kah olphong ni.
Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
29 Te khohnin ah tah, “A napa rhoek loh thaihkang a caak uh tih a ca rhoek a no yaa,” ti uh voel mahpawh.
“Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti, “Makolo adya mphesa zosapsa, koma mano a ana ndiye achita dziru.
30 Tedae hlang he amah kathaesainah dongah ni a. duek eh. Thaihkang aka ca hlang boeih tah a no yaa ni.
Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
31 BOEIPA kah olphong khohnin tah ha pawk coeng ke. Israel imkhui taeng neh Judah imkhui taengah paipi thai ka saii ni.
“Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
32 Egypt kho lamloh amih khuen ham a kut ah ka talong khohnin vaengkah a napa rhoek neh ka saii paipi bang te moenih. Amih loh ka paipi he phae cakhaw kai amih te ka yuunah ngawn ta. He tah BOEIPA kah olphong ni.
Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto; chifukwa anaphwanya pangano langa, ngakhale ndinali mwamuna wawo,” akutero Yehova.
33 Tedae paipi he Israel imkhui neh ka saii phoeikah khohnin ah tah ka olkhueng he amih kotak khuiah ka paek vetih a lungbuei ah ka daek pah ni. He tah BOEIPA kah olphong ni. Amih taengah Pathen la ka om vetih amih khaw kamah taengah pilnam la om uh ni.
“Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.
34 Hlang loh a hui te koep tukkil uh pawt vetih hlang loh a manuca te, “BOEIPA te ming laeh,” ti nah mahpawh. Amih te tanoe lamloh kangham duela kai boeih m'ming uh ni. He tah BOEIPA kah olphong ni. Amih kathaesainah te khodawk ka ngai vetih a tholhnah te ka poek voel mahpawh.
Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake, kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’ chifukwa onse adzandidziwa Ine, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,” akutero Yehova. “Ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
35 BOEIPA loh he ni a. thui. Khothaih kah vangnah ham khomik, khoyin kah vangnah ham hla neh aisi kah khosing khaw a khueh. Tuitunli te a kueng tih a tuiphu khaw kawk coeng. A ming tah caempuei BOEIPA ni.
Yehova akuti, Iye amene amakhazikitsa dzuwa kuti liziwala masana, amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku, amene amavundula nyanja kuti mafunde akokome, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
36 He tah BOEIPA kah olphong ni. Oltlueh he ka mikhmuh lamloh khum koinih hnin takuem ka mikhmuh ah namtu la aka om Israel tiingan khaw kangkuen uh ni.
Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
37 BOEIPA loh he ni a. thui. Vaan ke a so la a nueh uh thai tih diklai a yung hmui duela a khe uh thai mak atah Israel kah tiingan boeih te a saii cungkuem dongah ka hnawt van bitni. He tah BOEIPA kah olphong ni.
Yehova akuti, “Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo. Ngati patapezeka munthu amene angathe kupima zakuthambo nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”
38 BOEIPA kah olphong khohnin ha pawk coeng ke. Te vaengah bangkil vongka kah Hananel rhaltoengim lamloh BOEIPA ham khopuei a thoh ni.
“Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
39 Gareb som te a hmai la rhilam rhui sen a toe thil vetih Goah duela a vael ni.
Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
40 Rhok neh maehhloi aka om tuikol boeih, lohmali neh hmangrhong boeih khaw, Kidron soklong neh khothoeng kah marhang vongka bangkil duela BOEIPA ham hmuencim la om ni. Kumhal duela koep kuel pawt vetih koengloeng voel mahpawh.
Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”