< Jeremiah 10 >

1 Israel imkhui nangmih taengah BOEIPA loh a thui olka te ya uh.
Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
2 BOEIPA loh he ni a. thui. Namtom kah longpuei te awt uh boel lamtah vaan miknoek nen khaw rhihyawp uh boeh. Te lamlong ni namtom rhoek khaw a rhihyawp uh.
Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
3 A honghi pilnam kah khosing dongah he duup lamkah thing ni kutthai kut kah bibi loh tubael neh a saii ngawn.
Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
4 ngun neh, sui neh a sawtthen sak tih, thicung neh thilung neh a khing dongah lol voel pawh.
Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
5 Te te uitang lo kah vatai bangla om tih cal thai pawh. A kan uh thai pawt dongah a koh la a koh uh. Te te rhih uh boeh. Thaehuet uh thai pawt tih a voelphoeng ham khaw a om uh moenih.
Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
6 BOEIPA namah bang moenih. Namah tah na len tih na ming khaw, thayung thamal dongah tanglue pai.
Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
7 Namtom kah manghai namah aka rhih pawt te unim? Namtom hlangcueih boeih khuikah khaw na taengah naep ngawn tih a ram pum ah namah bang a om moenih.
Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
8 Pakhat la dom uh thae tih a hong thing kah thuituennah dongah ang uh.
Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
9 Tarshish lamkah cak ben hang khuen tih Uphaz lamkah sui khaw kutthai kah a bibi mai ni. Te boeih te aka picai kah kut long ni hlangcueih kah bibi bangla a pueinak te a thim neh daidi neh a loeih pah.
Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
10 Tedae BOEIPA amah he oltak Pathen, mulhing Pathen neh kumhal manghai ni. A thinhul dongah diklai hinghuen tih a kosi te namtom loh ueh pawh.
Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
11 Amih pathen rhoek taengah khaw he tlam he thui uh. Amih loh vaan neh diklai a saii pawt dongah te rhoek tah diklai lamkah neh vaan hmui lamloh hmata uh ni.
“Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
12 A thadueng neh diklai a saii, a cueihnah neh lunglai a thoh tih a lungcuei neh vaan khaw a dih.
Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
13 Vaan kah tui len khaw a ol a paek tih diklai khobawt lamkah khoboei khaw a pongpa sak. Diklai te rhaek neh khotlan a saii pah tih a thakvoh lamloh khohli a thoeng sak.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
14 Hlang boeih he mingnah dongah rhawm coeng tih aka picai boeih khaw mueithuk dongah koh coeng. A muei hong neh a khuiah hil om pawh.
Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
15 Amih ahonghi neh a hohap kah khoboe tah amamih kah cawhnah tue vaengah milh bitni.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
16 Jakob kah hamsum tah he bang moenih. Amah kah rho la Israel koca boeih aka hlinsai tah a ming khaw caempuei BOEIPA ni.
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
17 Vongup ah aka om, aka om loh na hnocun te diklai lamloh coi uh laeh.
Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
18 BOEIPA loh he ni a. thui. Tahae ah diklai khosa rhoek te voeikhat la ka dong coeng he. Amih soah ka daengdaeh daengah ni a. hmuh uh eh.
Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
19 Anunae kai aih he, ka pocinah dongah ka hmasoe khaw nue coeng. Tedae tloh he ka phuei mai eh ka ti coeng.
Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
20 Ka dap khaw a rhoelrhak tih ka liva khaw boeih pat. Ka ca rhoek khaw kai lamloh coe uh tih om uh pawh. Ka dap aka tuk tih ka himbaiyan aka thoh khaw om voel pawh.
Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
21 Boiva aka dawn khaw a dom coeng tih BOEIPA te toem uh pawh. Te dongah ni cangbam uh pawt tih a rhamtlim khaw boeih a taekyak pah.
Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
22 Tlangpuei khohmuen lamkah hinghuennah puei loh Judah khopuei te khopong kah pongui khuirhung la khueh ham olthang ol ha pawk coeng ke.
Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
23 BOEIPA aw, a longpuei te hlang kah pawt tih hlang dongah a pongpa kolla a khokan a rhoekbah te khaw ka ming.
Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
24 Aw BOEIPA kai he tiktamnah nen mah n'thuituen lamtah na thintoek nen boel saeh. Kai nan hnop ve.
Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
25 Nang aka ming pawh namtom so neh na ming aka phoei pawt cako soah na kosi te hawk mai. Jakob te a yoop la a yoop uh coeng. Te dongah amah te a khah uh tih a tolkhoeng te a pong sakuh.
Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.

< Jeremiah 10 >