< Isaiah 59 >
1 Khang hamla BOEIPA kut loh ngun pawt tih a yaak ham a hna a bing moenih.
Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 Tedae nangmih kathaesainah he tuiphih rhaboe la nangmih laklo neh na Pathen laklo ah om. A yaak ham akhaw nangmih kah tholhnah kongah ni nangmih taeng lamkah maelhmai a thuh.
Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
3 Na kut ah thii neh, na kutdawn te thaesainah neh nok uh. Na hmuilai loh a honghi a thui tih na ol te dumlai la muep.
Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 Duengnah neh aka khue pawt tih uepomnah neh lai aka tloek pawt tah, hinghong dongah pangtung tih a poeyoek la cal. Thakthaenah a yom tih boethae a cun.
Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 Rhulthae duei te a khaeh uh tih bumba rhui a yen uh. A duei aka ca tah duek. A hep vaengah rhulthae la khae.
Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Amih kah rhui te himbai la poeh hae pawt tih amamih kah bibi nen khaw khuk uh tloel. Amih kah khoboe khaw boethae kah khoboe ni. A kut dongkah bisai khaw kuthlahnah ni.
Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 A kho te boethae taengla yong paitok tih ommongsitoe kah thii kingling ham tokthuet uh. Amih kopoek he boethae kah kopoek neh rhoelrhanah ni. Amih kah longpuei ah pocinah om.
Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 Rhoepnah longpuei te ming uh pawt tih a namtlak ah tiktamnah om pawh. A hawn te amamih taengla a kawn sak uh tih a sokah aka pah boeih loh rhoepnah ming voel pawh.
Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 Te dongah tiktamnah he mamih lamloh lakhla tih duengnah loh mamih ng'kae voel pawh. Vangnah te n'lamtawn uh dae hmuep coeng ke. Khosaeng yueng la khohmuep ah m'pongpa uh.
Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Mikdael bangla pangbueng m'phatuem uh tih mik aka mueh bangla m'phatuem uh. Khothun ah khaw hlaemhmah bangla, thaom thathueng lakli ah hlang duek bangla m'paloe uh.
Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Mamih he vom bangla boeih n'kawk uh tih vahui bangla n'tuk la n'tuk uh. Tiktamnah te n'lamtawn dae om voel pawt tih khangnah khaw mamih lamloh hla coeng.
Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Kaimih kah boekoek he na hmaiah pung tih kaimih kah tholhnah tah kamamih taengah phoe coeng. Mamih kah boekoek he mamih taengah om tih mamih kathaesainah te khaw m'ming uh.
Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 BOEIPA taengah boekoek neh basa tih mamih kah Pathen hnuk lamloh balkhong coeng. Hnaemtaeknah neh a cal phoeiah koeknah la vawn tih a lungbuei lamkah a honghi ol te a thuep.
Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 Tiktamnah loh a hnuk la balkhong coeng tih duengnah loh a hlahloei ah pai. Oltak khaw toltung ah paloe tih oldueng loh a kun ham coeng pawh.
Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Oltak aka om te a hmaai tih boethae lamkah aka nong khaw a buem hnap. Tedae tiktamnah a tal te BOEIPA loh a hmuh vaengah a mik ah a lolh pah.
Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 Hlang a om pawt te a hmuh vaengah a doo pawt te khaw hal coeng. Tedae amah ham khaw amah bantha long ni a khang pah tih a duengnah long ni amah a talong.
Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 Duengnah te caempho la a bai tih, khangnah lumuek te a lu dongah a muek. Phulohnah himbai te hnicu la a bai tih thatlainah neh hnikul bangla khuk uh.
Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 A khoboe bangla kosi te a rhal taengah, a thaphu te a thunkha taengah a thuung tangloeng ni. Sanglak rhoek taengah khaw a thaphu te a thuung ni.
Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 BOEIPA ming te khotlak lamloh, a thangpomnah te khomik khocuk lamloh a rhih uh ni. Hlang aka va tuiva bangla ha pawk vaengah anih te BOEIPA mueihla loh a rhaelrham sak.
Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
20 Aka tlan kung loh Zion neh boekoek aka mael tak Jakob te a paan ni. BOEIPA kah olphong ni.
“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
21 Kamah kah paipi he kamah long ni amih taengah ka khueh. BOEIPA loh, “Ka mueihla he nang soah, ka ol he na ka dongah ka khueh vetih na ka lamloh, na tiingan kah ka lamloh, na tiingan kah tiingan patoeng kah ka lamkah khaw nong mahpawh,” a ti. BOEIPA loh tahae lamkah neh kumhal ham ni a thui.
Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.