< Hosea 2 >

1 Na manuca rhoek te, 'Ka pilnam, na ngannu rhoek te 'Kan haidam 'ti nah.
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 Na nu te ho rhoe ho laeh. Anih te kai yuu pawt tih kai khaw a va moenih. A pumyoihnah te a mikhmuh lamloh, a samphainah a rhangsuk laklo lamkah khoe laeh saeh.
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 Anih te pumtling la ka hlik vetih a thang hnin kah bangla amah ka khueh tarha ve. Anih te khosoek bangla ka khueh vetih rhamrhae khohmuen la ka khueh phoeiah tuihalh neh ka duek sak ni.
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 Amih pumyoi ca rhoek mai te, a ca rhoek te khaw ka haidam mahpawh.
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 A manu te cukhalh pai tih amih a yom te yak. Ka buh, ka tui, ka tumul, ka hlamik, ka situi neh ka tuiok aka pae ka lungnah hnukah ni ka caeh eh?,” a ti.
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Te dongah kamah loh a longpuei te hling neh ka buk pah. A vongtung te ka biing pah vetih a hawn hmu voel mahpawh.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 A lungnah rhoek te a hloem dae amih te kae mahpawh. Amih te a tlap akhaw hmu mahpawh. Te vaengah, “Ka cet vetih lamhma kah ka va taengah ka mael ni. Kai hamla tah then ngai mai coeng.
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 Kai loh anih taengah cangpai, misur thai, situi khaw ka paek tih anih soah cak khaw ka kum sak dae sui te Baal hamla a khueh uh.
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 Te dongah amah tue vaengah ka cangpai neh a khoning vaengkah ka misur thai te ka lat pah vetih ka loh pah ni. A yah a khuk nah ka tumul neh ka hlamik khaw ka lat ni.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 Te phoeiah a yah te a hlang ngaih mikhmuh ah ka poelyoe pah pawn vetih hlang loh anih te ka kut lamkah huul thai mahpawh.
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 A omthennah, a khotue, a hlasae neh a Sabbath khaw, a tingtunnah boeih khaw boeih ka paa sak ni.
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 A misur neh a thaibu khaw ka pong sak ni. “Te rhoek te kamah kah pumyoih phu la ka hlang ngaih rhoek loh kai taengah m'paek uh,” a ti. Te cakhaw te te duup la ka khueh vetih kohong mulhing loh a caak ni.
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 Amih taengah a phum bangla Baal kah khohnin khaw anih taengah ka cawh ni. A hnaii neh a hnaphaa a thawn tih a hlang ngaih hnukah cet dae kai, BOEIPA kah olphong te a hnilh.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 Te dongah kamah loh anih te ka hloih ni ne. Tedae amah te khosoek la pha sak phoeiah ni a lungbuei ah ka voek eh.
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 Te lamloh a misurdum te amah taengla ka paek vetih Akor kol te ngaiuepnah thohka la om ni. Te vaengah a camoe tue vaengkah bangla pahoi oei vetih Egypt kho lamloh a caeh hnin bangla om ni.
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 BOEIP A kah olphong te a khohnin neh a pha vaengah tah ka va la nan khue vetih kai taengah, “Kai kah Baal,” la na khue voel mahpawh.
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 Baal ming te a ka lamloh ka khoe pah vetih a ming te poek voel mahpawh.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 Te khohnin ah tah amih ham paipi te kohong mulhing neh, vaan kah vaa neh, diklai rhulcai neh ka saii pah ni. Diklai lamkah lii, cunghang neh caemtloek te ka bawt sak vetih amih te ngaikhuek la ka yalh sak ni.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 Nang te kamah ham kumhal duela kam bae vetih duengnah neh, tiktamnah neh, sitlohnah neh, haidamnah neh nang te kamah hamla kam bae ni.
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 Nang te kamah hamla uepomnah neh kam bae van daengah ni BOEIPA te na ming eh.
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 Te khohnin te a pha vaengah BOEIPA kah olphong te ka doo vetih vaan te khaw ka doo ni. Amih long khaw diklai te a doo uh ni.
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 Diklai long khaw cangpai misur thai neh situi te a doo vetih amih loh Jezreel te a doo ni.
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 Anih te kamah hamla lohma ah ka soem vetih a haidam pawt te ka haidam ni. Nang Laomi te ka pilnam ka ti vetih anih long khaw ka Pathen a ti ni.
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”

< Hosea 2 >