< Suencuek 50 >

1 Te vaengah Joseph loh a napa maelhmai a bakop thil tih a soah a rhah neh a mok.
Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira.
2 Te phoeiah Joseph loh a napa te sihluk ham a sal siboei rhoek te a uen tih siboei rhoek loh Israel te si a hluk uh.
Ndipo Yosefe analamula antchito ake a chipatala kuti akonze thupi la Israeli ndi mankhwala kuti lisawole. Kotero antchitowo anakonzadi thupilo.
3 Sihluknah khohnin te khohnin lipkip a di ham a om dongah khohnin a soep vanneh rhok te Egypt rhoek loh khohnin sawmrhih a rhah uh.
Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri.
4 Rhahnah khohnin a poeng vaengah Joseph loh Pharaoh im la, “Na mikhmuh ah mikdaithen ni ka dang atah Pharaoh kah hna kaep ah bet ka thui mai eh.
Yosefe atatha kulira maliro a abambo ake, anayankhula kwa nduna za Farao nati, “Ngati mungandikomere mtima, chonde mundiyankhulire kwa Farao kumuwuza kuti,
5 A pa loh, ‘Ka duek atah Kanaan kho ah kamah ham ka vueh tangtae phuel ah pahoi nan up ni,’ a ti tih kai he n'toemngam sak oeh dongah bet ka cet saeh lamtah a pa te ka up phoeiah ka bal mai eh,” a ti nah.
‘Abambo anga anandilumbiritsa ndipo anati, ‘Ndatsala pangʼono kumwalira, ukandiyike mʼmanda amene ndinakumba ndekha mʼdziko la Kanaani.’ Tsono mundilole ndikayike abambo anga, ndipo ndikabweranso.’”
6 Pharaoh long khaw, “Na toemngam vanbangla cet lamtah na pa te up dae,” a ti nah.
Farao anati, “Pita ukayike abambo ako monga anakulumbiritsa kuti uchite.”
7 Te dongah Joseph te a napa up ham a caeh hatah Pharaoh kah sal boeih neh a im kah a hamca rhoek long khaw, Egypt kho kah a hamca boeih long khaw,
Kotero Yosefe anapita kukayika abambo ake. Nduna zonse za Farao, akuluakulu a bwalo lake ndi akuluakulu a ku Igupto, anapita naye pamodzi.
8 Joseph cako boeih neh a manuca rhoek long khaw, a napa cako long khaw a thak puei uh. Camoe neh a boiva, saelhung bueng te Goshen kho ah a caehtak uh.
Anapitanso onse a pa banja la Yosefe ndi abale ake ndi onse amene anali a pa banja la abambo ake. Ana awo okha, nkhosa ndi ngʼombe zinatsala ku Goseni
9 Te dongah anih taengah aka cet te leng khaw, marhang caem khaw lambong yet la muep om.
Asilikali okwera pa magaleta ndi asilikali a pa akavalo anapita nayenso pamodzi. Linali gulu lalikulu.
10 Tedae Jordan rhalvangan kah Atad te a pha uh vaengah rhaengsaelung neh bungbung mat a rhaengsae uh tih a napa ham nguekcoinah te hnin rhih a yaeh uh.
Atafika pa Goreni ha-Atadi, pafupi ndi Yorodani, anachita mwambo waukulu wa maliro. Choncho Yosefe analira maliro a abambo ake masiku asanu ndi awiri.
11 Tedae Atad ah a nguekcoinah te Kanaan kho kah khosa rhoek loh a hmuh uh vaengah, “Hekah he Egypt rhoek loh mat a nguekcoinah ni,” a ti uh dongah Jordan rhalvangan kah a ming te Abelmizaim la a khue.
Akanaani amene ankakhala ku Goreni ha-Atadi ataona mwambo wa maliro anati, “Aigupto ali ndi mwambo wa maliro a akulu.” Ndi chifukwa chake malo amenewo a pafupi ndi Yorodani amatchedwa Abeli-Mizraimu.
12 Te dongah a uen vanbangla Israel ham a ca rhoek loh a saii uh tih,
Choncho ana a Yakobo anachita monga momwe abambo awo anawalamula:
13 Kanaan kho la a khuen uh. Te phoeiah Abraham loh phuel khohut la Khitti Ephron kah khohmuen Mamre ah a lai Makpelah lo kah lungko ah a up uh.
Ndiye kuti ana a Yakobo anamunyamula kupita naye ku Kanaani kuti akamuyike mʼphanga limene lili mʼmunda wa Makipela pafupi ndi Mamre. Abrahamu anagula mundawo kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
14 Joseph neh a manuca rhoek khaw, a napa up ham anih taengah aka cet boeih long khaw a napa te a up phoeiah Egypt la bal uh.
Atatha kuyika abambo ake, Yosefe anabwerera ku Igupto, pamodzi ndi abale ake ndi onse amene anapita nawo kukayika abambo ake.
15 Tedae a napa a duek coeng dongah Joseph te a manuca rhoek loh a hmuh uh vaengah, “Joseph he mamih taengah a konaeh koinih anih taengah boethae n'saii uh boeih te n'thuung rhoe n'thuung ni,” a ti uh.
Abale ake a Yosefe ataona kuti abambo awo amwalira, anati, “Nanga tidzatani ngati Yosefe anatisungira mangawa nafuna kutibwezera pa zoyipa zonse zimene tinamuchitira?”
16 Te dongah Joseph taengla ol a uen uh tih, “Na pa loh a duek hlan ah,
Motero anatumiza mawu kwa Yosefe kuti, “Abambo anu anasiya malangizo asanafe nati:
17 ‘Joseph te, Na manuca rhoek kah dumlai khaw, nang a thae la n'saii uh vaengkah tholhnah te khaw phuei mai ti nah,’ a ti tih n'uen dongah na pa Pathen sal rhoek kah boekoeknah te phuei mai,” a ti nah uh tih a thui uh vaengah Joseph rhap.
‘Zimene mudzayenera kunena kwa Yosefe ndi izi: Ndikukupempha kuti uwakhululukire abale ako cholakwa chawo ndi machimo awo, popeza anakuchitira zoyipa.’ Ndiye tsopano chonde tikhululukireni zolakwa zimene ife akapolo a Mulungu wa abambo anu tinachita.” Yosefe atangomva mawu amenewa anayamba kulira.
18 Te dongah a manuca rhoek khaw cet uh tih a hmai ah bakop uh tih kaimih he nang kah sal ni he a ti uh.
Kenaka abale ake anabwera nadzigwetsa pansi pamaso pake, nati, “Ife ndife akapolo anu.”
19 Tedae Joseph loh, “Kai he Pathen hnukthoi a? Rhih uh boeh saw.
Koma Yosefe anawawuza kuti, “Musachite mantha. Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu?
20 Nangmih loh kai taengah boethae la nan taeng uh cakhaw Pathen loh tahae khohnin kah bangla pilnam muep hing sak ham te a then la a moeh coeng.
Inu munafuna kundichitira zoyipa, koma Mulungu anasandutsa zoyipazo kuti zikhale zabwino kuti zikwaniritsidwe zimene zikuchitika panozi, zopulumutsa miyoyo yambiri.
21 Te dongah rhih uh boeh. Nangmih khaw, na ca rhoek khaw kan cangbam bitni,” a ti nah tih amih lungbuei te hloep ol a thui pah.
Kotero, musachite mantha. Ine ndidzasamalira inu pamodzi ndi ana anu omwe.” Tsono iye anawalimbitsa mtima powayankhula moleza mtima.
22 Joseph khaw Egypt ah a napa kah a cako neh kho a sak. Te vaengah Joseph te kum pasoi neh kum rha hing.
Yosefe anakhala mu Igupto pamodzi ndi banja lonse la abambo ake. Anakhala ndi moyo zaka 110
23 Te dongah Joseph loh Ephraim ca rhoek a khongthum duela a hmuh. Manasseh capa Makir ca rhoek khaw Joseph khuklu dongah a cun uh.
ndipo anaona mʼbado wachitatu wa ana a Efereimu. Yosefe anatenganso ana a Makiri, mwana wa Manase kukhala ngati ana a mʼbanja lake.
24 Te vaengah Joseph loh a manuca rhoek la, “Kai ka duek cakhaw Pathen loh nangmih n'hip khaw n'hip vetih nangmih te tahae kah kho lamkah Abraham, Isaak neh Jakob ham a toemngam tangtae khohmuen la n'khuen bitni,” a ti nah.
Kenaka Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndatsala pangʼono kufa. Koma mosakayika Mulungu adzakuyangʼanirani nadzakutengani kukutulutsani mʼdziko lino kupita ku dziko limene Iye analonjeza kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.”
25 Te dongah Joseph loh Israel ca rhoek te a toemngam sak tih, “Nangmih te Pathen loh n'hip rhoe la n'hip vaengah he lamkah ka rhuh na khuen uh ni,” a ti nah.
Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israeli lumbiro nati, “Lonjezani kuti Mulungu akadzakusungani mudzanyamula mafupa anga kuwachotsa ku malo kuno.”
26 Joseph he kum pasoi neh a lang a lo ca vaengah duek tih a rhok te si a hluk uh phoeiah Egypt kah thingkawng dongah a khueh uh.
Choncho Yosefe anafa ali ndi zaka 110. Motero iwo atakonza thupi lake ndi mankhwala kuti lisawole, analiyika mʼbokosi ku Igupto.

< Suencuek 50 >