< Ephisa 6 >

1 Ca rhoek, Boeipa ah na manu na napa te olngai pah. He tah a ol dueng ni.
Inu ana, mverani makolo anu mwa Ambuye, pakuti zimenezi ndi zoyenera.
2 Na nu neh na pa te hinyah lah. Te tah olkhueh neh olpaek lamhma la om.
“Lemekeza abambo ndi amayi ako.” Limeneli ndi lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo.
3 Te daengah ni nang taengah a then la ha om vetih diklai ah hingsennah na dang eh.
Ngati ulemekeza abambo ako ndi amayi ako, “zinthu zidzakuyendera bwino ndipo udzasangalala ndi moyo wautali pa dziko lapansi.”
4 Pa rhoek long khaw na ca rhoek te a thintoek sak boeh tedae amih te Boeipa kah hlinsainah neh rhalrhingnah dongah cuncah uh.
Abambo musakwiyitse ana anu; mʼmalo mwake, muwalere mʼchiphunzitso ndi mʼchilangizo cha Ambuye.
5 Sal rhoek, pumsa kah na boei rhoek taengah rhihnah neh olngai uh. Na thinko moeihoeihnah neh thuennah neh Khrih taengkah bangla omuh.
Inu antchito, mverani mabwana anu mwaulemu ndi mwamantha ndi moona mtima, monga momwe mungamvere Khristu.
6 Mikhmuh dongkah kolopatai rhoek banglam pawt tih hinglu lamloh Pathen kah kongaih aka saii Khrih kah sal rhoek la omuh.
Musawamvere pamene akukuonani kuti akukomereni mtima, koma ngati akapolo a Khristu ochita chifuniro cha Mulungu kuchokera mu mtima mwanu.
7 Hlang taengah pawt tih boeipa taengkah bangla lunghoihnah neh salbi uh.
Tumikirani ndi mtima wonse, ngati kuti mukutumikira Ambuye, osati anthu.
8 A then khat khat a saii te rhip ming saeh. Sal long khaw, aka loeih long khaw Boeipa taeng lamloh amah la a dang bitni.
Inu mukudziwa kuti Ambuye adzamupatsa munthu aliyense mphotho chifukwa cha ntchito yake yabwino imene anagwira, kaya munthuyo ndi kapolo kapena mfulu.
9 Boei rhoek nang khaw amah te te amih taengah saii uh. Amih na hihamnah te hlawt laeh. Amih rhoek neh nangmih kah boeipa tah vaan ah om tih a taengah maelhmai sawtnah khueh pawh tite ming uh.
Ndipo inu mabwana, muziwachitiranso chimodzimodzi antchito anu. Musamawaopseze, popeza mukudziwa kuti Mbuye wawo ndi wanunso, nonse Mbuye wanu ali kumwamba, ndipo Iyeyo alibe tsankho.
10 A tloihsoi ah boeipa neh a thadueng kah thaomnah dongah thaphoh uh.
Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye ndi mwa mphamvu zake zazikulu.
11 Rhaithae kah a lungpoek te na mah thai ham atah Pathen kah lungpok haica te bai uh.
Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana.
12 Thii neh pumsa kah hnueihnah te mamih taengah a om moenih. Tedae boeilu rhoek, saithainah, he yinnah khuikah diklai thaomnah, vaan ah halangnah mueihla ni m'pai thil uh. (aiōn g165)
Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. (aiōn g165)
13 Te dongah Pathen kah lungpok haica te muk uh tangloeng laeh. Te daengah ni khohnin thae vaengah khaw na tungaep thai vetih aka thoeng boeih te na pai thil thai eh.
Choncho valani zida zonse za Mulungu, kuti pamene tsiku loyipa kwambiri lifika, mudzathe kuyima chilili, ndipo mutatha kuchita zonse, mudzayimabe mwamphamvu.
14 Pai uh lamtah oltak neh na pumpu te yen uh. Te phoeiah duengnah rhangpho te bai uh.
Tsono imani mwamphamvu, mutamangira choonadi ngati lamba mʼchiwuno mwanu, mutavala chilungamo ngati chitsulo chotchinjiriza pa chifuwa.
15 Rhoepnah olthangthen dongkah sikimnah neh na kho te khom uh.
Valani Uthenga Wabwino wamtendere ku mapazi anu ngati nsapato.
16 Te phoeiah tangnah photling te muk uh. Te nen ni rhaithae kah thaltang a rhoh te boeih na thih uh thai eh.
Kuwonjezera pa zonsezi, nyamulani chishango cha chikhulupiriro, ndipo ndi chimenechi mudzatha kuzimitsa mivi yonse yoyaka moto ya oyipayo.
17 Te phoeiah khangnah lumuek neh mueihla cunghang te doe thiluh. Te tah Pathen kah olthui ni.
Valani chipewa cha chipulumutso ndi kutenga lupanga la mzimu, limene ndi Mawu a Mulungu.
18 Thangthuinah cungkuem neh rhenbihnah dongah a tue takuem ah Mueihla neh thangthui uh. He ham he khuituknah cungkuem nen khaw, hlangcim boeih ham rhenbihnah nen khaw hak uh.
Ndipo mupemphere mwa Mzimu nthawi zonse, mʼmitundu yonse ya mapemphero ndi zopempha. Ndipo pozindikira izi, khalani achangu kupempherera oyera mtima nthawi zonse.
19 Kai ham khaw thangthuiuh. Te daengah ni ka ka ongnah neh kai taengah olka m'paek vetih olthangthen kah olhuep te sayalh la ka phong thai eh.
Mundipempherere inenso, kuti nthawi iliyonse pamene nditsekula pakamwa panga, andipatse mawu kuti ndiwulule zinsinsi za Uthenga Wabwino mopanda mantha.
20 Te yueng la thirhui neh ka laipai. Te daengah ni a khuiah ka thui a kuek te tah ka sayalh van eh.
Ndine kazembe wa Uthenga Wabwinowu ngakhale ndili womangidwa mʼndende. Pempherani kuti ndilalikire mopanda mantha, monga ndiyenera.
21 Te daengah ni kai kawng he na ming uh van pueng eh. Ka saii boeih te thintlo manuca neh Boeipa dongah uepom tueihyoeih Tukhiko loh nangmih taengla ham phoe puei bitni.
Tukiko, mʼbale wanga wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye, adzakuwuzani zonse kuti inunso mudziwe mmene ndilili ndi zimene ndikuchita.
22 Amah te ham ni nangmih taengla anih kan tueih. Te daengah ni kaimih kawng te na ming vetih nangmih kah thinko te han hloep eh.
Ine ndikumutumiza kwa inu, kuti mudziwe za moyo wathu, ndi kuti akulimbikitseni.
23 Pa Pathen neh Boeipa Jesuh Khrih lamkah rhoepnah, tangnah neh lungnah tah manuca rhoek taengah om saeh.
Mtendere, chikondi pamodzi ndi chikhulupiriro kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi abale onse.
24 Lungvatnah tah mamih kah boeipa Jesuh Khrih te a cak la aka lungnah rhoek boeih soah om saeh.
Chisomo kwa onse amene amakonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosatha.

< Ephisa 6 >