< 2 Samuel 7 >
1 Manghai te amah im ah om tih kho a sak vaengah anih hamla a kaepvai kah a thunkha boeih te BOEIPA loh a duem sak.
Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
2 Te vaengah manghai loh tonghma Nathan taengah, “So lah, kamah tah lamphai im dongah kho ka sak coeng, tedae Pathen kah thingkawng tah himbaiyan khui ah sut ngol,” a ti nah.
mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
3 Te vaengah Nathan loh manghai te, “Na thinko khuikah aka om carhui te tah cet lamtah saii laeh, BOEIPA tah nang taengah om coeng,” a ti nah.
Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
4 Te kah khoyin ah om tih BOEIPA ol Te Nathan taengla a pawk hatah,
Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
5 “Cet lamtah ka sal David te thui pah. BOEIPA loh, 'Ka om nah ham ka im Te na sa aya?
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
6 Egypt lamkah Israel ca ka khuen khohnin lamloh tahae khohnin hil im khuiah kho ka sak moenih. Tedae dap khui neh dungtlungim khuiah ni ka om tih ka van.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
7 Israel ca rhoek boeih te kho tom ah ka caeh puei. Olka nen khaw Israel koca pakhat khaw ka voek a? Ka pilnam Israel te luem puei ham ka uen rhoek te, 'Balae tih kai ham tah lamphai im na sak pawh,’ ka ti.
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
8 Te dongah ka sal David te, “Caempuei rhoek kah BOEIPA loh, 'Kai loh nang Te boiva hnuk lamloh, tolkhoeng lamlom, ka pilnam soah neh Israel soah rhaengsang la om sak ham ni kan loh.
“Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
9 Kho tom ah na caeh te namah taengah ka om tih na mikhmuh lamkah na thunkha boeih te ka khoe coeng. Te dongah na ming te diklai hlanglen rhoek kah a ming bangla a tanglue la ka khueh ni.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
10 Ka pilnam ham neh Israel ham hmuen ka khueh pah vetih anih te ka phung ni. Te vaengah amah hmuen la om vetih tlai voel mahpawh. Lamhma kah bangla anih phaep ham khaw dumlai koca rhoek loh koei uh mahpawh.
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
11 Te khohnin van lamloh ka pilnam Israel soah lai aka tloek la kang uen coeng. Te dongah na thunkha cungkuem khui lamloh nang te kan duem sak ni. BOEIPA Te nang taengah a puen bangla BOEIPA loh nang ham im a thoh ni.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
12 Na khohnin a cup vaengah na pa rhoek taengla na khoem uh ni. Namah hnukkah na tii na ngan, na bung khui lamkah aka thoeng te ka thoh vetih a ram te ka pai sak ni.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
13 Ka ming ham Te anih loh im a sak ni vetih a ram kah ngolkhoel te kumhal duela ka cikngae sak ni.
Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
14 Kamah he a napa la ka om vetih, anih khaw ka ca la om ni. A paihaeh vaengah anih Te hlang kah caitueng neh, Adam ca rhoek kah tlohtat neh ka tluung ni.
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
15 Tedae ka sitlohnah he Saul taeng lamloh ka lat tih na mikhmuh lamloh ka khoe bangla anih taeng lamloh ka khoe mahpawh.
Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
16 Na im neh na ram tah na mikhmuh ah kumhal duela cak vetih na ngolkhoel khaw kumhal due a cikngae la om ni,” a ti,’ ti nah,” a ti nah.
Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
17 He ol boeih he olphong boeih vanbangla Nathan loh David taengla a thui pah.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
18 Te dongah manghai David te kun tih, BOEIPA hmaiah ngol. Te phoeiah, “Ka Boeipa Yahovah aw Kai he unim? he duela kai nang khuen ham akhaw, kai imkhui he me tlam a om.
Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
19 Hekah he ka Boeipa Yahovah kah na mikhmuh ah rhaidaeng pueng atah na sal kah imkhui te na thui mai. Ka Boeipa Yahovah aw hlang kah olkhueng he tah hlavak om coeng.
Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
20 Namah taengah thui ham khaw David loh ba nen nim a thap khovoeh ve. Na sal te ka Boeipa Yahovah namah loh na ming.
Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
21 Na ol kong ah ni na lungbuei kah bangla lennah cungkuem na saii. He ni na sal na ming sak.
Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
22 Te dongah ka Boeipa Yahovah na len pai. Kaimih hna neh boeih ka yaak uh vanbangla namah phoeiah tah namah bangla aka om om pawh, Pathen tloe khaw om pawh.
Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
23 Diklai ah Israel bangla, na pilnam aka tluk namtu pakhat khaw unim aka om? Te tah a pilnam la lat ham neh amah ming la khueh ham Pathen cet coeng. Na lennah na saii ham dongah na khohmuen ham tah na pilnam mikhmuh ah rhih uh pai. Te tah namtom Egypt neh a pathen rhoek taeng lamloh namah hamla na lat.
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
24 Na pilnam khaw namah ham, Israel khaw namah kah kumhal pilnam la na cikngae sak. Te dongah ni BOEIPA namah tah amih kah Pathen la na om pai.
Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
25 BOEIPA Pathen aw na sal ham neh a imkhui ham ol na thui coeng. Na thui bangla kumhal duela thoh puei lamtah saii laeh.
“Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
26 Te dongah BOEIPA Caempuei Pathen tah na ming kumhal duela len ti pai saeh. Israel so neh na sal David imkhui Te na mikhmuh ah cikngae la a om thil ni.
kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
27 Israel kah Caempuei Pathen BOEIPA namah loh na sal kah a hna te na hnacueh pah tih, 'Nang hamla im ka sa ni, ' a ti. Te dongah ni na taengah hekah thangthuinah neh thangthui ham khaw na sal kah a lungbuei loh a hmuh.
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
28 Ka Boeipa Yahovah namah tah Pathen la na om pai. Na ol khaw oltak la om tih, a then he ni na sal taengah na thui.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
29 Na sal imkhui te na mikhmuh ah kumhal om sak ham mulmet lamtah a yoethen sak. Ka Boeipa Yahovah na thui coeng dongah namah kah yoethennah neh na sal imkhui he kumhal duela a yoethen ni.
Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”