< 2 Manghai 22 >

1 Josiah he kum rhet a lo ca vaengah manghai tih Jerusalem ah sawmthum kum khat manghai. A manu ming tah Bozkath lamkah Adaiah canu Jedidah ni.
Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
2 BOEIPA mikhmuh ah a thuem a saii. A napa David kah longpuei cungkuem dongah pongpa tih banvoei bantang la phael pawh.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
3 Manghai Josiah kah kum hlai rhet dongla a pha vaengah tah manghai loh BOEIPA im kah cadaek Meshullam koca Azaliah capa Shaphan te a tah tih,
Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
4 “Khosoih puei Hilkiah taengla cet lamtah BOEIPA im kah a khuen tangka te cum sak saeh. Te te cingkhaa aka tawt loh pilnam taeng lamkah ni a. coi.
“Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
5 Te phoeiah BOEIPA im kah im bitat aka saii aka hung kut ah pae rhoe pae saeh. Te te BOEIPA im ah bi aka saii taeng neh im puut aka biing roek taengah,
Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
6 kutthai rhoek ham neh im aka sa rhoek ham khaw, aka biing ham neh thing lai ham khaw, im biing vaengkah lungrhaih lung ham khaw pae saeh,” a ti nah.
amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
7 Tedae amih khaw uepomnah neh a saii uh dongah amih kut dongah a paek tangka te amih taengah koep toem voel pawh.
Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
8 Te vaengah khosoih puei Hilkiah loh cadaek Shaphan taengah, “BOEIPA im ah olkhueng cabu ka hmuh,” a ti nah. Te phoeiah Hilkiah loh cabu te Shaphan taengah a paek tih a tae.
Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
9 Te phoeiah cadaek Shaphan te manghai taengla pawk tih manghai te ol a mael. Te vaengah, “Im khuikah a hmuh tangka te na sal rhoek loh a khok uh coeng. Te te BOEIPA im kah bi saii rhoek aka hung kut ah a paek uh coeng,” a ti nah.
Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
10 Cadaek Shaphan te manghai taengla puen tih, “Khosoih Hilkiah loh kai taengah cabu m'paek,” a ti nah. Te phoeiah te te Shaphan loh manghai mikhmuh ah a tae.
Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
11 Manghai loh olkhueng cabu dongkah ol te a yaak van neh a himbai te a phen coeng.
Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
12 Te dongah manghai loh khosoih Hilkiah, Shaphan capa Ahikam, Mikaiah capa Akbor, cadaek Shaphan neh manghai kah sal Asaiah te a uen tih,
Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
13 “Cet uh, kai ham neh pilnam ham khaw, Judah pum ham khaw BOEIPA te toem uh laeh. Cabu dongkah ol a hmuh dongah he BOEIPA kah kosi tah mamih taengah muep rhong coeng. He cabu olka he a pa rhoek lohngai uh pawh. Mamih ham a daek tah a cungkuem ah ngai ham om,” a ti nah.
“Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
14 Te dongah khosoih Hilkiah, Ahikam, Akbor, Shaphan neh Asaiah tah himbai aka khoem Harhas koca Tikvah capa Shallum yuu, tonghmanu Huldah taengla cet uh. Te vaengah anih te Jerusalem kah hnukthoi khopuei ah kho a sak tih amah te a voek uh.
Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
15 Te vaengah amih te, “Israel Pathen BOEIPA loh he ni a. thui. Kai taengla nangmih aka tueih hlang taengah thui pah.
Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
16 BOEIPA loh he ni a. thui. Kai loh he hmuen so neh a khuikah khosa rhoek soah khaw boethae ka khuen coeng. Cabu dongkah ol cungkuem te Judah manghai loh a tae coeng te.
‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
17 Kai n'toeng uh tih a kut dongkah bitat cungkuem neh kai veet hamla a tloe pathen taengah phum uh. Te dongah ka kosi loh he hmuen he a hlup tih daeh voel mahpawh.
Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
18 BOEIPA toem hamla nangmih aka tueih Judah manghai te a taengah Israel Pathen BOEIPA loh a thui ol he na yaak bangla thui pah.
Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
19 He hmuen so neh a khuikah khosa soah imsuep neh rhunkhuennah la om sak ham ka cal te na yaak vaengah na thinko phoena tih BOEIPA mikhmuh ah na kunyun coeng. Te vaengah na himbai te na phen tih ka mikhmuh ah na rhah khaw ka yaak bal coeng. He tah BOEIPA kah olphong ni.
Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
20 Te dongah kai loh nang te na pa rhoek taengla kan humcui sak bini ne. Na phuel ah ngaimong la na khoem uhvetih he hmuen soah ka khuen boethae cungkuem te na mik loh hmu mahpawh,” a ti nah. Te phoeiah manghai te ol a mael uh.
Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.

< 2 Manghai 22 >