< 1 Samuel 13 >

1 Saul a manghai kum neh Israel soah kum nit a manghai nen tah,
Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.
2 Israel hlang thawng thum te Saul loh amah ham a coelh. Te vaengah Mikmash kah Saul taeng neh Bethel tlang ah a thawng thawng om uh tih Benjamin Gibeah kah Jonathan taengah khaw a thawng thawng la om uh. Pilnam hlangrhuel rhoek te amah dap la boeih a tueih.
Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.
3 Geba kah Philisti khohung te Jonathan loh a tloek tih Philisti rhoek loh a yaak uh. Te dongah Saul loh kho takuem ah tuki a ueng tih, “Hebrew rhoek loh ya saeh,” a ti nah.
Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli.
4 Israel pum loh a yaak uh vaengah, “Saul loh Philisti khohung a tloek dongah Israel he Philisti ham a bo rhim coeng,” a ti uh. Te dongah pilnam khaw Gilgal kah Saul hnukah bukbuk pang uh.
Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.
5 Te dongah Philisti loh Israel te vathoh thil ham, leng thawng sawmthum neh marhang caem thawng rhuk neh pilnam te tuipuei tuikaeng kah laivin yet la taai uh. Te phoeiah cet uh tih Bethaven khothoeng Mikmash ah rhaeh uh.
Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni.
6 Pilnam taengah lai a suk pah tih puen a cak te Israel hlang loh a hmuh vaengah pilnam tah lungko khuila, hlingpuep khuila, thaelpang khuila, hmuensang neh tangrhom khuila thuh uh.
Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime.
7 Hebrew rhoek khaw Gad kho kah Jordan neh Gilead la kat uh. Tedae Saul amah tah Gilgal ah om pueng tih a hnukkah pilnam boeih long tah lakueng uh.
Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi. Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha.
8 Te dongah a khoning bangla Samuel te hnin rhih khuiah a rhing mai a rhing mai. Tedae Samuel te Gilgal la a pawk pawt dongah pilnam khaw Saul taeng lamloh taekyak uh.
Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja.
9 Te dongah Saul loh, “Hmueihhlutnah neh rhoepnah te kai taengla hang khuen,” a ti nah tih hmueihhlutnah te a nawn.
Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza.
10 Tedae hmueihhlutnah a nawn te a khah van neh Samuel te tarha ha pawk tih anih doe ham neh uem hamla Saul te cet.
Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.
11 Samuel loh, “Balae na saii?” a ti nah hatah, Saul loh, “Pilnam he kai taeng lamloh haeh coeng tih tingtunnah tue vaengah namah khaw na pawk voel pawh tila ka hmuh. Te vaengah Philisti loh Mikmash ah taai uh coeng.
Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?” Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi,
12 Tedae, “Philisti loh kai taengla Gilgal ah ha suntla uh pawn ni, BOEIPA maelhmai ka tong pawt ah,” ka ti dongah ka thiim uh tih hmueihhlutnah te ka nawn,” a ti nah.
ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”
13 Tedae Samuel loh Saul te, “Na pavai dongah ni BOEIPA na Pathen loh nang ng'uen olpaek na tuem pawh. Na ram he BOEIPA loh Israel taengah kumhal duela a thoh pawn suidae ta.
Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale.
14 Tedae na ram he pai voel mahpawh. BOEIPA loh nang ng'uen te na tuem pawt dongah amah kah thinko aka tong hlang ni BOEIPA loh a toem, anih te BOEIPA loh a pilnam soah rhaengsang la a uen coeng,” a ti nah.
Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
15 Te phoeiah Samuel te thoo tih Gilgal lamloh Benjamin Gibeah la cet. Pilnam te Saul loh a soep vaengah hlang ya rhuk tluk amah taengah a om pah.
Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.
16 Saul, a capa Jonathan neh a taengkah aka om pilnam loh Benjamin Geba ah a om vaengah Philisti tah Mikmash ah rhaeh.
Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi.
17 Te vaengah Philisti caem lamkah kutpo rhoek te, rhoi thum la coe uh tih rhoi at tah Shual kho kah Ophrah longpuei la hooi uh.
Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala.
18 Rhoi at te Bethhoron longpuei la hooi uh tih rhoi at te kolrhawk la aka dan khosoek rhi kah longpuei la hooi uh.
Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.
19 Te vaengah Israel kho tom ah kutthai ana om pawt hatah Philisti loh, “Hebrew te cunghang khaw, caai khaw saii uh phayoe ve,” a ti uh.
Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!”
20 Tedae a thecung neh a tuktong mai khaw, a hai neh a thecung mai khaw hlang loh a tah ham vaengah tah Philisti te Israel pum loh a suntlak thiluh.
Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo.
21 Tedae thecung neh tuktong khaw, thingsong pathum neh hai khaw, ciksum a ten ham koi khaw yula man la a om pah.
Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.
22 Te dongah caemtloek tue a pha vaengah Saul neh Jonathan taengkah pilnam he pakhat kut dongah khaw cunghang neh caai hmu voel pawh. Tedae Saul neh a capa Jonathan taengah ah dawk hmuh la om.
Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.
23 Te vaengah Philisti rhaltawt hmuen tah Mikmash lamkai la pawk coeng.
Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.

< 1 Samuel 13 >