< 1 Khawrin 9 >
1 A hoep la ka om moenih a? Caeltueih la ka om moenih a? Mamih Boeipa Jesuh ka hmuh moenih a? Nangmih te Boeipa ah ka kutngo la na om uh moenih a?
Kodi sindine mfulu? Kodi sindine mtumwi? Kodi sindinamuone Ambuye athu Yesu? Kodi inu sindiye zotsatira za ntchito yanga mwa Ambuye?
2 Hlang tloe taengah caeltueih la ka om pawt cakhaw nangmih ham ka om ngawn dae ta. Kai kah caeltueih coengnah kutnoek tah Boeipa ah nangmih na om uh ta.
Ngakhale kwa ena sindingakhale mtumwi, mosakayika ndine mtumwi kwa inu! Poti inu ndi chizindikiro cha utumwi wanga mwa Ambuye.
3 Kai aka boelh rhoek taengah kai kah olthungnah tah he coeng ni.
Kwa iwo wofuna kundizenga milandu ndimawayankha kuti:
4 Ka caak tih ka ok ham saithainah la ka khueh uh pawt moenih a?
Kodi ife tilibe ulamuliro wakudya ndi kumwa?
5 A tloe caeltueih rhoek, Boeipa kah manuca rhoek neh Kephas bangla ngannu, ka yuu khaw khuen ham saithainah ka khueh uh pawt moenih a?
Kodi ife tilibe ulamuliro wotenga mkazi wokhulupirira nʼkumayenda naye monga amachitira atumwi ena ndi abale awo a Ambuye ndiponso Kefa?
6 Kai neh Barnabas bueng long khaw saii pawt ham saithainah ka khueh rhoi moenih a?
Kodi kapena ine ndekha ndi Barnaba ndiye tikuyenera kugwira ntchito kuti tipeze zotisowa?
7 Amah buhcun neh aka vathoh noek te unim? Misur a tue dae a thaih aka ca pawt te unim? Tuping a dawn tih tuping kah suktui aka o pawt te unim?
Ndani angagwire ntchito ya usilikali namadzipezera yekha zofunika zonse? Kodi ndani amadzala mpesa koma wosadyako zipatso zake? Ndani amaweta nkhosa koma wosamwako mkaka wake?
8 Hekah he hlang lamloh ka thui moenih. Hekah he olkhueng long khaw a thui bal moenih.
Kodi moti zimene ndikunenazi ndimaganizo a umunthu chabe? Kodi Malamulo sakunena chimodzimodzinso?
9 Moses kah olkhueng dongah a daek coeng ta. Cang aka til vaito te a ka poi boeh. Vaito ham te Pathen a ngai a huet moenih a?
Popeza analemba mʼMalamulo a Mose kuti, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.” Kodi pamene Mulungu ananena zimenezi ankalabadira za ngʼombe zokha?
10 Mamih ham khaw a thui van ta. Mamih ham khaw a daek coeng. Aka thol loh ngaiuepnah neh a thol ham a kuek. Cangtil long khaw ngaiuepnah neh a cabol ham om ta.
Ndithu Iyeyo amanena za ifenso, kodi si choncho? Inde, izi anazilemba chifukwa cha ife, pakuti wolima ndiponso wopuntha, onsewo amagwira ntchito mwachiyembekezo chodzagawana zokololazo.
11 Kaimih loh nangmih taengah mueihla cangti ka tuh uh. Tedae kaimih loh nangmih kah te pumsa la ka at uh koinih rhoekoe aih ni ta.
Ngati tidzala mbewu yauzimu pakati panu, kodi ndi chovuta kwambiri kuti tikolole zosowa zathu kuchokera kwa inu?
12 A tloe rhoek loh nangmih kah saithainah he a cabol uh atah kaimih ngai pawt nim? Tedae hekah saithainah he ka rhoidoeng uh moenih. Tedae boeih ka ueh uh daengah ni tomtanah pakhat khaw om mueh la Khrih kah olthangthen te kam paek uh eh.
Ngati ena ali ndi ufulu wothandizidwa ndi inu, kodi ife sitikuyenera kukhala nawo ufulu ochulukirapo? Koma ife sitinagwiritse ntchito ufulu umenewu. Mʼmalo mwake timangodzichitira chilichonse posafuna kutsekereza ena kumva Uthenga Wabwino wa Khristu.
13 Aka cim la aka saii rhoek loh Bawkim kah te a caak uh te na ming uh pawt nim? hmueihtuk aka bulbo rhoek loh hmueihtuk taengkah te a bawn ta.
Kodi simukudziwa kuti wogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amapeza chakudya chawo mʼNyumbamo, ndipo kuti otumikira pa guwa lansembe amagawana zimene zaperekedwa pa guwa lansembelo.
14 Te vanbangla olthangthen aka doek rhoek te khaw olthangthen neh hing saeh tila Boeipa loh a uen coeng.
Chomwechonso Ambuye akulamula kuti wolalikira Uthenga Wabwino azilandira thandizo lawo polalikira Uthenga Wabwinowo.
15 Tedae kai loh hekah he khat khaw ka rhoidoeng moenih. Tekah bangla kai taengah om sak ham khaw hekah he ka daek moenih. Kai kah thangpomnah te a tlongtlai sak pawt atah ka duek te kai ham lat then ngai.
Koma ine sindinagwiritse ntchito ufulu woterewu. Sindikulemba izi ndi chiyembekezo choti mundichitire zoterezi. Kuli bwino ndife kusiyana nʼkuti wina alande zomwe ndimazinyadira.
16 Olthangthen ka phong atah kai ham thangpomnah om mahpawt nim? A kueknah khaw kai ham tah lalh bal. Phong kolla om cakhaw anunae kai ham aih he.
Komatu ndikamalalikira Uthenga Wabwino, sindingadzitamandire popeza ndimawumirizidwa kulalikira. Tsoka kwa ine ngati sindilalikira Uthenga Wabwino!
17 He he thahlue la ka saii atah thapang ka dang. Tedae ka ngaihak akhaw hnokhoemnah he kai n'kungsut coeng.
Ngati ndikugwira ntchitoyi mwakufuna kwanga, ndili ndi mphotho; koma ngati si mwakufuna kwanga, ndiye kuti ntchitoyi ndi Ambuye anandipatsa.
18 Te koinih kai ham mebang thapang nim aka om. Olthangthen ka phong he a yoeyap la ka khueh mai eh. Olthangthen dongah ka saithainah te ka lawn sak moenih.
Tsono mphotho yanga ndi chiyani? Ndi iyi: kuti polalikira Uthenga Wabwino ndiwupereke kwaulere komanso kuti ndisagwiritse ntchito ufulu wanga polalikira uthengawo.
19 Hlang boeih taeng lamkah aka loeih la ka om dae hlang boeih taengah kamah ka pinyen uh. Te daengah ni muep ka dang eh.
Ngakhale ndine mfulu ndipo sindine kapolo wa munthu, ndimadzisandutsa kapolo wa aliyense kuti ndikope ambiri mmene ndingathere.
20 Judah rhoek taengah Judah la ka om daengah ni Judah rhoek te ka dang eh. Kamah tah olkhueng hmuiah ka om pawt dae olkhueng hmuikah rhoek taengah olkhueng hmuikah bangla ka om daengah ni olkhueng hmuikah rhoek te ka dang eh.
Kwa Ayuda ndimakhala ngati Myuda kuti ndikope Ayuda. Kwa olamulidwa ndi Malamulo ndimakhala ngati wolamulidwa nawo (ngakhale kuti sindine wolamulidwa ndi Malamulowo) kuti ndikope amene amalamulidwa ndi Malamulo.
21 Lailak rhoek taengah lailak bangla ka om dae Pathen taengah lailak la ka om pawt tih Khrih kah a rhimong dongah ni ka om. Te daengah ni lailak rhoek te ka dang eh.
Kwa amene alibe Malamulo ndimakhala wopanda Malamulo (ngakhale kuti sindine wopanda Malamulo a Mulungu koma ndili pansi pa ulamuliro wa Khristu) kuti ndikope wopanda Malamulo.
22 Tattloel taengah tattloel la ka om daengah ni tattloel rhoek te ka dang eh. Hlang boeih taengah cungkuem la ka om daengah ni pakhat khaw ka khang tangloeng eh.
Kwa ofowoka ndimakhala wofowoka, kuti ndikope ofowoka. Ndimachita zinthu zilizonse kwa anthu onse kuti mwanjira ina iliyonse ndipulumutse ena.
23 Olthangthen ham a soep ka saii daengah ni te te aka bawn la ka om eh.
Ndimachita zonsezi chifukwa cha Uthenga Wabwino, kuti ndigawane nawo madalitso ake.
24 Phalong khat ah aka yong rhoek loh boeih yong uh ngawn dae pakhat long ni kutdoe a dang tila na ming uh moenih a? Na yong uh van daengah ni na dang uh eh.
Kodi simukudziwa kuti pa mpikisano wa liwiro onse amathamanga ndithu, koma mmodzi yekha ndiye amalandira mphotho? Motero thamangani kuti mupate mphotho.
25 Te dongah aka loehlang boeih loh boeih kuemsuem saeh. Te pataeng khaw amih loh aka hmawn koi rhuisam ni a. dang uh eh. Tedae mamih tah aka kuei ham ni n'thingthueluh.
Aliyense wochita mpikisano amakonzekera mwamphamvu. Amachita izi kuti alandire mphotho yankhata yamaluwa yomwe imafota. Koma ife timachita izi kuti tilandire mphotho yosafota.
26 Te dongah khungrhap la kai ka yong van moenih. Yilh aka bop bangla ka thoek van moenih.
Choncho sindithamanga monga wothamanga wopanda cholinga; komanso sindichita mpikisano wankhonya monga munthu amene amangomenya mophonya.
27 Tedae ka pum he ka ngae tih ka phaep. Hlang tloe taengah amah kah a lolhmaih aka hoe la ka om boel eh.
Ine ndimazunza thupi langa ndi kulisandutsa kapolo kuti nditatha kulalikira ena, ineyo ndingadzapezeke wosayenera kulandira nawo mphotho.