< Aroma 11 >
1 Ine ndikufunsa kuti kodi Mulungu anakana anthu ake? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Inenso ndine Mwisraeli, mmodzi mwa zidzukulu za Abrahamu, ndiponso wa fuko la Benjamini.
Mbe enaika, Angu Nyamuanga abhalemele abhanu bhae? Na katyali uli. Kwo kubha anye one nili Mwisilaeli, wo lwibhulo Lwa Ibhulaimu, wo luganda lwa Benyamini.
2 Mulungu sanawakane anthu ake amene Iye anawadziwiratu. Kodi inu simukudziwa zimene Malemba akunena pa ndime imene Eliya akudandaula kwa Mulungu kuneneza Aisraeli? Iye anati,
Nyamuanga hatabhalemele abhanu bhae, abho amenyele okwambila kubhwambilo. Angu mutakumenya elyandiko elyaika chinuki okulubhana na Eliya, lwa kutyo amukomelesishe Nyamuanga ingulu ya Israel?
3 “Ambuye, anthuwa apha aneneri anu ndi kugwetsa maguwa anu ansembe. Ndatsala ine ndekha wamoyo ndipo akufuna kundipha?”
“Latabhugenyi, bhabheta abhalagi bhao, nawe bhona bhafumya ebhigabhwilo bhyao. Anye omwene -ela nanye nasanga, nabho abhayeja obhuwanga bhwani.”
4 Ndipo yankho la Mulungu linali lotani? “Ine ndadzisungira ndekha anthu 7,000 amene sanapembedzepo Baala.”
Mbe nawe lisubhyo lya Nyamuanga elyaikaki kwawe? “Nibhikile ingulu yani abhanu bhiubhi musanju bhanu bhatakumubhumila bhiju Bhaali.”
5 Chimodzimodzinso lero lino, alipo Aisraeli pangʼono osankhidwa mwachisomo.
Nolwo kutyo, omwanya gunu ogwa woli one bhalio bhanu bhasagile kunsonga yo kusola mu chigongo.
6 Ndipo ngati ndi mwachisomo, sikungakhalenso mwa ntchito. Ngati zikanatero, chisomo sichikanakhalanso chisomo ayi.
Mbe nawe jikabha mu chigongo, atali lindi mu bhikolwa. kubhindi echigongo chitakubha lindi chigongo.
7 Nʼchiyani tsopano? Chimene Aisraeli anachifuna ndi mtima wonse sanachipeze koma osankhidwawo anachipeza. Enawo anawumitsidwa mtima
Mbe nichinuki woli? Echinu chinu Israeli aliga naiiga, atachibhwene, nawe abhasolwa bhachibhwene, na abhandi bhayanilwe bhusito.
8 monga kwalembedwa kuti, “Mulungu anawapatsa mzimu wosatha kumvetsa zinthu, maso osatha kupenya; makutu osatha kumva mpaka lero lino.”
Ni lwa kutyo jandikilwe: “Nyamuanga abhayae mwoyo gwo bhugunie, ameso koleleki bhasige okulola, na Matwi koleleki bhasige okungwa, kukinga lelo linu.”
9 Ndipo Davide akuti, “Maphwando awo asanduke msampha ndi diwa lowakola ndi chopunthwitsa kuti alandire chilango.
No mwene Daudi kaika, “Musige jimeja jebhwe na jibhe waya, mitego, kwibhala lwo kwikujula, no kusubhya olusima ingulu yebhwe.
10 Maso awo atsekedwe kuti asaone, ndi misana yawo ikhale yokhota nthawi zonse.”
Siga ameso gebhwe gatelweko echisunte koleleki bhasigo olola. Nubhenamye emigongo jebhwe Kata.”
11 Ine ndikufunsanso kuti, kodi iwo anapunthwa ndi kugwa kotheratu? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Koma chifukwa cha kulakwa kwawo, chipulumutso chinafika kwa a mitundu ina kuti Aisraeli achite nsanje.
Mbe woli enaika, “Angu, bhekujuye kukingila okugwa?” Jasiga kubha kutyo kajanende. Amwi nejo, kwo kuigwa kwebhwe, omwelulo gwabhakingiye abhanyamaanga, koleleki abhene bhejule lifuwa.
12 Koma ngati kulakwa kwawo kwapindulitsa dziko lapansi ndi kulephera kwawo kwapindulitsa a mitundu ina, nanga kudzakhala kupindula kwakukulu chotani iwo akadzabwera chonse!
Mbe woli kukabha kuli kuigwa kwebhwe ni bhunibhi bhwe Chalo, na alabha okufwilwamo kwebhwe kwa kutyo-ela ni bhunibhi bhwa Maanga, ni bhwafuki kukila kukumila kwebhwe?
13 Ine ndikuyankhula kwa inu a mitundu ina monga ine ndili mtumwi wa kwa a mitundu ina ndipo ndimawunyadira utumiki wangawu.
Mbe woli enaika nemwe abhanu bha Maanga. Kulwo kubha nabhee Intumwa ku bhanu bha Maanga agandi, enikuisha mukufulubhenda kwani.
14 Ine cholinga changa nʼchakuti ndichititse nsanje anthu a mtundu wanga kuti ena mwa iwo apulumutsidwe.
Amwi enichula nimbajisha lifuwa bhanu bhali mubhili gumwi nanye. Amwi echibhakisha abhandi bhebhwe.
15 Pakuti ngati kukanidwa kwawo kunayanjanitsa anthu a dziko lapansi ndi Mulungu, nanga kudzatani, Iye akadzawalandiranso? Kudzakhala monga ngati anthu akufa akuuka.
Kulwo kubha alabha okulemwa kwebhwe ni mekilishanyo ge Chalo, okulamilwa kwebhwe okubha atiki nakabhee obhuanga okusoka mu bhafuye?
16 Ngati chigawo chimodzi cha buledi woperekedwa monga zipatso zoyamba ndi choyera, ndiye kuti zonsezo ndi zoyera. Ngati muzu ndi oyera, nʼchimodzimodzinso nthambi zake.
Alabha amatwasho go Kwamba ni bhikilo, nikwo kutyo bhili kwo bhafu bhwa jisyanu. Alabha emisi ni libhikilo, amatabhi one nikwo kutiyo.
17 Ngati nthambi zina zinakhadzulidwa ndipo inu, inu ndiye nthambi za olivi wakuthengo, nʼkulumikizidwa pamalo pa nthambi zimenezo, ndipo tsopano mukulandira nawo zakudya zochokera ku mizu ya olivi,
Mbe nawe alabha agandi amatabhi gakatemwa, kuti awe, nawe litabhi lye mwila elyo musheka, linu lwayambilwe agati yebhwe, na nilisangila amwi nabho mu misi jo bhunibhi bhwo musheka,
18 musadzitame kunyoza nthambi zinazo. Ngati mutero, ganizirani ichi kuti Inu simugwiriziza mizu, koma muzu ukugwiriziza inu.
wasiga kwikuya ingulu ya matabhi. Nawe alabha owikuya, atali awe unu ousakila emisi, nawe emisi ejikusakila awe.
19 Tsono mudzati, “Nthambizo zinakhadzulidwa kuti ine ndilumikizidwepo.”
Mbe nawe owaika, “amatabhi gatemelwe koleleki niyambwe kwi Sina.
20 Nʼzoona. Koma iwo anakhadzulidwa chifukwa chosakhulupirira ndipo inu mukuyima mwachikhulupiriro. Musadzitukumule, koma muchite mantha.
Ejo ni ja chimali. Kunsonga yo kulema okwikilisha kwebhwe bhatemelwe, mbe nawe awe wemeleguyu ulumile koto kunsonga ye likilisha lyao. Wasiga okwiganilisha muno omwene -ela, nawe ubhaye.
21 Pakuti ngati Mulungu sanalekerere nthambi zachibadwidwe, Iye sadzakulekererani inunso.
Kulwo kubha akabha Nyamuanga atagasigile amatabhi go bhusimuka, atakusasila awe one.
22 Nʼchifukwa chake ganizirani za kukoma mtima ndi za ukali wa Mulungu. Ukali uli kwa iwo amene anagwa koma kukoma mtima kwa inu, malinga ngati musamala kukoma mtima kwakeko kupanda kutero inunso mudzakhadzulidwanso.
Mbe, nulole, ebhikolwa bhye kisi no bhululu bhwa Nyamuanga. kwi bhala limwi, obhululu bhunu bhwejile ingulu ya Bhayaudi bhanu bhaguye. Nawe kulubhala lundi, obhwekisi bhwa Nyamuanga bhwejile ingulu yao, nawe ukekomesha mu bhwekisi bhwae. Ukatasikana neJo awe one ulilemelelwa Kula.
23 Ngati iwo asiya kukhala osakhulupirira, adzalumikizidwanso pakuti Mulungu akhoza kuwalumikizanso.
Alabha bhene one bhakalema okugendelela mu bhunyantekilisha bhwebhwe, abhayambwa lindi. Kulwo kubha Nyamuanga ali no bhutulo bhwo kubhayamba lindi.
24 Pakuti ngati inu, mwa chilengedwe munali mtengo wa olivi wa kuthengo, Mulungu anakukhadzulani nakulumikizani ku mtengo wa olivi wodzalidwa, zomwe ndi zotsutsana ndi chilengedwe, kodi sikudzakhala kwapafupi kwa Iye kuwalumikizanso mu mtengo wawowawo wa olivi?
Kulwo kubha alabha emwe mwatemelwe anja ya bhinu bhuli bhusimuka bhwo musheka gwe mwila no bhutasikene bhwo bhusimuka mwayambilwe ku musheka gunu guli gwe kisi, atali kwiya kafu muno abhayaudi bhanu, bhali lwa matabhi go bhusimuka bhanu abhatula okuyambwa lindi mu masheka gebhwe abhene?
25 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa za chinsinsi ichi, kuti mungadziyese nokha anzeru. Kuwuma mtima kumene Aisraeli akuchita ndi kwa kanthawi kufikira chiwerengero cha a mitundu chitalowa.
Kulwo kubha bhaili nitakwenda musige okumenya, okulubhana na imbisike inu ati mwasiga okubha no bhumenyi mu okwiganilisha kwemwe abhene. Imbisike inu ni ati obhukomee bhusokele mu Israeli, kukinga mu kukumila kwa Maanga galijila.
26 Kotero tsono Aisraeli onse adzapulumuka, monga kwalembedwa kuti, “Mpulumutsi adzachokera ku Ziyoni; Iye adzachotsa zoyipa zonse za Yakobo.
Kwibhyo Israeli bhone abhwelulwa, kutyo jandikilwe.”Okusoka Sayuni Kaja omwelusi Kabhumenya obhujabhi okusoka ku yakobo.
27 Ndipo ili lidzakhala pangano langa ndi iwo pamene Ine ndidzachotsa machimo awo.”
Na linu elibha elagano lyani amwi nabho, omwanya ogwo nakabhisosheo ebhibhibhi bhyebhwe.”
28 Chifukwa cha Uthenga Wabwino, Aisraeli asanduka adani a Mulungu kuti inu mupindule. Koma kunena za kusankhidwa, iwo ndi okondedwa ndi Mulungu chifukwa cha makolo awo aja.
Ku lubhala oumwi okulubhana no misango no bhwana, abhabhabhiililwa ku Songa yemwe. Kwo lubhala lundi okulubhana no bhwausi bhwa Nyamuanga, abhene ku Songa ya bhajanji.
29 Pakuti Mulungu akayitana munthu ndi kumupatsa mphatso sangasinthenso.
Kwo kubha ebhiyanwa no kubhilikilwa kwa Nyamuanga bhutakuyinduka.
30 Monga mmene inu munalili, osamvera Mulungu pa nthawi ina, tsopano mwalandira chifundo chifukwa cha kusamvera kwawo.
Kwo kubha kubhwambilo emwe mwaliga muli bhanyamusi bha Nyamuanga, nawe oli mwachilamila echigongo ku Songa yokunyamula kwebhwe.
31 Chonchonso iwo akhala osamvera tsopano kuti iwonso alandire chifundo chifukwa cha chifundo cha Mulungu kwa inu.
Kwa injila eye yo, Oli Abhayaundi bhanu bhanyamuye. Nawe okumala kwendao ni bha ati okulubhana no kubhasasila bhanu muli na mabhando emwe abhatula one okulamila echigongo.
32 Pakuti Mulungu anasandutsa anthu onse a mʼndende ya kusamvera kuti Iye akaonetse chifundo kwa onse. (eleēsē )
Kulwo kubha Nyamuanga abhabhoyele abhanu bhone mu bhunyamusi koleleki atule okubhasasila bhone. (eleēsē )
33 Aa! Nzeru za Mulungu ndi chidziwitso chake ndi zozama kwambiri! Ndani angazindikire maweruzidwe ake, ndipo njira zake angazitulukire ndani?
Lwa kutyo bhili bhikulu kubhunibhi no bhumenyi no bhwengeso bhwa Nyamuanga! jitakumenyelwa jindamu jae, na jinjila jae jitakumenyekana!
34 “Kodi wadziwa ndani maganizo a Ambuye? Kapena ndani anakhalapo mlangizi wake?”
“Kwibhyo niga unu kaimenya injila ya Latabhugenyi? Amwi niga unu aliga ali mulwaji wae?
35 “Kodi ndani anapereka mphatso kwa Mulungu, kuti Mulunguyo amubwezere iye?”
Amwi niga unu atangatile okumuyana echinu Nyamuanga, koleleki aliywe lindi?
36 Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni. (aiōn )
“Ku lwebhyo okusoka kumwene, na kunjila yae na kumwene, ebhinu bhyona bhilo abhilabhile kumwene libhwe kusho kajanende. Amina. (aiōn )