< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
Слово Господнє, що було́ до Софо́нії, сина Куші, сина Ґеда́лії, сина Амарії, сина Єзекі́ї, за днів Йосії, Амонового сина, Юдиного царя.
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
„Забираючи, все заберу́ з-над пове́рхні землі, промовляє Госпо́дь.
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
Заберу́ Я люди́ну й худобу, заберу́ птаство небесне і риби морські́, і спокуси з безбожними, і витну люди́ну з пове́рхні землі, промовляє Госпо́дь.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
І руку Свою простягну́ Я на Юду і на всіх ме́шканців Єрусалиму, — і ви́гублю з місця оцьо́го оста́нок Ваа́ла, іме́ння жерці́в зо священиками,
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
і тих, хто вклоня́ється на даха́х світи́лам небесним, і тих, хто вклоняється, хто присягає Го́сподом, і хто присягає царем своїм,
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
і тих, хто відступає від Господа, і хто не шукає Господа, і не звертається до Нього.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Замовчи́ перед Го́сподом Богом, бо близьки́й день Господній, бо жертву Господь пригото́вив, посвятив Своїх покли́каних.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
І станеться в день Господньої жертви, і навіщу́ Я князі́в, і синів царя, і всіх, хто зодяга́є одежу чужи́нну.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
І навіщу́ Я кожного, хто перескакує через поріг того дня, тих, хто наповнює дім свого пана насиллям й оманою.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
І буде в дні то́му, — говорить Госпо́дь, — голос крику із Рибної брами, і завива́ння із Міста Ново́го, і велика руїна із па́гірків.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
Ридайте, мешка́нці Махте́шу, бо пони́щений буде ввесь купе́цький наро́д, будуть ви́гублені всі, хто важить срібло́.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
І станеться ча́су того, і перешукаю Я з ля́мпами Єрусалим, і навіщу́ Я тих му́жів, які задубі́ли на дрі́жджах своїх, що говорять у серці своє́му: „Господь не вчинить добра, і ли́ха не зробить.“
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
І здо́биччю стане все їхнє багатство, а їхні доми́ — за спусто́шення, — І бу́дуть вони будувати доми́, але в них не сиді́тимуть, і виноградники будуть сади́ти, та вина їхнього не питимуть.
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
Близьки́й день Господній великий, він близьки́й й дуже швидко настане. Ось голос Господнього дня, — тоді гірко кричатиме навіть хоробрий!
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
День гніву цей день, день смутку й наси́лля, день збу́рення та зруйнува́ння, день темно́ти та те́мряви, день хмари й імли́,
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
день су́рмлення й окрику проти укрі́плених міст та проти високих міськи́х заборо́лів.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
І бу́ду чинити Я у́тиск люди́ні, і бу́дуть ходити вони, як сліпі́, бо згріши́ли вони проти Го́спода. І ви́ллється кров їхня, немов той пісок, а їхнє тіло, — як гній.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Спасти́ їх не зможе в день гніву Господнього ні їхнє срібло́, ані золото їхнє, — і огнем Його за́здрощів буде поїджена ціла земля́, бо скі́нчення тільки приспі́шене зробить зо всіми мешка́нцями кра́ю цього́.

< Zefaniya 1 >