< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
Detta är Herrans ord, som skedde till Zephania, Chusi son, Gedalja sons, Amarja sons, Hiskia sons, uti Josia tid, Amons sons, Juda Konungs.
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
Jag skall taga bort all ting utu landena, säger Herren.
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
Jag skall borttaga både folk och fä, både himmelens foglar, och fiskarna i hafvet, samt med afgudarna och de ogudaktiga; ja, jag skall utrota menniskorna af landena, säger Herren.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
Jag skall uträcka mina hand öfver Juda, och öfver alla de som i Jerusalem bo; alltså skall jag borttaga det qvart är af Baal, dertill de namn, Munkar och Prester, utu desso rumme;
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
Och de som på taken tillbedja himmelens här; de som honom tillbedja, och svärja dock vid Herran, och vid Malcham derjemte;
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
Och de som affalla ifrå Herranom, och intet fråga efter Herran, och intet akta honom.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Varer tyste för Herranom Herranom; ty Herrans dag är för handene; ty Herren hafver tillredt ett slagtoffer, och budit der sina gäster till.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
Och på Herrans slagtoffers dag skall jag hemsöka Förstarna och Konungsbarnen, och alla de som bära en främmande kyrkoskrud.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
Och skall jag den tiden hemsöka dem som öfver tröskelen springa; de deras herrars hus uppfylla med rot och bedrägeri.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
På den tiden, säger Herren, skall upphäfva sig ett högt rop ifrå fiskaportenom, och en gråt ifrå dem andra portenom, och en stor jämmer på högomen.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
Jämrer eder, I som bon i qvarnene; ty hela krämarefolket är borto, och alle de som penningar församla, äro förgångne.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
På den tiden skall jag utransaka Jerusalem med lyktor, och skall hemsöka dem som ligga på sine drägg, och säga i sitt hjerta: Herren varder hvarken godt eller ondt görandes.
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
Och deras ägodelar skola till rofs varda, och deras hus till ett öde; de skola bygga hus, och intet bo deruti; de skola plantera vingårdar, och intet vin dricka deraf.
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
Ty Herrans store dag är hardt för handene; han är hardt när, och hastar sig svårliga. När det ropet om Herrans dag kommandes varder, så skolade starke ropa bitterliga.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
Ty denne dagen är en grymhets dag, en bedröfvelses och ångests dag en väders och storms dag, en mörkers, och dimbos dag, en molns och töcknes dag;
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
En basuns och trummetes dag, emot de fasta städer och höga borger.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
Jag skall göra menniskomen bekymmer, så att de skola gå omkring såsom de blinde; derföre, att de emot Herran syndat hafva; deras blod skall utgjutet varda, lika som det stoft vore, och deras kroppar såsom träck.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Deras silfver och guld skall intet kunna hjelpa dem på Herrans vredes dag; utan hela landet skall genom hans nits eld förtärdt varda; ty han skall snarliga en ända göra med alla de som bo i landena.

< Zefaniya 1 >