< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
La palabra del Señor que vino a Sofonías, hijo de Cusi, hijo de Gedalías, hijo de Amarías, hijo de Ezequías, en los días de Josías, hijo de Amón, rey de Judá.
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
Destruiré todo de la faz de la tierra, dice el Señor.
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
Destruiré al hombre y la bestia; destruiré las aves del cielo y los peces del mar; causando la caída de los malhechores, y destruiré al hombre de la faz de la tierra, dice el Señor.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
Y mi mano se extenderá sobre Judá y sobre todo el pueblo de Jerusalén, destruiré el nombre del Baal de este lugar, y el nombre de los falsos sacerdotes,
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
Y los que se suben a las azoteas para adorar a los astros, a los que se postran y juran, y los adoradores del Señor que juraron por Milcom,
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
Y aquellos que se han apartado de mi, y aquellos que no han hecho oración al Señor ni han recibido instrucciones de él.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Que no haya sonido delante del Señor Dios: porque el día del Señor está cerca; porque el Señor ha preparado una ofrenda, ha santificado a sus invitados.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
Y sucederá el día de la ofrenda del Señor, que enviaré castigo a los gobernantes y a los hijos del rey y a todos los que estén vestidos con túnicas de tierras extranjeras.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
Y en ese día enviaré castigo a todos los que salten por los umbrales y llenen la casa de su amo con conducta violenta y engaño.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
Y en ese día, dice el Señor, se oirá un grito desde La puerta del Pez, y un clamor desde la segunda, y un grito de quebrantamiento de los collados.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
Giman habitantes del mortero. Debido a la caída de todo el pueblo de Canaán; todos los que traían plata fueron destruidos.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
Y sucederá en ese tiempo, que iré a buscar a través de Jerusalén con lámparas; y enviaré castigo a los hombres que reposan como vino en su sedimento, que se dicen a sí mismos: El Señor no hará el bien ni hará el mal.
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
Y sus riquezas serán quitadas violentamente, y sus casas serán destruidas. Seguirán construyendo casas y nunca vivirán en ellas, y plantarán viñas pero no beberán vino de ellas.
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
El gran día del Señor está cerca, está cerca y viene muy rápido; Se acerca el amargo día del Señor, amargamente gritará el guerrero.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
Ese día es un día de ira, un día de angustia y tristeza, un día de ruina y destrucción, un día de noche oscura y sombra profunda, un día de nubes y oscuridad espesa.
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
Un día de trompeta y el grito de guerra contra las ciudades amuralladas y las altas torres.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
Y enviaré angustias a los hombres para que anden como ciegos, porque han hecho lo malo contra el Señor; y su sangre será escurrida como polvo, y su carne como estiércol.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Incluso su plata y su oro no podrán mantenerlos a salvo en el día de la ira del Señor; pero toda la tierra se quemará en el fuego de su ira amarga; porque él pondrá fin, incluso de repente, a todos los que viven en la tierra.

< Zefaniya 1 >