< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
O KA olelo a Iehova, ka mea i hiki mai io Zepania la i ke keiki a Kusi, ke keiki a Gedalia, ke keiki a Amaria, ke keiki a Hizekia, i na la o Iosia ke keiki a Amona, ke alii o ka Iuda.
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
E lawe loa aku auanei au i na mea a pau mai luna aku o ka aina, wahi a Iehova.
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
E lawe auanei au i na kanaka a me na holoholona; E lawe auanei au i na manu o ka lewa, a me na ia o ke kai, A me na mea e hina ai, me ka poe hewa; A e hooki iho hoi au i na kanaka mai luna aku o ka aina, wahi a Iehova.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
E kau aku hoi au i kuu lima maluna o ka Iuda, A me na kanaka a pau o Ierusalema: A e hooki iho au i ke koena o ko Baala, mai keia wahi aku, A me ka inoa o na mea hoomanakii a me na kahuna hoi;
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
A me ka poe hoomana i ka puali o ka lani maluna o na hale; A me ka poe hoomana, a hoohiki hoi ma Iehova, A me ka hoohiki ma Malekama;
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
A me ka poe i hoi ihope mai o Iehova aku; A me ka poe aole i imi ia Iehova, aole hoi i ninau aku nona.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
E hamau oe ma ke alo o Iehova ka Haku: No ka mea, ua kokoke mai nei ka la o Iehova: No ka mea, ua hoomakaukau mai la o Iehova i ka mohai, A ua hoolaa iho la oia i kona poe hoaai.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
A i ka la o ko Iehova mohai ana, E hoopai auanei au i na alii a me na keiki a ke alii, A me ka poe a pau i aahuia i na kapa e.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
Ia la no, e hoopai au i ka poe a pau e lele ana maluna o ka paepae puka, A e hoopiha i ka hale o ko lakou haku i na mea i hao wale ia a me ka hoopunipuni.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
A ia la no, wahi a Iehova, He leo no ka uwe ana mai ka puka-ia mai, A he aoa ana mai ka apana alua mai, A me ka luku nui ana mai na puu mai.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
E kanikau oukou, e na kanaka o Maketesa; No ka mea, ua hookiia ae na kanaka kuai a pau; O ka poe a pau i kaumaha i ke kala, ua okiia.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
Ia manawa no, e huli iho no wau ia Ierusalema me na kukui, A e hoopai i ka poe e noho paakiki ana maluna o ko lakou maku; E olelo ana iloko o ko lakou naau, Aole e hana mai ana o Iehova i ka maikai, aole hoi e hana ia i ka ino.
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
Nolaila, e lilo auanei ko lakou waiwai i pio, A me na hale o lakou i neoneo: E kapili lakou i na hale, aole hoi e noho iloko; E kanu lakou i na malawaina, aole hoi e inu i ka waina olaila.
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
Ua kokoke mai ka la nui o Iehova, ua kokoke mai, A e wikiwiki loa mai ana ka leo no ka la o Iehova: Ilaila e uwe nui ai ke kanaka ikaika.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
He la no ka inaina ua la la, He la popilikia a me ka poino, He la e hao wale ia'i a me ka hooneoneo, He la pouli wale a me ka poeleele, He la e uhi mai ai na ao a me ka pouli paapu,
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
He la o ka pu kani a me ka hookani ana, E ku e i na kulanakauhale i puni i ka pa, a me na halekiai kiekie.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
A e hoopilikia no wau i na kanaka, I hele ai lakou e like me na makapo, No ka mea, ua hana hewa aku lakou ia Iehova; A e nininiia aku ko lakou koko e like me ka lepo, A o ko lakou io e like me ka opala.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Aole hoi e hiki i ka lakou kala, Aole hoi i ka lakou gula ke hoopakele ia lakou i ka la o ko Iehova inaina; Aka, e pau auanei ka aina a pau i ke ahi o kona lili ana; No ka mea e hoopau koke ana oia i ka poe a pau e noho ana ma ka aina.

< Zefaniya 1 >