< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
The word of the Lord that came to Sophonias the son of Chusi, the son of Godolias, the son of Amarias, the son of Ezechias, in the days of Josias the son of Amon king of Juda.
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
Gathering, I will gather together all things from off the face of the land, saith the Lord:
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
I will gather man, and beast, I will gather the birds of the air, and the fishes of the sea: and the ungodly shall meet with ruin: and I will destroy men from off the face of the land, saith the Lord.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
And I will stretch out my hand upon Juda, and upon all the inhabitants of Jerusalem: and I will destroy out of this place the remnant of Baal, and the names of the wardens of the temples with the priests:
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
And them that worship the host of heaven upon the tops of houses, and them that adore, and swear by the Lord, and swear by Melchom.
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
And them that turn away from following after the Lord, and that have not sought the Lord, nor searched after him.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Be silent before the face of the Lord God: for the day of the Lord is near, for the Lord hath prepared a victim, he hath sanctified his guests.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
And it shall come to pass in the day of the victim of the Lord, that I will visit upon the princes, and upon the king’s sons, and upon all such as are clothed with strange apparel.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
And I will visit in that day upon every one that entereth arrogantly over the threshold: them that fill the house of the Lord their God with iniquity and deceit.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
And there shall be in that day, saith the Lord, the noise of a cry from the fish gate, and a howling from the Second, and a great destruction from the hills.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
Howl, ye inhabitants of the Morter. All the people of Chanaan is hush, all are cut off that were wrapped up in silver.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
And it shall come to pass at that time, that I will search Jerusalem with lamps, and will visit upon the men that are settled on their lees: that say in their hearts: The Lord will not do good, nor will he do evil.
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
And their strength shall become a booty, and their houses as a desert: and they shall build houses, and shall not dwell in them: and they shall plant vineyards, and shall not drink the wine of them.
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
The great day of the Lord is near, it is near and exceeding swift: the voice of the day of the Lord is bitter, the mighty man shall there meet with tribulation.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
That day is a day of wrath, a day of tribulation and distress, a day of calamity and misery, a day of darkness and obscurity, a day of clouds and whirlwinds,
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
A day of the trumpet and alarm against the fenced cities, and against the high bulwarks.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
And I will distress men, and they shall walk like blind men, because they have sinned against the Lord: and their blood shall be poured out as earth, and their bodies as dung.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Neither shall their silver and their gold be able to deliver them in the day of the wrath of the Lord: all the land shall be devoured by the fire of his jealousy, for he shall make even a speedy destruction of all them that dwell in the land.

< Zefaniya 1 >