< Zefaniya 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
Biada brudnemu i splugawionemu miastu ucisku!
2 Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
Nie słuchało głosu ani nie przyjmuje upomnienia, nie zaufało PANU, nie zbliżyło się do swego Boga.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Jego książęta pośrodku niego są lwami ryczącymi, jego sędziowie są wilkami nocnymi, [które] nie gryzą kości aż do rana.
4 Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
Jego prorocy są lekkomyślni, to ludzie przewrotni; jego kapłani zbezcześcili świątynię, pogwałcili prawo.
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
PAN sprawiedliwy jest pośród niego, nie czyni nieprawości; każdego poranka wystawia swój sąd na światłość i nie zawodzi; lecz złośnik nie zna wstydu.
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
Wykorzeniłem narody, ich baszty są spustoszone, spustoszyłem ich ulice, tak że nikt nie przechodzi. Ich miasta są zniszczone, tak że nie ma ani człowieka, ani [żadnego] mieszkańca.
7 Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
Powiedziałem: Teraz na pewno będziesz się mnie bać, przyjmiesz upomnienie, aby nie zostało zniszczone twoje mieszkanie, jakkolwiek cię ukarzę. Ale wstali rano i psuli wszystkie swoje czyny.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
Dlatego oczekujcie mnie, mówi PAN, do dnia, w którym powstanę do łupu. Postanowiłem bowiem zebrać narody i zgromadzić królestwa, aby wylać na nie swoje rozgniewanie, całą zapalczywość swojego gniewu. Zaprawdę, cała ziemia będzie pożarta ogniem mojej gorliwości.
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
Wówczas bowiem przywrócę narodom czyste wargi, aby wszyscy wzywali imienia PANA i służyli mu jednomyślnie.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
Zza rzek Etiopii przyniosą mi dary moi czciciele, córka moich rozproszonych.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
W tym dniu nie zawstydzisz się z powodu wszystkich twoich uczynków, którymi wystąpiłeś przeciwko mnie. Wtedy bowiem usunę spośród ciebie tych, którzy chełpią się twoją sławą, i już nie będziesz się wywyższać na mojej świętej górze.
12 Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
I pozostawię pośród ciebie lud ubogi i nędzny, i będzie ufać imieniu PANA.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
Resztka Izraela nie będzie czynić nieprawości ani nie będzie mówić kłamstwa; nie znajdzie się w jej ustach język zdradliwy. Ale będzie się paść i odpoczywać, a nikt nie będzie jej straszyć.
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Zaśpiewaj, córko Syjonu! Wykrzykuj, Izraelu! Ciesz się i raduj z całego serca, córko Jerozolimy!
15 Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
PAN oddalił twoje sądy, usunął twojego wroga. Król Izraela, PAN, [jest] pośród ciebie. Nie będziesz już oglądał zła.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
W tym dniu powiedzą do Jerozolimy: Nie bój się! [A do] Syjonu: Niech nie mdleją twoje ręce!
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
PAN, twój Bóg, pośród ciebie jest potężny; on [cię] zbawi i rozraduje się wielce nad tobą; będzie się cieszyć ze swojej miłości [wobec ciebie] i rozweseli się nad tobą ze śpiewaniem, [mówiąc]:
18 “Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
Zbiorę tęskniących za uroczystym zgromadzeniem, [bo] wśród ciebie są [też smutni z powodu] brzemienia zniewagi włożonego na ciebie.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
Oto w tym czasie uczynię kres wszystkim, którzy cię trapią, a zbawię chromą i zgromadzę wygnaną; okryję ich chwałą i imieniem w całej ziemi, w której doznawali hańby.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.
W tym czasie przyprowadzę was, w tym czasie, mówię, zgromadzę was. Dam wam bowiem imię i chwałę pośród wszystkich narodów ziemi, gdy na waszych oczach odwrócę waszą niewolę – mówi PAN.

< Zefaniya 3 >