< Zefaniya 3 >
1 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
Ve den gjenstridige og urene, staden som er full av vold!
2 Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
Den hører ikke på nogens røst, tar ikke mot tukt; til Herren setter den ikke sin lit, til sin Gud holder den sig ikke nær.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Høvdingene i den er brølende løver, dens dommere er som ulver om aftenen; de gjemmer ikke noget til om morgenen;
4 Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
dens profeter er storskrytere, troløse menn; dens prester vanhelliger det som er hellig, de gjør vold på loven.
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
Herren råder der med rettferd, han gjør ikke urett; hver morgen lar han sin dom komme for lyset, det slår ikke feil. Men den urettferdige kjenner ikke til skam.
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
Jeg har utryddet hedningefolk, deres murtinder er ødelagt; jeg har gjort deres gater øde, så ingen går gjennem dem; deres byer er herjet, så det ikke finnes folk, ikke bor nogen der.
7 Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
Jeg sa: Bare du vil frykte mig, ta mot tukt; da skal din bolig ikke bli utryddet, ikke noget skje av det jeg har besluttet mot dig. Men de har tvert imot lagt vinn på å forderve alle sine gjerninger.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
Derfor, bi på mig, sier Herren, på den dag jeg reiser mig for å ta hærfang! For min dom er at jeg samler hedningefolk, sanker riker sammen, utøser min harme over dem, all min brennende vrede; for ved min nidkjærhets ild skal hele jorden bli fortært.
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
For da vil jeg gi folkene nye, rene leber, så de alle påkaller Herrens navn og tjener ham med ett sinn.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
Fra landet bortenfor Etiopias elver skal de føre mine tilbedere, mitt spredte folk, som offergave til mig.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
På den dag skal du ikke mere skamme dig over alle de gjerninger hvormed du forbrøt dig mot mig; for da vil jeg rydde bort hos dig dem som jubler så stolt i din midte, og du skal ikke mere ophøie dig selv på mitt hellige berg.
12 Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
Men jeg vil levne hos dig et bøiet og ringe folk, og de skal ta sin tilflukt til Herrens navn.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
Israels rest skal ikke gjøre urett; de skal ikke tale løgn, og det skal ikke finnes en svikefull tunge i deres munn; for de skal finne føde og leve i ro, og ingen skal forferde dem.
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Fryd dig storlig, Sions datter! Rop høit, Israel! Gled dig og fryd dig av fullt hjerte, Jerusalems datter!
15 Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
Herren har tatt bort dine straffedommer, han har ryddet bort din fiende; Israels konge, Herren, er i din midte, du skal ikke mere se noget ondt.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
På den dag skal det sies til Jerusalem: Frykt ikke! Sion, la ikke dine hender synke!
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
Herren din Gud er i din midte, en kjempe som frelser; han fryder sig over dig med glede, han tier i sin kjærlighet, han jubler over dig med fryderop.
18 “Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
Dem som sørger for høitidens skyld, samler jeg - de er fra dig, vanære tynger på dem.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
Se, jeg skal på den tid ha med alle dem å gjøre som har plaget dig, og jeg vil frelse det haltende og sanke det bortdrevne, og jeg vil gjøre dem til pris og til ry over hele jorden, hvor de er blitt så vanæret.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.
På den tid vil jeg føre eder hit, på den tid vil jeg sanke eder; for jeg vil gjøre eder til ry og til pris blandt alle jordens folk, når jeg gjør ende på eders fangenskap for eders øine, sier Herren.