< Zefaniya 3 >
1 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
Asi pay ti managsukir a siudad! Natulawanen ti naranggas a siudad!
2 Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
Saan daytoy a dimngeg iti timek ti Dios, wenno saan nga immawat iti pannursuro manipud kenni Yahweh! Saan isuna nga agtalek kenni Yahweh ken saan nga umasideg iti Diosna.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Dagiti prinsipena ket kasla ngumerngernger a leon iti nagtengngaanna! Dagiti ukomna ket kasla kadagiti lobo iti rabii a saan a mangitedda iti kanenda iti agsapa!
4 Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
Dagiti profetana ket nadursok ken manangliput a lallaki! Rinugitan dagiti padina ti nasantoan ken nagaramid iti panaglabsing iti linteg!
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
Nalinteg ni Yahweh iti nagtengngaanna! Dinto agaramid iti biddut! Iti tunggal bigat, ipaayna ti husticia! Saanto nga mailemmeng iti lawag, ngem ti managdakdakes ket dina ammo ti agbain!
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
“Dinadaelko dagiti nasion; nadadael dagiti sarikedkedda. Dinadaelko dagiti kalsadada tapno awan a pulos iti makalabas kadagitoy. Nadadael dagiti siudadda ket awan ti tao a makapagnaed kadagitoy.
7 Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
Kinunak, ‘Sigurado nga agbutengkanto kaniak! Umawatka iti pannakaisuro ket saanka a mapapanaw kadagiti pagtaengam iti amin a pinanggepko nga aramiden kenka!' Ngem aggagarda a mangirugi iti tunggal agsapa babaen iti panangpadakesda kadagiti amin nga aramidda.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
Ngarud, urayendak”—kastoy ti pakaammo ni Yahweh— “agingga iti aldaw a tumakderak nga agsamsam! Ta ti pangngedengko ket urnongek dagiti nasion, ummongek dagiti pagarian, ken tapno idissuorko kadakuada ti ungetko, ti narungsot a pungtotko, tapno maikisap amin ti daga babaen iti apuy ti ungetko.
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
Ngem urayno kasta, ikkakto iti nadalus a pagsasao dagiti tattao, tapno umawagda amin iti nagan ni Yahweh, tapno agserbida kaniak nga addaan iti panagkaykaysa.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
Manipud iti labes ti karayan ti Etiopia a mangidaydayaw kaniak—dagiti naiwara-wara a tattaok—mangyegto kadagiti daton a para kaniak.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
Iti dayta nga aldaw, saankayonto a maibabain gapu kadagiti amin nga aramidyo a maibusor kaniak, agsipud ta iti dayta a tiempo, ikkatekto kadakayo dagiti nangramrambak iti kinatangsityo, ken gapu ta saankayontno nga agtignay a sipapalangguad iti tapaw ti nasantoan a bantayko.
12 Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
Ngem ibatikayo a kas nanumo ken napanglaw a tattao, ket agkamangkayonto iti nagan ni Yahweh.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
Saanton nga aglabsing wenno agulbod dagiti nabatbati iti Israel, ken awan ti manangallilaw a dila iti masarakanto kadagiti ngiwatda; isu nga agarab ken agiddada, ken awanto iti pagbutbutnganda.”
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Agkantaka, O anak a babbai ti Sion! Agdir-ika, O Israel! Agrag-o ken agragsakka iti amin a pusom, O anak a babai ti Jerusalem!
15 Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
Inikkaten ni Yahweh ti dusam; pinapanawnan dagiti kabusormo! Ni Yahweh ti ari ti Israel nga adda kadagiti nagtengngaanyo. Saanmonto manen a kabuteng ti dakes!
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
Iti dayta nga aldaw, kunaendanto iti Jerusalem, “Saanka nga agbuteng, O Sion. Saanmo nga itulok a kumapuy dagiti imam.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
Ni Yahweh a Diosyo ket adda kadakayo, ti mannakabalin a mangisalakan kadakayo. Agrambakto isuna gapu kadakayo ken paginanaennakayonto iti ayatna nga addaan rag-o; Maragsakanto isuna kadakayo ket agpukkawto isuna iti rag-o.
18 “Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
Dagiti nagladingit gapu iti naituding a fiesta—inummongko ida manipud kadakayo, nagbalinda a dadagsen ken nakaigapuan ti pannakaibabainyo.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
Adtoy, iti dayta a tiempo, dusaekto dagiti amin a nangparparigat kadakayo. Ispalekto dagiti pilay ken ummongekto dagiti napatalaw. Ikkatekto ti nakaibabainanda ket pagbalinekto ida a nadayaw ken natan-ok iti entero a daga.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.
Iti dayta a tiempo, idauloan ken pagmaymaysaenkayonto. Raemen ken idayawdakayonto dagiti amin a nasion iti daga, inton makitayo nga insublik ti kinarang-ayyo,” kuna ni Yahweh.