< Zefaniya 3 >
1 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
Ô ville insigne et mise à rançon, malheur à toi! La colombe
2 Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
n'a pas entendu Ma voix ni recueilli l'avertissement; elle n'a point eu foi au Seigneur, et ne s'est point approchée de son Dieu.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Ses princes sont, au milieu d'elle, comme des lions rugissants, et ses juges comme des loups d'Arabie; et ils n'ont pas subsisté jusqu'à l'aurore.
4 Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
Ses prophètes, hommes méprisants, sont inspirés par le mauvais esprit; ses prêtres profanent les choses saintes, et ne respectent point la loi.
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
Mais le Seigneur juste est au milieu d'elles, et Il ne fera rien d'inique; demain Il produira Son jugement à la lumière: car Dieu ne Se cache point; Il ne connaît l'iniquité ni par exaction ni par violence.
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
J'ai attiré les superbes dans la ruine; leurs tours sont en poussière; Je ferai leurs rues si désertes, que nul n'y passera; leurs villes ont dépéri, parce qu'il n'y a plus personne qui vive et demeure en elles.
7 Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
J'ai dit: Craignez-Moi, recueillez Mon enseignement, et vous ne serez pas exterminés de la face de la terre, partout où Je me suis vengé d'elle; tiens- toi prêt, lève-toi et fuis dès l'aurore, car tous leurs raisins sont gâtés.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
Attends-Moi, dit le Seigneur; jusqu'au jour de Ma résurrection, où Je rendrai témoignage; car Mon jugement s'exercera dans l'assemblée des nations pour y recevoir les rois et répandre sur eux toute ma colère, parce que dans le feu de Mon zèle toute la terre périra.
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
Alors Je rendrai aux peuples une langue comme à l'origine, afin que tous invoquent le Nom du Seigneur, et le servent sous un joug unique.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
Depuis les sources des fleuves de l'Éthiopie, J'accueillerai les gentils avec ceux de Mon peuple qui sont dispersés, et ils M'offriront leurs sacrifices.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
En ce jour, tu n'auras plus à rougir des œuvres où tu as prévariqué contre Moi; car alors Je t'aurai ôté de ton orgueil dédaigneux, et tu ne continueras plus de te glorifier sur la montagne de Mon sanctuaire.
12 Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
Et Je trouverai en toi un peuple rempli d'humilité et de douceur; et ils auront en vénération le Nom du Seigneur,
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
ceux qui resteront encore d'Israël; et ils ne feront plus d'iniquité; et ils ne parleront plus de vanités, et, dans leur bouche, la langue ne sera plus trouvée trompeuse; et Mon troupeau pourra paître et se reposer sans être effrayé de personne.
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Réjouis-toi, Sion, Ma fille; proclame ton allégresse, Jérusalem, Ma fille; tressaille et réjouis-toi de tout ton cœur, Jérusalem, Ma fille.
15 Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
Le Seigneur t'a remis tes iniquités; Il t'a racheté des mains de tes ennemis; le roi d'Israël, qui est le Seigneur, est au milieu de toi: tu ne verras plus de malheurs.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
En ce temps-là, le Seigneur dira à Jérusalem: Rassure-toi, Sion, que tes mains ne soient pas défaillantes.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
Le Seigneur ton Dieu est avec toi; le Tout-Puissant te sauvera: Il te rendra la joie; Il te rajeunira de Son amour; en toi Il sera ravi de joie, comme en un jour de fête.
18 “Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
Et Je rassemblerai tes affligés; malheur à qui l'a outragée!
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
Voilà que J'agirai en toi, pour l'amour de toi, en ce temps-là, dit le Seigneur; et je sauverai celle qui a été opprimée, et je recueillerai celle qui a été répudiée, et je glorifierai ses fils, et ils auront un nom par toute la terre.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.
En ce temps-là vos ennemis seront confondus lorsque J'en userai ainsi avec vous, et que Je vous aurai bien accueillis; car Je vous donnerai un nom célèbre, et vous serez glorifiés par tous les peuples de la terre, après que Je vous aurai ramené tous vos captifs, dit le Seigneur.