< Zefaniya 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
Malheur à celle qui est rebelle et souillée, à la ville oppressive!
2 Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
Elle n'a pas obéi à la voix. Elle n'a pas reçu de correction. Elle ne s'est pas confiée à Yahvé. Elle ne s'est pas approchée de son Dieu.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Ses princes sont des lions rugissants. Ses juges sont des loups du soir. Ils ne laissent rien au lendemain.
4 Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
Ses prophètes sont des gens arrogants et perfides. Ses prêtres ont profané le sanctuaire. Ils ont fait violence à la loi.
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
Yahvé, en elle, est juste. Il ne fait pas de mal. Chaque matin, il fait éclater sa justice. Il ne faillit pas, mais les injustes ne connaissent pas la honte.
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
J'ai exterminé des nations. Leurs remparts sont désolés. J'ai rendu leurs rues désertes, pour que personne n'y passe. Leurs villes sont détruites, il n'y a plus d'homme, il n'y a plus d'habitant.
7 Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
J'ai dit: « Crains-moi seulement. Recevez la correction », afin que sa demeure ne soit pas anéantie, selon tout ce que j'ai prévu à son sujet. Mais ils se sont levés de bonne heure et ont corrompu toutes leurs actions.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
« Attendez-moi donc », dit Yahvé, « jusqu'au jour où je me lèverai sur la proie, car ma résolution est de rassembler les nations, d'assembler les royaumes pour répandre sur eux ma fureur, toute mon ardente colère, car toute la terre sera dévorée par le feu de ma jalousie ».
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
Car alors je purifierai les lèvres des peuples, afin qu'ils invoquent tous le nom de Yahvé, pour le servir épaule contre épaule.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
De l'autre côté des fleuves de Cusch, mes adorateurs, les filles de mon peuple dispersé, apporteront mon offrande.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
En ce jour-là, vous ne serez pas déçus pour toutes les actions que vous avez commises contre moi; car alors j'ôterai du milieu de vous vos orgueilleux, et vous ne serez plus arrogants sur ma montagne sainte.
12 Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
Mais je laisserai parmi vous un peuple affligé et pauvre, et il se réfugiera dans le nom de l'Éternel.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
Le reste d'Israël ne commettra pas d'iniquité, ne dira pas de mensonges, et il ne se trouvera pas de langue mensongère dans leur bouche; ils paîtront et se coucheront, et personne ne leur fera peur. »
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Chante, fille de Sion! Crie, Israël! Sois dans l'allégresse et réjouis-toi de tout ton cœur, fille de Jérusalem!
15 Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
L'Éternel a ôté tes jugements, Il a chassé ton ennemi. Il a chassé ton ennemi. Le roi d'Israël, Yahvé, est au milieu de toi. Tu ne craindras plus le mal.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
En ce jour-là, on dira à Jérusalem: « Ne crains pas, Sion. Ne laisse pas tes mains s'affaiblir. »
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
Yahvé, ton Dieu, est au milieu de toi, un puissant qui sauve. Il se réjouira de toi dans l'allégresse. Il te calmera dans son amour. Il se réjouira de toi en chantant.
18 “Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
J'éloignerai de toi ceux qui s'affligent au sujet des fêtes fixées. Ils sont pour toi un fardeau et un opprobre.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
Voici, en ce temps-là, je m'occuperai de tous ceux qui t'affligent, je sauverai les boiteux et je rassemblerai ceux qui ont été chassés. Je leur donnerai la louange et l'honneur, eux dont la honte a été dans toute la terre.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.
En ce temps-là, je vous ferai entrer, et en ce temps-là, je vous rassemblerai, car je vous rendrai honneur et louange parmi tous les peuples de la terre, quand je rétablirai votre fortune sous vos yeux, dit l'Éternel.

< Zefaniya 3 >