< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
RAB, Yahuda Kralı Amon oğlu Yoşiya zamanında Hizkiya oğlu Amarya oğlu Gedalya oğlu Kuşi oğlu Sefanya'ya şöyle seslendi:
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
“Yeryüzünden her şeyi silip süpüreceğim.
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
İnsanları, hayvanları, Gökteki kuşları, Denizdeki balıkları, Kötüleri ve onların günah tuzaklarını silip süpüreceğim. Yok edeceğim insanı yeryüzünden.” İşte böyle diyor RAB.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
“Elimi Yahuda ve Yeruşalim'de yaşayanlara karşı uzatacağım. Baal'dan kalan izleri, Putperest din adamlarıyla kâhinlerin adını, Damlardan gök cisimlerine tapınanları, Hem benim adıma, hem de Molek putu adına ant içip tapınanları, Yolumdan dönenleri, Bana yönelmeyenleri, Kılavuzluğumu istemeyenleri buradan yok edeceğim.”
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Susun Egemen RAB'bin önünde, Çünkü O'nun günü yaklaştı. RAB bir kurban hazırladı, Konuklarını çağırdı.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
“O kurban günü” diyor RAB, “Önderleri, kral oğullarını, Yabancıların geleneklerine uyanları Cezalandıracağım.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
İlahların tapınaklarını zorbalık ve hileyle dolduran putperestleri O gün cezalandıracağım.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
Diyorum ki, o gün kentin Balık Kapısı'ndan çığlıklar, İkinci Mahalle'den feryatlar Ve tepelerden büyük çatırtılar yükselecek.” İşte böyle diyor RAB.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
“Kentin aşağı mahallesinde oturanlar, feryat edin. Bütün tüccarlarınız yok olacak, Gümüş ticareti yapanların hepsi mahvolacak.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
O gün kandille arayacağım Yeruşalim'in her yanını, İçlerinden, ‘RAB bir şey yapmaz, Ne iyilik eder ne kötülük’ Diyen o rahatına düşkün aymazları cezalandıracağım.
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
Servetleri yağmalanacak. Viraneye dönecek evleri. Yaptıkları evlerde oturamayacak, Diktikleri bağların şarabını içemeyecekler.”
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
RAB'bin büyük günü yaklaştı, Yaklaştı ve çabucak geliyor. Dinleyin, RAB'bin gününde En yiğit asker bile acı acı feryat edecek.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
Öfke günü o gün! Acı ve sıkıntı, Yıkım ve felaket, Zifiri karanlık bir gün olacak, Bulutlu, koyu karanlık bir gün.
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
Surlu kentlere, köşelerdeki yüksek kulelere karşı Savaş borularının çalındığı, Savaş naralarının atıldığı gündür.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
RAB diyor ki, “İnsanları öyle bir felakete uğratacağım ki, Körler gibi, nereye gittiklerini göremeyecekler. Çünkü bana karşı günah işlediler. Su gibi akacak kanları, Bedenleri yerde çürüyecek.”
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
RAB'bin öfke gününde, Altınları da gümüşleri de Onları kurtaramayacak. RAB'bin kıskançlık ateşi bütün ülkeyi yakıp yok edecek. RAB ülkede yaşayanların hepsini korkunç bir sona uğratacak.

< Zefaniya 1 >