< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
The word of Jehovah, which came to Zephaniah, the son of Cushi, the son of Gedaliah, the son of Amariah, the son of Hizkiah, in the days of Josiah, the son of Amon, king of Judah.
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
I will utterly consume all things from the face of the land, saith Jehovah;
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
I will consume man and beast; I will consume the birds of heaven, and the fishes of the sea, And the stumbling-blocks with the wicked; And I will cut off man from the face of the land, saith Jehovah.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
I will stretch out my hand over Judah, And over all the inhabitants of Jerusalem, And I will cut off from this place the residue of Baal, The name of the idol-sacrificers with the priests,
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
And those who bow themselves on the house-tops to the host of heaven, And those who bow themselves and swear by Jehovah, And also swear by their idol,
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
And those that turn back from Jehovah, And those that seek not Jehovah, nor inquire for him.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Be silent before the Lord Jehovah! For the day of Jehovah is near; For Jehovah hath prepared a sacrifice; He hath appointed his guests.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
And in the day of the sacrifice of Jehovah it shall come to pass That I will punish the princes and the sons of the king, And all that are clothed with foreign apparel.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
In that day also will I punish all that leap over the threshold, That fill the houses of their master with violence and deceit.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
And it shall come to pass in that day, saith Jehovah, That there shall be the noise of a cry from the fish-gate, And of a howling from the other part of the city, And of great destruction from the hills.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
Howl, ye inhabitants of Maktesh! For all the trafficking people are cut down; All they that bear silver are destroyed.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
And it shall come to pass at that time, That I will search Jerusalem with lamps, And I will punish the men that are settled on their lees; That say in their hearts, “Jehovah doeth neither good nor evil.”
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
Their substance shall become a spoil, And their houses a desolation; They shall also build houses, but not inhabit them; And shall plant vineyards, but not drink the wine thereof.
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
The day of Jehovah is near, the great day; It is near, and hasteth greatly; The day of Jehovah shall resound; Bitterly shall the mighty man cry for help.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
That day is a day of wrath, A day of distress and anguish, A day of destruction and desolation, A day of darkness and gloominess, A day of clouds and thick darkness,
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
A day of the trumpet and the war-shout, Against the fenced cities, And against the high towers.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
And I will distress the men, so that they shall walk like the blind, Because they have sinned against Jehovah. And their blood shall be poured out as dust, And their flesh as dung.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Neither their silver nor their gold shall be able to deliver them in the day of the wrath of Jehovah, But by the fire of his indignation shall the whole land be devoured; For destruction, and that a speedy one, will he bring Upon all that dwell in the land.

< Zefaniya 1 >