< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
The word of the Lord that came to Zephaniah the son of Cushi, the son of Gedaliah, the son of Amariah, the son of Hezekiah, in the days of Josiah the son of Amon, king of Judah.
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
While gathering, I will gather together all things from the face of the earth, says the Lord.
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
I will gather man and cattle; I will gather the flying things of the air and the fish of the sea. And the impious will be a catastrophe. And I will disperse men before the face of the earth, says the Lord.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
And I will extend my hand over Judah and over all the inhabitants of Jerusalem. And I will disperse from this place the remnant of Baal, and the names of the administrators along with the priests,
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
and those who adore the military campaign over the ceiling of the sky, both those who adore and swear by the Lord, and those who swear by Melchom,
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
both those who turn aside from following after the Lord, and those who have not sought the Lord, nor inquired about him.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Be silent before the face of the Lord God. For the day of the Lord is near; for the Lord has prepared a victim, he has sanctified those he has called.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
And this shall be: in the day of the victim of the Lord, I will visit upon the leaders, and upon the sons of the king, and upon all who have been clothed with strange garments.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
And I will visit upon all who enter arrogantly over the threshold in that day, those who fill the house of the Lord their God with iniquity and deceit.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
And this shall be in that day, says the Lord: the voice of an outcry from the fish gate, and a howling from the Second, and a great contrition from the hills.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
Howl, inhabitants of the Pillar. All the people of Canaan have fallen silent. All were ruined who had been wrapped in silver.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
And this shall be in that time: I will scrutinize Jerusalem with lamps, and I will visit upon the men who have become stuck in the dregs, who say in their hearts, “The Lord will not do good, and he will not do evil.”
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
And their strength will be in plundering, and their houses in the desert. And they will build houses and not dwell in them, and they will plant vineyards and not drink their wine.
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
The great day of the Lord is near; it is near and exceedingly swift. The voice of the day of the Lord is bitter; the strong will be tested there.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
That day is a day of wrath, a day of tribulation and anguish, a day of calamity and misery, a day of darkness and gloom, a day of clouds and whirlwinds,
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
a day of the trumpet and the trumpet blast over fortified cities and over exalted ramparts.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
And I will trouble men, and they will walk like the blind, because they have sinned against the Lord. And their blood will be poured out like soil, and their bodies like manure.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Neither their silver, nor their gold, will be able to free them in the day of the wrath of the Lord. All the land will be devoured in the fire of his zeal, for with all speed, he will bring to consummation every inhabitant of the land.

< Zefaniya 1 >