< Zekariya 1 >

1 Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
I den ottende Måned i Darius's andet Regeringsår kom HERRENs Ord til Profeten Zakarias, en Søn af Berekja, en Søn af Iddo, således:
2 “Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
HERREN var fuld af Harme imod eders Fædre.
3 Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Men sig til dem: Så siger Hærskarers HERRE: Vend om til mig, lyder det fra Hærskarers HERRE, så vil jeg vende om til eder, siger Hærskarers HERRE.
4 Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
Vær ikke som eders Fædre, til hvem de tidligere Profeter talte således: Så siger Hærskarers HERRE: Vend om fra eders onde Veje og onde Gerninger! Men de hørte ikke og ænsede mig ikke, lyder det fra HERREN.
5 Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
Eders Fædre, hvor er de? Og Profeterne, lever de evigt?
6 Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
Men mine Ord og Bud, som jeg overgav mine Tjenere Profeterne, nåede de ikke eders Fædre, så de måtte vende om og sige: "Som Hærskarers HERRE havde sat sig for at gøre imod os for vore Vejes og Gerningers Skyld, således gjorde han."
7 Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
På den fire og tyvende dag i den ellevte Måned, det er Sjebat Måned, i Darius's andet Regeringsår kom HERRENs Ord til Profeten Zakarias, en Søn af Berekja, en Søn af Iddo, således:
8 Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
Jeg skuede i Nat, og se, en Mand på en rød Hest holdt mellem Bjergene ved den dybe Kløft, og bag ham var der røde, mørke, hvide og brogede Heste.
9 Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
Jeg spurgte: "Hvad betyder de, Herre?" Og Engelen, som talte med mig, sagde: "Jeg vil vise dig, hvad de betyder."
10 Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
Så tog Manden, som holdt mellem Bjergene, til Orde og sagde: "Det er dem, HERREN udsender, for at de skal drage Jorden rundt."
11 Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
Og de tog til Orde og sagde til HERRENs Engel, som stod mellem Bjergene: "Vi drog Jorden rundt, og se, hele Jorden er rolig og stille.
12 Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
HERRENs Engel tog da til Orde og sagde: "Hærskarers HERRE! Hvor længe varer det, før du forbarmer dig over Jerusalem og Judas Byer, som du nu har været vred på i halvfjerdsindstyve År?"
13 Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
Og til Svar gav HERREN Engelen, som talte med mig, gode og trøstende Ord.
14 Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
Engelen, som talte med mig, sagde så til mig: Tal og sig: Så siger Hærskarers HERRE: Jeg er fuld af Nidkærhed for Jerusalem og Zion
15 koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
og af Harme mod de trygge Hedninger, fordi de hjalp til at gøre Ulykken stor, da min Vrede kun var lille.
16 “Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Derfor, så siger HERREN: Jeg vender mig til Jerusalem og forbarmer mig over det; mit Hus skal opbygges der, lyder det fra Hærskarers HERRE, og der skal udspændes Målesnor over Jerusalem.
17 “Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
Tal videre: Så siger Hærskarers HERRE: Mine Byer skal atter strømme med Velsignelse, og HERREN vil atter trøste Zion og udvælge Jerusalem.
18 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
Derpå løftede jeg mine Øjne og skuede, og se, der var fire Horn.
19 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
Jeg spurgte Engelen, som talte med mig: "Hvad betyder de?" Han svarede: "Det er de Horn, som har spredt Juda, Israel og Jerusalem."
20 Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
Så lod HERREN mig se fire Smede.
21 Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”
Jeg spurgte: "Hvad kommer de for?" Og han svarede: "Hine er de Horn, som spredte Juda, så det ikke kunde løfte sit Hoved; og nu kommer disse for at hvæsse Økser til at slå Hornene til Jorden på de Hedninger, som løftede deres Horn mod Judas Land for at sprede det."

< Zekariya 1 >