< Zekariya 1 >

1 Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
I den ottende Maaned, i Darius's andet Aar, kom Herrens Ord til Profeten Sakarias, en Søn af Berekias, en Sønnesøn af Iddo, saaledes:
2 “Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
Herren har været højlig fortørnet paa eders Fædre.
3 Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Og du skal sige til dem: Saa siger den Herre Zebaoth: Vender om til mig, siger den Herre Zebaoth, saa vil jeg vende om til eder, siger den Herre Zebaoth.
4 Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
Værer ikke som eders Fædre, til hvilke de forrige Profeter raabte og sagde: Saa siger den Herre Zebaoth: Vender dog om fra eders onde Veje og eders onde Idrætter; men de hørte ikke og gave ikke Agt paa mig, siger Herren.
5 Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
Eders Fædre, hvor ere de? og Profeterne, mon de leve til evig Tid?
6 Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
Dog, mine Ord og mine Bestemmelser, som jeg meddelte mine Tjenere, Profeterne, have de ikke rammet eders Fædre, saa de vendte om og sagde: Ligesom den Herre Zebaoth havde tænkt at gøre imod os efter vore Veje og efter vore Idrætter, saaledes har han gjort imod os.
7 Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
Paa den fire og tyvende Dag i den ellevte Maaned, det er Maaneden Sebat, i Darius's andet Aar, kom Herrens Ord til Profeten Sakarias, Berekias's Søn, Iddos Sønnesøn, saaledes:
8 Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
Jeg saa om Natten, og se, en Mand, der red paa en rød Hest, og han holdt stille imellem Myrtetræerne, som vare i Dalen, og bag ham var der røde, graa og hvide Heste.
9 Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
Og jeg sagde: Hvad betyde disse, min Herre? Og Engelen, som talte med mig, sagde til mig: Jeg vil lade dig se, hvad disse betyde.
10 Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
Og den Mand, som holdt stille imellem Myrtetræerne, svarede og sagde: Det er dem, som Herren har sendt til at vandre Jorden rundt.
11 Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
Og de svarede Herrens Engel, som stod imellem Myrtetræerne, og sagde: Vi have vandret Jorden rundt, og se, hele Jorden nyder Ro og Hvile.
12 Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
Da svarede Herrens Engel og sagde: Herre Zebaoth! hvor længe varer det, inden du vil forbarme dig over Jerusalem og over Judas Stæder, paa hvilke du har været vred nu i halvfjerdsindstyve Aar?
13 Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
Og Herren svarede Engelen, som talte med mig, med gode Ord, med trøstende Ord.
14 Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
Og Engelen, som talte med mig, sagde til mig: Raab og sig: Saa siger den Herre Zebaoth: Jeg har været nidkær for Jerusalem og for Zion med en stor Nidkærhed.
15 koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
Men med en stor Fortørnelse er jeg fortørnet paa Hedningerne, som ere saa trygge; thi da jeg en liden Stund havde været fortørnet, saa hjalp de til Ulykken.
16 “Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Derfor, saa siger Herren, har jeg atter vendt mig til Jerusalem med Barmhjertighed, mit Hus skal bygges derudi, siger den Herre Zebaoth, og Maalesnoren skal udstrækkes over Jerusalem.
17 “Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
Raab fremdeles, og sig: Saa siger den Herre Zebaoth: Mine Stæder skulle endnu strømme over af gode Ting, og Herren skal endnu trøste Zion og endnu udvælge Jerusalem.
18 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
Og jeg opløftede mine Øjne og saa, og se, fire Horn!
19 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
Og jeg sagde til Engelen, som talte med mig: Hvad betyde disse? og han sagde til mig: Disse ere de Horn, som adspredte Juda, Israel og Jerusalem.
20 Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
Da lod Herren mig se fire Smede.
21 Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”
Og jeg sagde: Hvad komme disse for at gøre? og han sagde: Hine ere de Horn, som adspredte Juda paa den Maade, at ingen opløftede sit Hoved; men saa kom disse for at forfærde dem, for at nedslaa de Hedningers Horn, som rejste Horn imod Judas Land, for at adsprede det.

< Zekariya 1 >