< Zekariya 1 >

1 Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
Měsíce osmého, léta druhého Dariova, stalo se slovo Hospodinovo k Zachariášovi synu Barachiáše, syna Iddova, proroku, řkoucí:
2 “Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
Rozhněval se Hospodin na otce vaše velice.
3 Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Protož rci těmto: Takto praví Hospodin zástupů: Navraťte se ke mně, praví Hospodin zástupů, a navrátím se k vám, praví Hospodin zástupů.
4 Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
Nebuďte jako otcové vaši, na něž volávali proroci onino předešlí, říkajíce: Takto praví Hospodin zástupů: Navraťte se nyní od cest svých zlých, i od skutků vašich zlých, ale neuposlechli, ani pozorovali mne, praví Hospodin.
5 Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
Otcové vaši kde jsou? A proroci ti zdali na věky živi jsou?
6 Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
Ale však slova má a soudové moji, kteréž jsem přikázal služebníkům svým prorokům, zdali nepostihli otců vašich? tak že obrátivše se, řekli: Jakž uložil Hospodin zástupů učiniti nám podlé cest našich, a podlé skutků našich, tak učinil nám.
7 Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
Dne čtyřmecítmého, jedenáctého měsíce, kterýž jest měsíc Šebat, léta druhého Dariova, stalo se slovo Hospodinovo k Zachariášovi synu Barachiáše, syna Iddova, proroku, řkoucí:
8 Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
Viděl jsem v noci, a aj, muž sedí na koni ryzím, kterýž stál mezi myrtovím, kteréž bylo v dolině, za ním pak koně ryzí, strakaté a bílé.
9 Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
I řekl jsem: Kdo jsou tito, Pane můj? Řekl mi anděl ten, kterýž mluvil se mnou: Já ukáži tobě, kdo jsou tito.
10 Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
Tedy odpovídaje muž ten, kterýž stál mezi myrtovím, řekl: Tito jsou, kteréž poslal Hospodin, aby zchodili zemi.
11 Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
I odpověděli andělu Hospodinovu tomu, kterýž stál mezi myrtovím, a řekli: Zchodili jsme zemi, a aj, všecka země bezpečně bydlí, a pokoje užívá.
12 Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
Tedy odpověděl anděl Hospodinův a řekl: Ó Hospodine zástupů, až dokudž ty se nesmiluješ nad Jeruzalémem a nad městy Judskými, na kteréž jsi hněval se již sedmdesáte let?
13 Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
I odpověděl Hospodin andělu tomu, kterýž mluvil se mnou, slovy dobrými, slovy potěšitelnými.
14 Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
Tedy řekl mi anděl, kterýž mluvil ke mně: Volej a rci: Takto praví Hospodin zástupů: Horlím pro Jeruzalém a Sion horlením velikým.
15 koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
A hněvám se náramně na ty národy, kteříž mají pokoj; nebo když jsem já se málo rozhněval, oni pomáhali k zlému.
16 “Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Protož takto praví Hospodin: Navrátil jsem se k Jeruzalému milosrdenstvím, dům můj staven bude v něm, praví Hospodin zástupů, a pravidlo vztaženo bude na Jeruzalém.
17 “Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
Ještě volej a rci: Takto praví Hospodin zástupů: Ještěť se rozsadí města má pro hojnost dobrého; neboť utěší ještě Hospodin Sion, a vyvolí ještě Jeruzalém.
18 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
Tedy pozdvihl jsem očí svých, a uzřel jsem, a aj, čtyři rohové.
19 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
I řekl jsem andělu, kterýž mluvil se mnou: Co jest toto? I řekl mi: To jsou ti rohové, kteříž zmítali Judou, Izraelem a Jeruzalémem.
20 Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
Ukázal mi také Hospodin čtyři kováře.
21 Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”
I řekl jsem: Co jdou dělati tito? I mluvil, řka: Tito jsou rohové, kteříž zmítali Judou, tak že žádný nemohl pozdvihnouti hlavy své. Protož přišli tito, aby je přestrašili, a srazili rohy těch národů, kteříž pozdvihli rohu proti zemi Judské, aby ní zmítali.

< Zekariya 1 >